< Efeso 5 >

1 Ngarud agbalinkayo a mannulad ti Dios, a kas dagiti ay-ayatenna nga annak.
Choncho, monga ana okondedwa, tsatirani chitsanzo cha Mulungu.
2 Ken agbiagtayo iti ayat, kas inayatnatayo met ni Cristo ken intedna ti bagina para kadatayo. Maysa isuna a daton ken sagut, nga agbalin a makaay-ayo nga ayamuom iti Dios.
Muzikondana monga Khristu anakonda ife nadzipereka yekha chifukwa cha ife monga chopereka cha fungo lokoma ndi nsembe kwa Mulungu.
3 Nasken a saan a madakamat kadakayo ti kinaderrep wenno aniaman a kinarugit wenno nagartem a panangagum, a kas umno kadagiti namati.
Koma pakati panu pasamveke nʼpangʼono pomwe zadama, kapena za mtundu wina uliwonse wa chodetsa, kapena za umbombo, chifukwa izi ndi zosayenera kwa anthu oyera a Mulungu.
4 Saanyo nga ibaga uray dagiti naaalas, minamaag a sasao, wenno makaidadanes nga angaw, a saan nga umno. Ngem ketdi adda koma ti kinamanagyaman.
Musamatukwane, kuyankhula zopusa kapena kunena nthabwala zopanda pake, zomwe ndi zosayenera, koma mʼmalo mwake muziyamika.
5 Ta nalawag nga ammoyo nga awan ti naderrep, narugit, wenno naagum a tao, nga isu ket, maysa nga agrukbab kadagiti didiosen, nga adda tawidna iti pagarian ni Cristo ken ti Dios.
Dziwani ichi, palibe wadama, wochita zonyansa kapena waumbombo, munthu wotero ali ngati wopembedza mafano, amenewa alibe malo mu ufumu wa Khristu ndi Mulungu.
6 Saanyo a palubosan iti uray maysa nga allilawennakayo babaen ti ubbaw a sasao. Gapu kadagitoy a banbanag ket umay ti pungtot ti Dios kadagiti annak ti kinasukir.
Musalole wina akunamizeni ndi mawu opanda pake, pakuti chifukwa cha zinthu ngati izi mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa amene samvera.
7 Isu a saankayo a makipaset kadagitoy.
Nʼchifukwa chake musamayanjane nawo anthu otere.
8 Ta naminsan a dakayo ket kinasipnget, ngem ita ket lawagkayon iti Apo. Isu a magnakayo a kas annak ti lawag.
Pajatu inu nthawi ina munali mdima, koma tsopano ndinu kuwunika mwa Ambuye. Mukhale ngati ana akuwunika
9 Ta ti bunga ti lawag ket amin a kinaimbag, kinalinteg, ken kinapudno.
(pakuti pamene pali kuwunika pamapezekaponso zabwino zonse, chilungamo ndi choonadi).
10 Ammoenyo ania iti makaay-ayo iti Apo.
Inu mufufuze chimene chimakondweretsa Ambuye.
11 Saankayo a makipaset kadagiti saan a nabunga nga ar-aramid iti kinasipnget. Ngem ketdi, ibutaktakyo dagitoy.
Musayanjane nazo ntchito zosapindulitsa za mdima, koma mʼmalo mwake muzitsutse.
12 Ta dagiti banbanag a naaramid babaen kadakuada iti nalimed ket nakababain unay nga iladawan.
Pakuti ndi zochititsa manyazi ngakhale kutchula zomwe zimachitika mseri.
13 Amin a banbanag, no maiparangarangda babaen iti lawag, ket naibutaktak.
Koma kuwala kumawunikira zinthu, ndipo chilichonse chimaonekera poyera. Choncho chilichonse choonekera poyera chimasandukanso kuwala.
14 Ta ti tunggal banag a naiparangarang ket agbalin a lawag. Ngarud ibagbaga daytoy, “Agriingkayo, dakayo a matmaturog, ket agungarkayo manipud iti patay, ket agranniagto ni Cristo kadakayo.”
Nʼchifukwa chake Malemba akuti, “Dzuka, wamtulo iwe, uka kwa akufa, ndipo Khristu adzakuwalira.”
15 Ngarud agannadkayo iti panagbiagyo, saan a kas kadagiti tattao a saan a nasirib ngem kas nasirib.
Samalani makhalidwe anu, musakhale ngati opanda nzeru koma ngati anzeru.
16 Subbotenyo iti tiempo gapu ta dagiti al-aldaw ket dakes.
Gwiritsani ntchito mpata uliwonse, chifukwa masiku ano ndi oyipa.
17 Saankayo nga agbalin a maag. Ngem ketdi, awatenyo no ania ti pagayatan iti Dios.
Choncho musakhale opusa, koma mudziwe zimene Ambuye akufuna kuti muchite.
