< 1 Corinto 15 >

1 Ita, ipalagipko kadakayo kakabsat, ti maipapan iti ebanghelio nga inwaragawagko kadakayo, nga inawatyo ken pagtaktakderanyo.
Tsono abale, ndikufuna ndikukumbutseni za Uthenga Wabwino umene ndinakulalikirani. Munawulandira ndipo munawukhulupirira kolimba.
2 Naisalakankayo babaen iti daytoy nga ebanghelio, no iggamanyo a sititibker ti sao nga inkasabak kadakayo, malaksid no inuubbaw ti panamatiyo.
Inu munapulumutsidwa ndi Uthenga Wabwinowu, ngati mwasunga mawu amene ndinakulalikirani. Kupanda kutero, mwangokhulupirira pachabe.
3 Ta intedko kadakayo a kas umuna a kapatgan ti isu met laeng nga inawatko: a natay ni Cristo gapu kadagiti basbasoltayo segun iti Nasantoan a Sursurat,
Pakuti chimene ndinalandira ndinapereka kwa inu monga chofunika kuposa zonse, kuti Khristu anafera zoyipa zathu monga mwa Malemba,
4 a naitanem ken nagungar isuna iti maikatallo nga aldaw segun iti Nasantoan a Surat.
kuti anayikidwa mʼmanda, kuti anaukitsidwa tsiku lachitatu monga mwa Malemba;
5 Ken nagparang isuna kenni Cefas ken kalpasanna, kadagiti Sangapulo ket Dua.
ndipo kuti anaonekera kwa Petro, ndipo kenaka kwa Atumwi khumi ndi awiriwo.
6 Kalpasanna naminpinsan a nagparang isuna kadagiti nasurok a lima gasut a kakabsattayo. Kaadduan kadakuada ti sibibiag pay laeng ngem nakaturogen dagiti dadduma.
Pambuyo pake, Iye anaonekera kwa anthu oposa 500 mwa abale pa nthawi imodzi, ndipo ambiri mwa iwo akanali ndi moyo ngakhale kuti ena anagona tulo.
7 Kalpasanna nagparang isuna kenni Santiago, ken kadagiti amin nga apostol.
Kenaka anaonekeranso kwa Yakobo, kenaka kwa atumwi onse.
8 Maudi iti amin, nagparang isuna kaniak, a kas iti maysa nga ubing a naiyanak iti saan nga umiso a tiempo.
Potsiriza pa onse anaonekeranso kwa ine, monga mwana wobadwa nthawi isanakwane.
9 Ta siak ti kababaan kadagiti amin nga apostol. Saanak a maikari a maawagan nga apostol, gapu ta indadanesko ti iglesia ti Dios.
Pakuti ine ndine wamngʼono kwa atumwi ndipo sindiyenera nʼkomwe kutchedwa mtumwi chifukwa ndinazunza mpingo wa Mulungu.
10 Ngem babaen iti parabur ti Dios siak ket siak, ken saan nga ubbaw ti parabur ti Dios nga adda kaniak. Ngem ketdi, ad-adda nga inkarkarigatak ti nagtrabaho ngem iti amin kadakuada. Ngem saan a siak ti nagtrabaho no di ket ti parabur ti Dios nga adda kaniak.
Koma mwachisomo cha Mulungu, ndili mmene ndililimu, ndipo chisomo chake kwa ine sichinali chopanda ntchito. Ndinagwira ntchito kuposa ena onse a iwo. Choncho sindine koma chisomo cha Mulungu chimene chinali ndi ine.
11 Ngarud, siak man wenno isuda, nangasabakami isu a namatikayo.
Tsono kaya ndi ineyo kapena iwowo, izi ndi zomwe timalalikira, ndipo izi ndi zimene munakhulupirira.
12 Ita no naiwaragawag ni Cristo a kas nagungar manipud iti patay, kasano a maibaga iti dadduma kadakayo nga awan ti panagungar dagiti natay.
