< Isaias 55 >

1 “Umaykayo, dakayo amin a mawaw, umaykayo iti danum! Ken, dakayo nga awan kuartana umaykayo, gumatangkayo ken mangankayo! Umaykayo, gumatangkayo iti arak ken gatas uray awan kuarta ken awan iti pagbayadyo.
“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
2 Apay a mangtimbankayo iti pirak para iti saan a tinapay? Ken agtrabahokayo para iti saan a makapnek? Dumngegkayo a nasayaat kaniak ket mapnekayo, a kasla mangankayo iti kaimasan a taraon.
Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
3 Dumngegkayo ket umaykayo kaniak! Dumngegkayo, tapno agbiagkayo! Pudno a makitulagak kadakayo iti agnanayon a tulag, iti napudno a tulag a naited kenni David.
Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
4 Kitaenyo, insaadko isuna a kas saksi kadagiti nasion, a kas pangulo ken mangidadaulo kadagiti tattao.
Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
5 Kitaenyo, umawagkayonto iti nasion a saanyo nga am-ammo; ken agtarayto nga agturong kadakayo ti nasion a saan a makaam-ammo kadakayo gapu kenni Yahweh a Diosyo, a Nasantoan ti Israel, a nangpadayaw kadakayo.”
Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
6 Birokenyo ni Yahweh kabayatan a mabirukan pay laeng isuna; umawagkayo kenkuana bayat nga asideg isuna.
Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
7 Panawan koma ti nadangkes ti dalanna, ken ti managbasol a tao ti panunotna. Agsubli koma isuna kenni Yahweh, ket kaasiannanto isuna, ken iti Diostayo, a mangpakawanto kenkuana.
Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
8 “Ta ti panunotko ket saan a kas iti panunotmo, kasta met a dagiti wagasmo ket saanko a wagas—kastoy ti pakaammo ni Yahweh—
“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
9 ta no kasano a nangatngato dagiti langit ngem ti daga, kasta met a nangatngato dagiti wagasko ngem dagiti wagasmo, ken dagiti kapanunotak ngem dagiti kapanunotam.
“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
10 Ta no kasano nga agtinnag ti tudo ken niebe manipud langit ket saan nga agsubli sadiay no di ket sibuganda ti daga ket pagtuboenda ti bukel a lumangto ket mangipaay iti bukel kadagiti agmulmula ken tinapay kadagiti mangmangan,
Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 kastanto met ti sao a rummuar iti ngiwatko: saan daytoy nga agsubli kaniak nga awan serserbina, ngem tungpalen daytoy ti tarigagayko, ken agballiginto daytoy iti nangibaonak.
Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
12 Ta rummuarkayonto nga addaan rag-o ken maiturongkayonto a sitatalna; agpukkawto a sirarag-o dagiti bantay ken dagiti turod iti sangoananyo, ken agpalakpakto dagiti ima dagiti amin a kayo iti tay-ak.
Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
13 Imbes a dagiti sisiitan, agtubonto dagiti kayo; ken imbes a dagiti kalkalunay, agtubonto dagiti kayo nga arrayan, ket maipaayto daytoy kenni Yahweh, para iti naganna, a kas agnanayon a pagilasinan a saanto a mapukaw.”
Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”

< Isaias 55 >