18 Ken saankayo nga agbartek iti arak, ta mangiturong dayta iti pannakadadael. Ngem ketdi, mapnokayo koma iti Espiritu Santo.
Musaledzere ndi vinyo, chifukwa adzawononga moyo wanu. Mʼmalo mwake, mudzazidwe ndi Mzimu Woyera.
19 Agsaritakayo iti tunggal maysa babaen kadagiti salmo ken kadagiti himno ken naespirituan a kankanta. Agkanta ken agdaydayawkayo babaen iti pusoyo iti Apo.
Muziyankhulana wina ndi mnzake mawu a Masalimo, nyimbo za Mulungu ndi nyimbo za uzimu. Muziyimbira Ambuye movomerezana ndi mitima yanu.
20 Agyamankayo a kankanayon para kadagiti amin a banbanag iti nagan ni Apotayo a Jesu-Cristo iti Dios Ama.
Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
21 Agpaituraykayo iti tumunggal maysa kas panagraem kenni Cristo.
Gonjeranani wina ndi mnzake, kuonetsa kuopa Khristu.
22 Assawa a babbai, agpaituraykayo kadagiti assawayo a lallaki, a kas iti Apo.
Inu akazi, muzigonjera amuna anu, monga mumagonjera kwa Ambuye.
23 Ta ti asawa a lalaki ti ulo iti asawa a babai, a kas met ni Cristo nga ulo iti iglesia. Isuna iti mangisalakan iti bagi.
Pakuti mwamuna ndi mutu wa mkazi monga momwe Khristu ali mutu wa mpingo, thupi lake, limene Iyeyo ndi Mpulumutsi wake.
24 Ngem kas iti iglesia ket iturayan ni Cristo, kasta met dagiti asawa a babbai kadagiti asawada a lallaki iti amin a banag.
Tsono monga mpingo umagonjera Khristu, momwemonso akazi akuyenera kugonjera amuna awo mu zonse.
25 Asawa a lallaki, ayatenyo dagiti asawayo a babbai a kas inayat ni Cristo ti iglesia ken intedna ti bagina para kenkuana.
Inu amuna, kondani akazi anu monga momwe Khristu anakondera mpingo nadzipereka yekha mʼmalo mwa mpingowo
26 Inaramidna daytoy tapno mapagbalinna isuna a nasantoan. Dinalusanna ti iglesia babaen iti panangugasna iti danum babaen ti sao.
kuti awupatule ukhale oyera, atawuyeretsa powusambitsa ndi madzi omwe ndi mawu ake.
27 Inaramidna daytoy tapno maiparangna iti bagina ti maysa a nadayag nga iglesia, nga awan mansana wenno karetket wenno aniaman a kas kadagitoy a banag, ngem ketdi nasantoan ken awan biddutna.
Anachita zimenezi kuti awupereke mpingowo kwa Iye mwini, mpingo wowala ndi waulemerero, wopanda banga kapena makwinya kapena chilema chilichonse, koma oyera ndi wangwiro.
28 Iti isu met laeng a wagas, masapul nga ayaten dagiti asawa a lallaki dagiti bukodda nga asawa a babbai a kas bukodda a bagi. Ti siasinoman nga agay-ayat iti bukodna nga asawa a babai ket ay-ayatenna ti bagina.
Momwemonso, amuna akuyenera kukonda akazi awo monga matupi awo. Iye amene akonda mkazi wake adzikondanso yekha.
29 Awan ti siasinoman a nanggura iti bukodna a bagi. Ngem ketdi, pakanenna ken ayatenna daytoy, a kas ay-ayaten met ni Cristo ti iglesia.
Pakuti palibe amene amadana nalo thupi lake, koma amalidyetsa ndi kulisamalira bwino, monga momwe Khristu amachitira ndi mpingo wake
30 Ta kamkamengnatayo iti bagina.
pakuti ndife ziwalo za thupi lake.
31 “Para iti daytoy a rason a panawan ti lalaki ti ama ken inana ket maitipon iti asawana a babai, ket ti dua ket agbalin a maysa a bagi.”
“Pa chifukwa ichi, mwamuna adzasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.”
32 Daytoy ket dakkel a nailimed a kinapudno, ngem agsasaoak maipanggep kenni Cristo ken ti iglesia.
Ichi ndi chinsinsi chozama, koma ine ndikunena za Khristu ndi mpingo.
33 Nupay kasta, masapul met nga ayaten ti tunggal maysa kadakayo ti bukodna nga asawa a babai a kas iti bagina, ken masapul a raemen ti asawa a babai ti asawana a lalaki.
Chomwecho, aliyense mwa inu akuyenera kukonda mkazi wake monga adzikondera iye mwini, ndipo mkazi akuyenera kulemekeza mwamuna wake.

< Efeso 5 >