Koma ngati timalalikira kuti Khristu anaukitsidwa kwa akufa, zikutheka bwanji kuti ena mwa inu azinena kuti kulibe kuuka kwa akufa?
13 Ngem no awan ti panagungar dagiti natay, saan met ngarud a napagungar uray pay ni Cristo.
Ngati kulibe kuuka kwa akufa, ndiye kuti ngakhale Khristu sanaukenso.
14 Ken no saan a napagungar ni Cristo, ubbaw ngarud dagiti ikaskasabatayo ken uray dagiti pammatiyo ket ubbaw met laeng.
Ndipo ngati Khristu sanaukitsidwe, ndiye kuti kulalikira kwathu nʼkopanda ntchito, ndipo chikhulupiriro chanu nʼchopandanso ntchito.
15 Ken naduktalan a datayo ket palso a saksi ti Dios, gapu ta nangibagatayo iti pammaneknek a maibusor ti Dios, ibagbagatayo a pinagungarna ni Cristo, ngem saan met.
Kuwonjezera pamenepa, ndiye kuti ndife mboni zabodza pa za Mulungu, pakuti tikuchita umboni kuti Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa. Ngati nʼzoona kuti akufa saukitsidwa, ndiye kuti Mulungu sanaukitsenso Khristu.
16 Ta no saan a napagungar dagiti natay, saan met garud a napagungar ni Cristo.
Pakuti ngati akufa saukitsidwa, ndiye kuti nayenso Khristu sanaukitsidwe.
17 Ket no saan a napagungar ni Cristo, dagiti pammatiyo ket ubbaw, ken addakayo pay laeng kadagiti basbasolyo.
Ndipo ngati Khristu sanaukitsidwe, chikhulupiriro chanu nʼchopanda ntchito; mukanali mu machimo anu.
18 Ket uray dagidiay natay kenni Cristo ket napukawda met.
Ndiye kuti nawonso amene agona tulo mwa Ambuye ndi otayika.
19 No iti daytoy laeng a biag nga addaantayo iti namnama para iti masakbayan kenni Cristo, datayo ti kangrunaan a makaassian kadagiti amin a tattao.
Ngati kukanakhala kuti tili ndi chiyembekezo mwa Khristu mʼmoyo uno wokha, tikanakhala omvetsa chisoni kuposa anthu ena onse.
20 Ngem ita, napagungaren ni Cristo manipud iti patay, dagiti umuna a bunga dagiti natay.
Koma nʼzoonadi kuti Khristu anaukitsidwa kwa kufa, chipatso choyamba cha onse ogona tulo.
21 Agsipud ta immay ti patay babaen iti tao, babaen met laeng iti tao nga immay ti panagungar dagiti natay.
Pakuti monga imfa inadza kudzera mwa munthu, kuuka kwa akufa kwabweranso kudzera mwa munthu.
22 Ta kas kenni Adan a matay ti amin, kas met laeng kenni Cristo mapabbiag ti amin.
Pakuti monga mwa Adamu onse amafa, chomwechonso mwa Khristu onse adzakhala ndi amoyo.
23 Ngem iti panagsasaruno segun kenni Cristo: Ni Cristo, ti immuna a bunga, ken kalpasanna, mapabbiagto met dagidiay naibilang kenni Cristo iti yaayna.
Koma aliyense adzauka pa nthawi yake. Khristu ndiye woyambirira, pambuyo pake, pamene Khristu adzabwera, iwo amene ali ake adzauka.
24 Ket daytoyto ti pagleppasanna, inton ited ni Cristo ti pagarian ti Dios Ama. Mapasamak daytoy inton ikkatenna amin a paglintegan, turay ken pannakabalin.
Pamenepo chimaliziro chidzafika, pamene Iye adzapereka ufumu kwa Mulungu Atate, atathetsa ufumu wonse, ulamuliro wonse ndi mphamvu zonse.
25 Ta masapul nga agturay isuna aginggana a maikabilna amin dagiti kabusorna iti sirok iti sakana.
Pakuti Iye ayenera kulamulira mpaka Mulungu atayika pansi pa mapazi ake adani ake onse.
