< Yeremia 29 >

1 Aku menulis surat kepada imam-imam, nabi-nabi, pemimpin-pemimpin bangsa yang masih hidup, dan kepada semua orang lain yang telah diangkut dari Yerusalem ke Babel oleh Nebukadnezar.
Yeremiya anatumiza kalata kuchokera ku Yerusalemu kupita kwa akuluakulu amene anali ku ukapolo, ndiponso kwa ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse amene Nebukadinezara anawatenga ku Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
2 Surat itu kutulis setelah Raja Yoyakhin, ibunya, pegawai-pegawai istana, pejabat-pejabat pemerintahan Yehuda dan Yerusalem, para pengrajin, dan para pekerja ahli diangkut ke pembuangan.
Zimenezi zinachitika mfumu Yekoniya, amayi a mfumu, nduna za mfumu ndiponso atsogoleri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, anthu aluso ndi amisiri atatengedwa ku Yerusalemu kupita ku ukapolo.
3 Aku menitipkan surat itu kepada Elasa anak Safan, dan Gemarya anak Hilkia yang diutus Zedekia raja Yehuda kepada Nebukadnezar raja Babel. Surat itu berbunyi,
Yeremiya anapatsira kalatayo Eleasa mwana wa Safani ndi Gemariya mwana wa Hilikiya, amene Zedekiya mfumu ya Yuda anawatumiza kwa Mfumu Nebukadinezara ku Babuloni. Mʼkalatamo analembamo kuti:
4 "Beginilah kata TUHAN Yang Mahakuasa, Allah Israel kepada semua orang yang telah dibuangnya dari Yerusalem ke Babel:
Anthu onse amene anatengedwa ukapolo kuchokera ku Yerusalemu kupita ku Babuloni, Yehova akuwawuza kuti,
5 'Menetaplah di situ. Bangunlah rumah-rumahmu. Bukalah ladang dan nikmatilah hasilnya.
“Mangani nyumba ndipo muzikhalamo. Limani minda ndipo mudye zipatso zake.
6 Kawinlah supaya kamu mendapat anak, dan biarlah anak-anakmu juga kawin supaya mereka pun mendapat anak. Jumlahmu harus bertambah dan tidak boleh berkurang.
Kwatirani ndipo mubereke ana aamuna ndi aakazi. Ana anu aamuna muwasankhire akazi ndipo muwasankhire amuna ana anu aakaziwo, kuti nawonso abale ana aamuna ndi aakazi. Muchulukane kumeneko. Chiwerengero chanu chisachepe.
7 Bekerjalah untuk kesejahteraan kota-kota tempat kamu Kubuang. Berdoalah kepada-Ku untuk kepentingan kota-kota itu, sebab kalau kota-kota itu makmur, kamu pun akan makmur.
Ndiponso muzifunafuna mtendere ndi ubwino wa mzinda umene ndinakupirikitsirani ku ukapoloko. Muzipempherera mzindawo kwa Yehova, kuti zikuyendereni bwino.”
8 Aku TUHAN, Yang Mahakuasa, Allah Israel, memperingatkan kamu supaya jangan membiarkan dirimu ditipu oleh nabi-nabi yang tinggal di tengah-tengahmu atau oleh siapapun juga yang berkata bahwa mereka dapat meramalkan masa depan. Jangan memperhatikan mimpi-mimpi mereka.
Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, “Musalole kuti aneneri ndi owombeza amene ali pakati panu akunyengeni. Musamvere maloto awo.
9 Mereka memakai nama-Ku untuk menceritakan kepadamu hal-hal yang tidak benar. Aku tidak menyuruh mereka. Aku, TUHAN, telah berbicara.'
Iwo akunenera zabodza kwa inu mʼdzina langa ngakhale Ine sindinawatume,” akutero Yehova.
10 TUHAN berkata, 'Apabila telah genap masa tujuh puluh tahun bagi Babel, Aku akan memperhatikan kamu lagi, dan menepati janji-Ku untuk membawa kamu kembali ke tempat ini.
Yehova akuti, “Zaka 70 za ku Babuloni zikadzatha, ndidzabwera kudzakuchitirani zabwino zonse zimene ndinakulonjezani zija, ndipo ndidzakubwezerani ku malo ano.
11 Bukankah Aku sendiri tahu rencana-rencana-Ku bagi kamu? Rencana-rencana itu bukan untuk mencelakakan kamu, tetapi untuk kesejahteraanmu dan untuk memberikan kepadamu masa depan yang penuh harapan.
Pakuti Ine ndikudziwa zimene ndinakukonzerani,” akutero Yehova, “ndimalingalira zabwino zokhazokha za inu osati zoyipa, ayi. Ndimalingalira zinthu zokupatsani chiyembekezo chenicheni pa za mʼtsogolo.
