< Kejadian 49 >

1 Kemudian Yakub memanggil anak-anaknya dan berkata, "Berkumpullah di sini, di dekatku. Akan kuberitahukan kepadamu apa yang akan kalian alami di kemudian hari:
Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
2 Berkumpullah, hai anak-anak Yakub, dengarlah Israel, ayahmu.
“Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
3 Ruben, anakku yang sulung, engkaulah kekuatanku, buah pertama keperkasaanku. Engkau tergagah dan terkuat di antara semua anakku.
“Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
4 Engkau mudah tergoncang seperti air, sehingga bukan yang utama; sebab engkau tidur dengan selirku, kaunodai tempat tidur ayahmu.
Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
5 Simeon dan Lewi bersaudara; senjata mereka alat kekerasan.
“Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
6 Aku takkan ikut dalam permupakatan mereka, juga tidak di dalam perkumpulan mereka. Sebab mereka membunuh dalam kemarahan, melumpuhkan banteng demi kesenangan.
Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
7 Terkutuklah kemarahan mereka, karena dahsyatnya. Terkutuklah keberangan mereka, karena kejamnya. Aku akan menceraiberaikan mereka di seluruh Israel. Aku akan menghamburkan mereka di antara seluruh bangsa.
Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
8 Yehuda, engkau akan menerkam tengkuk musuhmu; saudara-saudaramu akan memujimu dan sujud di hadapanmu.
“Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
9 Yehuda bagaikan singa muda; ia membunuh mangsanya, lalu kembali ke sarangnya; ia menggeliat lalu berbaring, dan tak seorang pun berani mengusiknya.
Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
10 Yehuda akan memegang tongkat kerajaan, keturunannya akan memerintah selama-lamanya. Bangsa-bangsa akan membawa upeti, dan sujud dengan takluk di hadapannya.
Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
11 Anak keledainya diikatnya pada pohon, pohon anggur yang paling baik. Dia mencuci pakaiannya dengan anggur, anggur semerah darah.
Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
12 Merah matanya karena minum anggur, putih giginya karena minum susu.
Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
13 Zebulon akan diam di dekat laut; kapal-kapal akan berlabuh di pantainya; sampai Sidon batas wilayahnya.
“Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
14 Isakhar itu bagaikan keledai kuat yang berbaring di antara keranjang bebannya.
“Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
15 Dilihatnya betapa baiknya tempat itu dan betapa indahnya negeri itu, maka membungkuklah ia rela dibebani, dan dipaksa bekerja sebagai hamba.
Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
16 Engkau Dan, akan mengadili bangsamu, engkau menjadi suku seperti suku lain di Israel.
“Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
17 Engkau seperti ular di pinggir jalan, ular berbisa di tepi lorong, yang memagut tumit kuda sampai terlempar penunggangnya.
Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
18 Ya TUHAN, keselamatan yang Kauberikan, itulah yang kunanti-nantikan.
“Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
19 Gad, engkau akan diserang perampok, namun engkau akan balik merampok mereka.
“Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
20 Asyer, makananmu limpah mewah, kau akan menyediakan makanan bagi raja-raja.
“Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
21 Naftali, laksana rusa terlepas, sangat cantik anak-anaknya.
“Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
22 Yusuf bagai keledai muda, keledai liar dekat mata air, berlari-lari di lereng gunung.
“Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
23 Musuh menyerang dengan sengit, mengejarnya dengan busur dan panah.
Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
24 Namun Yusuf tetap kukuh lengannya, tetap kuat panahnya, karena kuasa Sang Gembala Mahakuat, Allah Yakub, Pelindung Israel.
Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
25 Allah ayahmu menolong engkau; Yang Mahakuasa memberkati engkau dengan hujan dari langit dan air dari bawah tanah. Dengan anak dan sapi,
Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
26 gandum dan bunga. Berkat Allah bapakmu melebihi kekayaan gunung-gunung yang sangat tua. Semoga turunlah semua berkat itu ke atas kepala Yusuf, ke atas dahinya. Dialah yang teristimewa di antara saudara-saudaranya.
Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
27 Benyamin adalah serigala ganas. Di pagi hari ia menerkam mangsanya. Di malam hari ia membagi-bagikannya."
“Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
28 Itulah kedua belas suku Israel, dan kata-kata yang diucapkan ayah mereka ketika memberi salam perpisahan kepada mereka masing-masing.
Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
29 Kemudian Yakub berpesan kepada anak-anaknya, "Sebentar lagi aku akan berpulang seperti leluhurku. Kuburkanlah aku nanti di samping mereka dalam gua di Makhpela, sebelah timur Mamre di tanah Kanaan. Abraham telah membeli gua dan ladang di sekitarnya dari Efron orang Het untuk dijadikan pekuburan.
Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
31 Di situ dikuburkan Abraham dan Sara, Ishak dan Ribka; dan di situ juga aku menguburkan Lea.
Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
32 Ladang dan gua yang ada di situ telah dibeli dari orang Het. Kuburkanlah aku di situ."
Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
33 Setelah Yakub selesai berpesan kepada anak-anaknya, berbaringlah ia lalu meninggal.
Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.

< Kejadian 49 >