26 Ti kabusor a maudi a madadael ket ti patay.
Mdani wotsiriza kuwonongedwa ndi imfa.
27 Ta “inkabilna amin a banag iti sirok dagiti sakana.” Ngem no ibagbaga nga, “inkabilna ti amin a banag,” nalawag a saan a mairaman ti nangikabil iti tunggal banag iti turayna.
Pakuti Mulungu “wayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake.” Ponena kuti wayika “zinthu zonse pansi pa mapazi ake,” nʼchodziwikiratu kuti sakuphatikizapo ndi Mulungu yemwe, amene anayika zinthu zonse pansi pa Khristu.
28 Inton iturturayannan ti tunggal banag, mismo a ti Anak ket iturayan met ti nangikabil iti amin iti turayna. Mapasamak daytoy tapno agbalin ti Dios Ama nga amin kadagiti amin.
Pamene adzatsiriza kuchita zimenezi, Mwana weniweniyo adzakhala pansi pa ulamuliro wa Iye amene anayika zinthu zonse pansi pake, kuti Mulungu akhale zonse mu zonse.
29 Ta no saan, ania ngarud ti aramiden dagidiay nabautisaran maipaay kadagiti natay? No saan a pulos a napagungar dagiti natay, apay ngarud ta nabautisaranda maipaay kadakuada?
Tsono ngati kulibe kuuka kwa akufa, kodi iwo amene akubatizidwa chifukwa cha akufa, adzatani? Ngati akufa saukitsidwa nʼkomwe, bwanji nanga anthu akubatizidwa mʼmalo mwawo?
30 Ken apay ngarud nga adda tayo iti peggad iti tunggal oras?
Ndipo kwa ife, tikuyikiranji moyo wathu pachiswe nthawi ndi nthawi?
31 Kakabsat, babaen ti panangipasindayawko kadakayo, nga adda kaniak kenni Cristo Jesus nga Apotayo, ipakdaarko daytoy: Inaldawak a matmatay.
Abale, ndimafa tsiku ndi tsiku, ndikunenetsa zimenezi, mongotsimikizira monga ndimakunyadirani mwa Khristu Yesu Ambuye athu.
32 Ania ti magun-odko, manipud iti panagkita dagiti tattao, no makirangetak kadagiti narurungsot nga ayup idiay Efeso, no saan a napagungar dagiti natay? “Mangan ken uminomtayo, ta mataytayon no bigat.”
Ngati ndinalimbana ndi zirombo za kuthengo ku Efeso pa zifukwa za umunthu chabe, ndapindulanji? Ngati akufa sadzaukitsidwa, “Tiyeni tidye ndi kumwa, pakuti mawa tifa.”
33 Saankayo nga agpaallilaw, “Daddadaelen dagiti dakes a kakadua dagiti nasasayaat a kagagalad.”
Musasocheretsedwe, “Kukhala mʼmagulu oyipa kumawononga makhalidwe abwino.”
34 Agriingkayo! Agbiagkayo iti nalinteg! Saanyon nga itultuloy ti agbasol. Ta ti dadduma kadakayo ket awan ti ammoda maipapan ti Dios. Ibagak daytoy tapno agbainkayo.
Ganizani bwino monga kuyenerera, ndiye lekani kuchimwa; pakuti pali ena amene sadziwa Mulungu. Ndikunena izi kuti muchite manyazi.
35 Ngem addanto ti mangibaga, “Kasano a napagungar dagiti natay? Ania a kita ti bagi ti pagbalinanda no umayda?
Koma wina akhoza kufunsa kuti, “Kodi akufa amaukitsidwa motani? Adzauka ndi thupi la mtundu wanji?”
36 Nagkukunengkayo unay! Saan a mangrugi a dumakkel ti aniaman nga inmulayo malaksid a matay daytoy.
Wopusa iwe! Chimene mudzala sichikhala ndi moyo pokhapokha chitayamba chafa.