12 Maka kamu akan minta tolong kepada-Ku. Kamu akan datang untuk berdoa kepada-Ku, dan Aku akan menjawab doamu.
Nthawi imeneyo mudzandiyitana, ndi kunditama mopemba ndipo ndidzakumverani.
13 Kamu akan mencari Aku dan menemukan Aku, sebab kamu mencari dengan sepenuh hati.
Mudzandifunafuna ndipo mudzandipeza. Mukadzandifuna ndi mtima wanu wonse
14 Sungguh, kamu akan menemukan Aku. Kamu akan Kukumpulkan dari tengah-tengah setiap bangsa dan dari setiap negeri tempat kamu diceraiberaikan dan dibuang. Kamu akan Kubawa kembali ke negeri asalmu ini serta memulihkan keadaanmu. Aku, TUHAN, telah berbicara.'
mudzandipezadi,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubwezerani zabwino zanu. Ndidzakusonkhanitsani kuchokera ku mayiko onse ndi kumalo konse kumene munali,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubweretsani kumalo kumene munali ndisanakuchotseni kukupititsani ku ukapolo.”
15 Menurut kamu, TUHAN telah memberikan kepadamu nabi-nabi di Babel.
Inu mumati, “Yehova watiwutsira aneneri athu ku Babuloni,”
16 Dengarkan apa yang dikatakan TUHAN tentang raja yang memerintah sekarang ini, yaitu raja keturunan Daud, dan tentang penduduk kota ini, yaitu sanak keluargamu yang tidak diangkut ke pembuangan bersama kamu.
koma zimene Yehova akunena za mfumu imene ikukhala pa mpando waufumu wa Davide pamodzi ndi anthu onse amene anatsala mu mzinda muno, abale anu amene sanapite nanu ku ukapolo ndi izi,
17 TUHAN Yang Mahakuasa berkata, 'Aku akan mendatangkan peperangan, kelaparan, dan wabah penyakit ke atas mereka. Mereka akan Kuperlakukan seperti buah-buah ara yang terlalu busuk sehingga tak dapat dimakan.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawapha ndi nkhondo, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa ngati nkhuyu zowola kwambiri, zosati nʼkudya.
18 Mereka akan Kukejar-kejar dengan peperangan, kelaparan, dan wabah penyakit sehingga segala bangsa di seluruh dunia akan merasa ngeri melihat keadaan mereka. Di mana saja Aku menceraiberaikan mereka, orang akan merasa ngeri dan takut melihat apa yang telah terjadi dengan mereka. Mereka akan diejek, dan nama mereka dipakai sebagai kutukan.
Ndidzawalondola ndi lupanga, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa anthu amayiko onse a pa dziko lapansi. Adzakhala otembereredwa, ochititsa mantha, onyozeka ndiponso ochitidwa chipongwe pakati pa anthu a mitundu yonse kumene ndawapirikitsirako.
19 Semua itu terjadi atas mereka, karena mereka tidak menuruti pesan-Ku yang terus-menerus Kusampaikan kepada mereka melalui para nabi hamba-hamba-Ku. Mereka tidak mau memperhatikan pesan-Ku itu.
Zidzatero chifukwa sanamvere mawu anga amene ndinkawatumizira kudzera mwa atumiki anga, aneneri. Ngakhale inu amene muli ku ukapolo simunamverenso,” akutero Yehova.
20 Dan kamu semua yang telah Kubuang ke Babel, dengarkan apa yang Aku, TUHAN, katakan.'
Choncho, imvani mawu a Yehova, inu akapolo nonse amene ndinakuchotsani mu Yerusalemu ndi kukupititsani ku Babuloni.
21 TUHAN Yang Mahakuasa, Allah Israel, telah berbicara mengenai Ahab putra Kolaya, dan mengenai Zedekia putra Maaseya yang memakai nama TUHAN untuk menyampaikan kepadamu hal-hal yang tidak benar. TUHAN berkata bahwa Ia akan menyerahkan mereka kepada kekuasaan Nebukadnezar raja Babel, yang akan membunuh mereka di depan matamu.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti zokhudza Ahabu mwana wa Kolaya ndi Zedekiya mwana wa Maseya, amene akulosera zabodza kwa inu mʼdzina langa: “Taonani ndidzawapereka kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzawapha inu mukupenya.
22 Maka apabila orang-orang yang telah diangkut dari Yerusalem ke Babel hendak mengutuki seseorang, mereka akan berkata, 'Semoga TUHAN memperlakukan engkau seperti Zedekia dan Ahab, yang telah dibakar hidup-hidup oleh raja Babel.'
