< 2 Ar-ari 19 >

1 Napasamak daytoy nga idi nangngeg ni Ari Hezekias ti padamagda, rinay-abna ti pagan-anayna, nagkawes isuna iti nakersang a lupot, ket simrek iti balay ni Yahweh.
Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
2 Imbaonna a nakakawes iti nakersang a lupot da Eliakim a mangimatmaton iti palasio, ni Sebna nga eskriba ken dagiti panglakayen dagiti papadi kenni Isaias a propeta, nga anak ni Amos.
Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
3 Kinunada kenkuana, “Kuna ni Hezekias, 'Daytoy nga aldaw ket aldaw ti pannakaparparigat, pannakatubngar ken pannakaibabain, ta dimtengen ti tiempo ti pannakaiyanak dagiti ubbing, ngem awanen ti pigsa tapno maiyanakda.
Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.
4 Mabalin a denggen ni Yahweh a Diosmo dagiti amin a sasao ti panguloen a komandante, nga imbaon ti ari ti Asiria nga apona tapno ibabainna ti sibibiag a Dios, ken tapno tubngarennanto dagiti sasao a nangngeg ni Yahweh a Diosmo. Ita, itag-aymo ti kararagmo para kadagiti nabati nga adda agingga ita.”'
Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’”
5 Isu a napan dagiti adipen ni Ari Hezekias kenni Isaias,
Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
6 ket kinuna ni Isaias kadakuada, “Ibagayo iti amoyo: 'kuna ni Yahweh, “Saanka nga agbuteng kadagiti sasao a nangngegam, a nangibabainan kaniak dagiti adipen ti ari ti Asiria.
Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
7 Kitaem, mangikabilak iti espiritu kenkuana, ket mangngegna ti maysa a damag ket agsubli iti bukodna a daga. Tinnagek isuna babaen iti kampilan iti bukodna a daga."”'
Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
8 Ket nagsubli ti panguloen a komandante ket naduktalanna a makigubgubat ti ari ti Asiria a maibusor iti Libna, ta nangngegna a pimmanaw ti ari manipud idiay Lakis.
Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
9 Kalpasanna, nangngeg ni Senakerib a nagsagana ni Tirhaka nga ari ti Etiopia ken Egipto a manggubat a maibusor kenkuana, isu a nangibaon manen isuna kadagiti mensahero nga addaan iti mensahe kenni Hezekias:
Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
10 “Ibagayo kenni Hezekias nga ari ti Juda, 'Saanmo nga ipalubos nga allilawennaka ti Diosmo a pagtaltalkam iti panangibagbagana, “Saanto a maiyawat ti Jerusalem iti ari ti Asiria.”
“Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
11 Kitaem, nangngegmo ti inaramid dagiti ar-ari ti Asiria kadagiti amin a daga babaen iti panangdadaelda amin kadagitoy. Maispalnakanto ngata met?
Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka?
12 Naispal kadi ida dagiti dios dagiti nasion, dagiti nasion a dinadael dagiti ammak: ti Gosan, Haran, Resef, ken dagiti tattao ti Eden idiay Telassar?
Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa?
13 Sadino ti ayan dagiti ari ti Hamat, ti ari ti Arpad, ti Ari dagiti siudad ti Sefravaim, Hena ken Ivva?'”
Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”
14 Naawat ni Hezekias daytoy a surat manipud kadagiti mensahero ket binasana daytoy. Kalpasanna, simmang-at isuna idiay balay ni Yahweh ket inyukradna daytoy iti sangoananna.
Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova.
15 Ket nagkararag ni Hezekias iti sangoanan ni Yahweh ket kinunana, '“Yahweh a Mannakabalin-amin, Dios ti Israel, sika a nakatugaw iti ngatoen dagiti kerubim, sika laeng ti Dios kadagiti amin a pagarian ditoy daga. Pinarsuam ti langit ken ti daga.
Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Ipangagmo Yahweh, ket dumngegka. Luktam dagita matam Yahweh ket kumitaka ken denggem dagiti sao ni Senakerib nga impatulodna tapno laisenna ti sibibiag a Dios.
Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.
17 Pudno Yahweh, a dinadael dagiti ar-ari ti Asiria dagiti nasion ken dagiti dagada.
“Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo.
18 Impuorda dagiti diosda, ta saan dagitoy a dios, aramid laeng dagitoy dagiti ima dagiti tattao, kayo ken bato laeng dagitoy. Isu a dinadael ida dagiti Asiriano.
Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu.
19 Ita ngarud, Yahweh a Diosmi, isalaknnakami, agpakaasiak kenka, manipud iti kinabilegna, tapno maammoan dagiti amin a pagarian ditoy daga a sika ni Yahweh nga agmaymaysa a Dios.”
Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”
20 Ket nangipatulod iti mensahe ni Isaias nga anak ni Amos kenni Hezekias a kunana, “Ibagbaga ni Yahweh a Dios ti Israel, 'Gapu ta nagkararagka kaniak maipapan kenni Senakerib nga ari ti Asiria, nangngegka.
Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’”
21 Daytoy ti sao ni Yahweh maipapan kenkuana: “Lalaisennaka ti birhen nga anak a babai ti Sion ken katawaannaka nga umsien. Iwingiwingna ti ulona kenka ti anak a babai ti Jerusalem.
Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa: “Namwali wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka iwe. Mwana wamkazi wa Yerusalemu akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.
22 Siasino ti kinarit ken linaismo? Ket siasino ti binugkawam ken kinitam nga addaan iti kinatangsit? Maibusor iti Nasantoan iti Israel!
Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani? Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako ndi kumuyangʼana monyada? Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!
23 Babaen kadagiti mensaherom, kinaritmo ti Apo, ket kinunam, 'Babaen kadagiti adu a karwahek, nakasang-atak kadagiti tapaw dagiti banbantay, inggana kadagiti kangangatoan a banbantay iti Libano. Pukanekto dagiti nangangato a sedro ken dagiti kasasayaatan a kaykayo ti saleng sadiay. Ket serkekto dagiti kaaadaywan a paset daytoy, iti nabunga unay a paset ti kabakiran.
Kudzera mwa amithenga ako wonyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta ochuluka ndinakwera mapiri ataliatali, pa msonga za mapiri a Lebanoni. Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri, mitengo yake ya payini yabwino kwambiri. Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni, mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.
24 Nagkaliak kadagiti bubon ket umminumak kadagiti ganggannaet a danum. Pinamagaak amin dagiti karayan ti Egipto kadagiti dapanko.'
Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndipo ndinamwa madzi a kumeneko. Ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’”
25 Saanmo kadi a nanggeg no kasano nga inkeddengko idi pay laeng, ket inaramidko daytoy idi pay punganay? Ita, tungtungpalekon. Adtoyka a mamagbalin kadagiti natalged a siudad a gabsuon dagiti dadadel.
“‘Kodi sunamvepo? Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale. Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndachita kuti zichitikedi, iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
26 Dagiti awanan pigsa nga agnanaed kadagitoy ket nawarawara ken nabainan. Kaslada kadagiti mulmula iti talon, berde a ruot, ti ruot a nagtubo iti bubongan wenno iti talon, nakset sakbay a dimmakkel.
Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu, athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi. Ali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu womera pa denga, umene umawuma usanakule nʼkomwe.’”
27 Ngem ammok no agtugtugawka, no rumrummuarka, no umun-unegka ken no makapungpungtotka kaniak.
“‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako, kutuluka kwako ndi kulowa kwako, ndi mkwiyo wako pa Ine.
28 Gapu iti panagpungpungtotmo kaniak, ken gapu ta nangngegko ti kinatangsitmo, taldengak ta agongmo, ken busalak ta ngiwatmo; isublika iti dalan a naggapuam.”
Chifukwa chakuti wandikwiyira ndipo ndamva za mwano wako, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa njira yomwe unadzera pobwera.’
29 Daytoyto ti pagilasinam; Ita a tawen, kanem dagiti agtubtubo laeng, ket iti maikadua a tawen, kanem ti agtubo manipud iti dayta. Ngem iti maikatlo a tawen, masapul nga agmulaka ket apitem, agmulaka kadagiti ubas ket kanem dagiti bungada.
“Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi: “Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa, ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera. Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola, mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.
30 Agramut manen ket agbunga dagiti nabati a nakalasat iti balay ti Juda.
Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale adzazika mizu ndi kubereka zipatso.
31 Ta manipud iti Jerusalem, ti nabati ket rummuarto, umayto dagiti nakalasat manipud iti Bantay Sion. Ti regta ni Yahweh a Mannakabalin-amin ti mangaramid iti daytoy.
Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.” “Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
32 Ngarud kinuna ni Yahweh daytoy maipapan iti ari ti Asiria: “Saanto isuna a makastrek iti daytoy a siudad wenno mangibiat ti pana sadiay. Saanto nga makaumay isuna a sikakalasag a makaasideg iti siudad wenno mangbangon ti panglakub iti aglawlawna.
“Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi: “‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi. Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.
33 Ti dalan a nagnaanna nga immay ket isunto met laeng ti dalan a pagsublianna; saanto a sumrek iti daytoy a siudad. Daytoy ti pakaammo ni Yahweh.”
Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu, akutero Yehova.
34 Ta salaknibak ken ispalekto daytoy a siudad, para iti bukodko a dayaw ken gapu iti adipenko a ni David.'”
Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
35 Napasamak daytoy iti rabbii a rimmuar ti maysa nga anghel ni Yahweh, ket rinautna ti kampo dagiti Siriano, pinapatayna ti 185, 000 a soldado. Idi nakariing dagiti tattao iti agsapa, agkaraiwara dagiti bangkay.
Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda!
36 Isu a pimmanaw ni Senakerib nga ari ti Asiria iti Israel ket nagawid ken nagnaed idiay Nineve.
Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.
37 Iti saan a nagbayag, kabayatan iti panagdaydayawna iti balay ni Nisrok a diosna, pinapatay isuna dagiti annakna a da Adramelek ken Sarezer babaen iti kampilan. Ket naglibasda a napan idiay daga ti Ararat. Ni Esarhadon nga anakna ti nagbalin nga ari a simmukat kenkuana.
Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Ar-ari 19 >