< Yeremia 19 >

1 TUHAN menyuruh aku pergi membeli kendi, dan mengajak beberapa pemimpin bangsa serta beberapa imam yang tua-tua,
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukagule mʼphika wadothi kwa munthu wowumba. Utenge akuluakulu ena a anthuwa ndi ansembe
2 untuk pergi bersama-sama mereka ke Lembah Hinom melalui Pintu Gerbang Beling. Di sana aku harus mengumumkan apa yang dipesankan-Nya kepadaku.
ndipo mupite ku Chigwa cha Hinomu chimene chili pafupi ndi pa chipata cha mapale. Pamenepo ukalengeze mawu amene ndikakuwuze.
3 Aku harus berkata begini, "Hai raja-raja Yehuda dan penduduk Yerusalem! Dengarkan apa yang Aku, TUHAN Yang Mahakuasa, Allah Israel, hendak katakan kepadamu. Aku akan mendatangkan malapetaka yang besar ke atas tempat ini sehingga orang yang mendengarnya terkejut.
Ukanene kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu a ku Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu. Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti: Tamverani! Ine ndibweretsa mavuto pa malo pano mwakuti aliyense amene adzamve adzadzidzimuka.
4 Hal itu Kulakukan karena bangsa ini telah meninggalkan Aku. Mereka menajiskan tempat ini dengan mempersembahkan kurban kepada dewa-dewa yang asing bagi mereka, bagi leluhur mereka dan bagi raja-raja Yehuda. Mereka juga telah mengisi tempat ini dengan darah orang-orang yang tak bersalah.
Pakuti anthu andikana Ine ndipo ayipitsa malo ano. Afukiza lubani pa malo ano kwa milungu imene iwo ngakhale makolo awo ngakhalenso mafumu a ku Yuda sanayidziwe. Iwo adzaza malowa ndi magazi a anthu osalakwa.
5 Mereka mendirikan mezbah bagi Baal untuk mempersembahkan anak-anak mereka sebagai kurban bakaran, padahal Aku tak pernah menyuruh mereka melakukan hal itu, bahkan tak pernah hal semacam itu timbul dalam pikiran-Ku.
Amanga nsanja zopembedzerapo Baala, kuperekapo ana awo kuti akhale nsembe zopsereza kwa Baala, chinthu chimene Ine sindinalamule kapena kuchiyankhula, ngakhalenso kuchiganizira.
6 Karena itu, akan tiba waktunya tempat ini tidak lagi disebut Tofet atau Lembah Hinom, melainkan Lembah Pembantaian.
Nʼchifukwa chake taonani, masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzatchulanso malo ano kuti Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma Chophera anthu.
7 Di tempat ini Aku akan menggagalkan semua rencana orang Yehuda dan penduduk Yerusalem. Mereka akan Kubiarkan dikalahkan oleh musuh-musuh mereka dan dibunuh dalam pertempuran. Mayat mereka akan Kubiarkan dimakan burung dan binatang buas.
“‘Pamalo pano ndidzasokoneza maganizo a anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. Ndidzachititsa kuti adani awo awaphe ku nkhondo. Ndidzawakanthitsa kwa anthu amene akuwazonda. Mitembo yawo ndidzayipereka kwa mbalame za mlengalenga ndi zirombo za kutchire kuti ikhale chakudya chawo.
8 Aku akan menimpakan malapetaka yang dahsyat ke atas kota ini sehingga setiap orang yang lewat di situ akan terkejut dan ngeri.
Mzinda uno ndidzawusakaza ndi kuwusandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyansa. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
9 Musuh akan mengepung kota ini, dan berusaha membunuh penduduknya. Pengepungan itu begitu hebat, sehingga orang-orang di dalam kota ini saling memakan temannya, bahkan anak-anak mereka sendiri."
Adani awo adzawuzinga mzindawo kufuna kuwapha motero kuti anthu a mʼkatimo adzafika pomadyana wina ndi mnzake. Adzadya ana awo aamuna ndi ana awo aakazi.’
10 Kemudian TUHAN menyuruh aku memecahkan kendi itu di depan orang-orang yang mengikuti aku.
“Tsono iwe udzaphwanye mtsukowo anthu amene udzapite nawowo akuona,
11 Aku harus mengatakan kepada mereka bahwa TUHAN Yang Mahakuasa berkata begini, "Bangsa dan kota ini akan Kuhancurkan sehingga menjadi seperti kendi yang pecah itu yang tak dapat diperbaiki lagi. Orang akan menguburkan mayat-mayat mereka di Tofet, karena tak ada lagi tempat pekuburan lain.
ndipo ukawawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndidzaphwanya dziko lino ndi mzinda uno ngati momwe wowumba amaphwanyira mbiya yake ndipo sangathe kuyikonzanso. Adzayika anthu akufa ku Tofeti chifukwa padzasowa malo ena owayika.
12 Kota ini dengan penduduknya akan Kujadikan seperti Tofet.
Umu ndi mmene ndidzachitire ndi malo ano pamodzi ndi anthu okhalamo, akutero Yehova. Ndidzasandutsa mzindawu kukhala ngati Tofeti.
13 Semua rumah di Yerusalem dan semua rumah raja-raja Yehuda akan menjadi najis seperti Tofet; karena di atas atap rumah-rumah itu orang telah membakar dupa untuk dewa-dewa langit, dan mempersembahkan anggur untuk dewa-dewa lain."
Nyumba za mu Yerusalemu ndi za mafumu a ku Yuda ndidzazisandutsa ngati za ku Tofeti chifukwa ndi nyumba zimene pa madenga ake ankafukiza lubani kwa zolengedwa zamlengalenga ndi kuthira nsembe zachakumwa kwa milungu ina.’”
14 Lalu aku meninggalkan Tofet, tempat aku disuruh menyampaikan pesan TUHAN. Aku pergi ke pelataran Rumah TUHAN dan berdiri di situ, lalu memberitahukan kepada semua orang,
Kenaka Yeremiya anabwerako ku Tofeti, kumene Yehova anamutuma kuti akanenere, nakayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Yehova ndi kuwawuza anthu kuti,
15 bahwa TUHAN Yang Mahakuasa, Allah Israel, berkata begini, "Karena kamu keras kepala dan tak mau mendengarkan, maka Aku akan mendatangkan ke atas kota ini dan ke atas semua desa di sekitarnya segala bencana yang telah Kurencanakan."
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Tamverani! Ine ndidzabweretsa masautso amene ndinanena aja pa mzinda uno ndi pa mizinda yozungulira, chifukwa anthu ake ndi nkhutukumve ndipo sanamvere mawu anga.’”

< Yeremia 19 >