< תהילים 19 >

למנצח מזמור לדוד ב השמים מספרים כבוד-אל ומעשה ידיו מגיד הרקיע 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
יום ליום יביע אמר ולילה ללילה יחוה-דעת 2
Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
אין-אמר ואין דברים בלי נשמע קולם 3
Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
בכל-הארץ יצא קום ובקצה תבל מליהם לשמש שם-אהל בהם 4
Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
והוא--כחתן יצא מחפתו ישיש כגבור לרוץ ארח 5
Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
מקצה השמים מוצאו--ותקופתו על-קצותם ואין נסתר מחמתו 6
Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
תורת יהוה תמימה משיבת נפש עדות יהוה נאמנה מחכימת פתי 7
Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
פקודי יהוה ישרים משמחי-לב מצות יהוה ברה מאירת עינים 8
Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
יראת יהוה טהורה--עומדת לעד משפטי-יהוה אמת צדקו יחדו 9
Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
הנחמדים--מזהב ומפז רב ומתוקים מדבש ונפת צופים 10
ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
גם-עבדך נזהר בהם בשמרם עקב רב 11
Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
שגיאות מי-יבין מנסתרות נקני 12
Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
גם מזדים חשך עבדך-- אל-ימשלו-בי אז איתם ונקיתי מפשע רב 13
Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
יהיו לרצון אמרי-פי והגיון לבי לפניך יהוה צורי וגאלי 14
Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.

< תהילים 19 >