37 Ken ti inmulayo ket saanto nga isu ti bagi a pagbalinanna, ngem maysa laeng a bukel. Mabalin nga agbalin daytoy a trigo wenno sabali.
Mukadzala, simudzala thupi limene lidzamere, koma mbewu chabe, mwina ya tirigu kapena ya china chake.
38 Ngem ikkanto ti Dios daytoy iti bagi segun iti pagayatanna, ken iti tunggal bukel ti bukodda a bagi.
Koma Mulungu amayipatsa thupi monga Iye wafunira, ku mbewu ya mtundu uliwonse amapereka thupi lakelake.
39 Saan nga agpapada ti amin a lasag. No diket, adda ti maysa a lasag dagiti tattao ken sabali pay a lasag para kadagiti ay-ayup, ken adda pay sabali a lasag para kadagiti billit ken sabali pay para kadagiti lames.
Mnofu siwofanana. Anthu ali ndi mnofu wa mtundu wina, nyama zili ndi wina, mbalame zili ndi wina, nsomba zili ndi winanso.
40 Adda met dagiti banbanag nga adda iti tangatang ken dagiti naindagaan a babanag. Ngem ti dayag dagiti banbanag nga adda iti tangatang ket maysa a kita ti dayag ken sabali met a dayag ti dayag dagiti naindagaan.
Palinso matupi akumwamba ndipo palinso matupi a dziko lapansi; koma ulemerero wa matupi akumwamba ndi wina, ndi wa matupi a dziko lapansi ndi winanso.
41 Adda ti maysa a dayag ti init, ken sabali pay a dayag ti bulan ken sabali a dayag dagiti bitbituen. Ta naiduma ti dayag ti maysa a bituen kadagiti sabali pay a bituen.
Dzuwa lili ndi ulemerero wake, ndipo pali ulemerero wina wa mwezi, palinso ulemerero winanso wa nyenyezi. Ulemerero wa nyenyezi ndi wosiyanasiyana.
42 Kastoy met laeng iti panagungar dagiti natay. Mapukaw ti aniaman a naimula, ken saan a mapukaw ti napagungar.
Zidzaterenso pamene akufa adzauka. Thupi loyikidwa mʼnthaka ngati mbewu limavunda, koma likadzauka lidzakhala losavunda.
43 Naimula daytoy iti pannakaibabain, napagungar daytoy iti dayag. Naimula daytoy iti kinakapsut, napagungar daytoy iti pannakabalin.
Limayikidwa mʼmanda mopanda ulemu, koma likadzaukitsidwa lidzakhala ndi ulemerero. Limayikidwa mʼmanda lili lofowoka, koma likadzaukitsidwa lidzakhala ndi mphamvu.
44 Naimula daytoy a gagangay a bagi, napagungar daytoy a naespirituan a bagi. No adda ti gagangay a bagi, adda met ti naespirituan a bagi.
Limayikidwa mʼmanda thupi la mnofu chabe, koma likadzaukitsidwa lidzakhala lauzimu. Ngati pali thupi la mnofu, palinso thupi lauzimu.
45 Isu a naisurat met laeng, “Nagbalin a sibibiag a kararua ti immuna a lalaki a ni Adan.” Nagbalin nga espiritu a mangit-ited iti biag ti naudi nga Adan.
Kwalembedwa kuti, “Munthu woyamba Adamu anakhala wamoyo,” Adamu wotsiriza anakhala wopatsa moyo.
46 Ngem saan nga immuna nga immay ti naespirituan ngem ketdi ti gagangay, ken kalpasanna ti naespirituan.
Zauzimu sizinabwere koyambirira, koma zachilengedwe, pambuyo pake zauzimu.
47 Ti immuna a lalaki ket nagtaud iti daga a naaramid manipud iti tapuk. Ti maikadua a tao ket naggapu idiay langit.
Munthu woyamba anali wa dziko lapansi, wochokera mʼnthaka koma munthu wachiwiri anali wochokera kumwamba.
