< Dagiti Salmo 77 >

1 Iyikkisko ti umawag iti Dios, umawagakto iti Dios babaen iti timekko ket denggennakto ti Diosko.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
2 Binirokko ti Apo iti aldaw ti pannakariribukko; inngatok dagiti imak iti rabii, ket saanda a mabannog. Saanko a kayat a maliwliwa.
Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
3 Pinanpanunotko ti Dios iti panagasugko; pinanpanunotko ti maipapan kenkuana iti panagkapsutko. (Selah)
Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
4 Pinagtalinaedmo a nakamulagat dagiti matak; saanak a makasao gapu iti pannakariribukko.
Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
5 Pinanpanunotko dagiti aldaw a naglabas, maipanggep kadagiti panawen iti napalabas.
Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
6 Iti rabii, linagipko ti kanta a kinantak iti naminsan. Inam-amirisko a nalaing ken pinadasko nga awaten iti napasamak.
Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
7 Agnanayonto kadi a laksidennak ti Apo? Saannakto kadi a pulos manen a kaasian?
“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
8 Agnanayonto kadi a mapukaw ti kinapudnona iti tulagna? Agnanayonto kadi a saan a matungpal ti karina?
Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
9 Nalipatan kadin ti Dios ti mangparabur. Pinagsardeng kadi ti pungtotna ti kinamanangngaasina? (Selah)
Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
10 Kinunak, “Daytoy ti pagladingitak: awanen kadatayo ti makannawan nga ima ti Mannakabalin-amin.
Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
11 Ngem laglagipekto dagiti ar-aramidmo, O Yahweh; Saanto nga iwaksi iti panunotko dagiti nakaskasdaaw nga inaramidmo idi.
Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
12 Amirisekto a nalaing amin dagiti inaramidmo ken utobekto dagidiay.
Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
13 Nasantoan ti wagasmo O Dios; ania a dios ti pakaiyaspingan ti naindaklan a Diosmi?
Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
14 Sika ti Dios nga agar-aramid kadagiti nakakaskasdaaw; imparangarangmo ti pigsam kadagiti tattao.
Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
15 Pinagballigim dagiti tattaom babaen iti naindaklan a pannakabalinmo — dagiti kaputotan da Jacob ken ni Jose. (Selah)
Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
16 Nakitadaka dagiti danum, O Dios; nakitadaka dagiti danum, ket nagbutengda; nagtigerger ti kaadalman a paset ti baybay.
Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
17 Nangibuyat dagiti ulep iti danum; naggurruod ti tangatang, naggilap dagiti panam.
Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
18 Ti kasla gurruod a timekmo ket nangngegan iti angin, ti kimat ket sinilnaganna ti lubong; ti daga ket nagkintayeg ken naggungon.
Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 Ti danam ket limmabas iti baybay ken ti dalanmo kadagiti dadakkel a danum, ngem saan a makita dagiti tugotmo.
Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
20 Indauloam a kasla arban dagiti tattaom, babaen kada Moises ken Aaron.
Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

< Dagiti Salmo 77 >