Chifukwa cha anthu awiriwo, akapolo onse ochokera ku Yuda amene ali ku Babuloni adzagwiritsa ntchito mawu awa potemberera: ‘Yehova achite nawe monga mmene anachitira ndi Zedekiya ndi Ahabu, amene mfumu ya ku Babuloni inawatentha.’
23 Begitulah nasib mereka karena telah melakukan dosa-dosa besar di Israel: mereka berzinah, dan memakai nama TUHAN untuk menceritakan hal-hal yang tidak benar. Itu bertentangan dengan kemauan TUHAN. Ia tahu apa yang mereka lakukan, dan ia sendiri menjadi saksi melawan mereka. TUHAN telah berbicara."
Pakuti anthu amenewa achita zoyipa kwambiri mu Israeli; achita chigololo ndi akazi a eni ake ndipo mʼdzina langa ankayankhula zabodza zimene sindinawawuze kuti atero. Ine ndikuzidziwa ndipo ndine mboni ya zimenezi,” akutero Yehova.
24 TUHAN Yang Mahakuasa, Allah Israel memberi pesan kepadaku untuk Semaya, orang Nehelam, karena Semaya telah mengirim surat atas namanya sendiri kepada seluruh penduduk Yerusalem, kepada Imam Zefanya anak Maaseya, dan kepada semua imam yang lain. Dalam surat itu Semaya menulis begini kepada Zefanya:
Ukamuwuze Semaya wa ku Nehelamu kuti,
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Iwe unatumiza kalata mʼdzina lako kwa anthu onse a mu Yerusalemu, kwa Zefaniya mwana wa wansembe Maseya, ndi kwa ansembe onse. Unalemba mu kalatayo kuti,
26 "TUHAN telah mengangkat engkau menjadi imam menggantikan Yoyada, dan sekarang engkaulah pejabat tertinggi di Rumah TUHAN. Tugasmu ialah memerintahkan supaya setiap orang gila, yang mengaku dirinya nabi, dibelenggu dengan rantai besi pada lehernya.
‘Yehova wakusankha kukhala wansembe mʼmalo mwa Yehoyada kuti ukhale wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Yehova. Munthu aliyense wamisala amene akudziyesa kuti ndi mneneri uzimuponya mʼndende ndi kumuveka goli lachitsulo.
27 Tetapi mengapa engkau tidak bertindak terhadap Yeremia orang Anatot itu yang telah berlaku sebagai nabi di antara bangsa kita?
Nanga tsono chifukwa chiyani simunamuchitire zimenezi Yeremiya wa ku Anatoti, amene amakhala ngati mneneri pakati panu?
28 Orang itu harus ditutup mulutnya, sebab ia mengatakan kepada orang-orang kita di Babel bahwa mereka masih lama tinggal di sana. Dan karena itu, katanya, mereka harus membangun rumah serta membuka ladang dan menikmati hasilnya."
Yeremiyayo watitumizira uthenga uwu kuno ku Babuloni: Ukapolo wanu ukhala wa nthawi yayitali. Choncho mangani nyumba ndipo muzikhalamo; limani minda ndipo mudye zipatso zake.’”
29 Surat itu dibacakan oleh Imam Zefanya kepadaku.
Koma wansembe Zefaniya anayiwerenga kalatayo pamaso pa mneneri Yeremiya.
30 Sebab itu TUHAN menyuruh aku
Ndipo Yehova anawuza Yeremiya kuti,
31 mengirim berita tentang Semaya kepada semua orang Israel yang dibuang di Babel. Inilah berita itu, "Semaya telah berbicara kepadamu seolah-olah ia nabi; padahal Aku, TUHAN, tidak menyuruh dia. Karena ia telah membuat kamu percaya kepada perkataan dusta,
“Tumiza uthenga uwu kwa akapolo onse: ‘Yehova akuti zokhudza Semaya wa ku Nehelamu: Semaya wakuloserani, ngakhale kuti Ine sindinamutume, ndipo wakunyengani kuti muzikhulupirira bodza.
32 dan karena ia telah menyuruh kamu melawan Aku, maka Aku akan menghukum dia dan keturunannya. Tidak seorang pun dari antara mereka yang akan tinggal di antara kamu untuk melihat hal-hal baik yang akan Kulakukan untuk seluruh umat-Ku. Aku, TUHAN, telah berbicara."
Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti: Mʼbanja lakelo sipadzakhala munthu pakati pa mtundu uno wa anthu amene adzaone zinthu zabwino zimene ndidzachitira anthu anga chifukwa analalika zondiwukira,’” akutero Yehova.

< Yeremia 29 >