48 Kas iti maysa a naaramid manipud iti tapuk, kasta met dagiti naaramid manipud iti tapok. Ken kas iti tao a naggapu iti langit, kasta met dagiti naggapu idiay langit.
Monga analili munthu wa dziko lapansi, momwemonso anthu onse amene ndi a dziko lapansi. Ndipo monga alili munthu wakumwamba, momwemonso anthu onse amene ndi akumwamba.
49 Kas iti panangawit tayo iti ladawan iti tao iti tapuk, awitentayonto met ti ladawan iti tao iti langit.
Ndipo monga momwe tinabadwa ofanana ndi munthu wa dziko lapansi uja, momwemonso tidzakhala ofanana ndi munthu wakumwamba.
50 Ita, daytoy ti ibagak kakabsat, a saan a matawid dayta a lasag ken dara ti pagarian ti Dios. Saan a matawid uray pay dagiti mapukaw ti saan a mapukaw.
Ndikunenetsa, abale, kuti thupi ndi magazi sizingathe kulowa mu ufumu wa Mulungu, ndipo zimene zimavunda sizingathe kulowa kumene zinthu sizivunda.
51 Kitaem! Ibagak kadakayo ti palimed a kinapudno: Saantayo amin a matay, ngem mabaliwantayonto amin.
Tamverani, ndikuwuzeni chinsinsi. Tonse sitidzagona tulo, koma tonse tidzasandulika.
52 Mabaliwantayonto iti apagbiit, iti panagkirem iti mata, iti maudi a panaguni ti trumpeta. Ta aguninto ti trumpeta, ken mapagungarto dagiti natay a saanen a mapukaw, ken mabaliwantayonto.
Zidzachitika mwadzidzidzi, mʼkamphindi kochepa, monga ngati kuphethira kwa diso, pa lipenga lotsiriza. Pakuti lipenga lidzalira, akufa adzaukitsidwa opanda chovunda, ndipo ife tidzasandulika.
53 Ta daytoy a mapukaw ket masapul nga ikabilna ti saan a mapukaw ken ti matay ket masapul nga ikabilna kenkuana ti saan a matay.
Pakuti chovunda chiyenera kuvala chosavunda, ndi thupi ili lakufa liyenera kuvala losafa.
54 Ngem no inkabilen daytoy a mapukaw ti saan a mapukaw ken inkabilen ti matay ti saan a matay, ket mapasamakto iti naibaga a nakasurat, “Tinilmonen ti balligi ti patay.”
Pamene thupi lovundali likadzasanduka losavunda, ndipo thupi lotha kufali likadzasanduka losatha kufa, pamenepo zidzakwaniritsidwa zimene zinalembedwa zakuti, “Imfa yogonjetsedwa kwathunthu.”
55 “Patay, sadino ti ayan iti balligim? Patay, sadino ti ayan iti silud mo?” (Hadēs g86)
“Iwe imfa, kupambana kwako kuli kuti? Iwe imfa, ululu wako uli kuti?” (Hadēs g86)
56 Ti silud iti patay ket basol ken ti pannakabalin iti basol ket ti linteg.
Ululu wa imfa ndi tchimo, ndipo mphamvu ya tchimo ndi lamulo.
57 Ngem agyamantayo iti Dios, nga isu ti mangmangted kadatayo iti balligi babaen iti Apotayo a ni Jesu-Cristo!
Koma tiyamike Mulungu amene amatipambanitsa mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
58 Ngarud kakabsatko, agbalinkayo a natibker ken agtalinaedkayo iti pinatiyo. Saysayaatenyo a kankanayon ti panagtrabahoyo maipaay iti Apo, gapu ta ammoyo a saan nga agbalin nga ubbaw dagiti trabahoyo iti Dios.
Choncho, abale anga okondedwa imani njii. Musasunthike ndi chilichonse. Nthawi zonse mudzipereke kwathunthu ku ntchito ya Ambuye, chifukwa mukudziwa kuti ntchito zanu mwa Ambuye sizili zopanda phindu.

< 1 Corinto 15 >