< תהילים 113 >

הללו-יה הללו עבדי יהוה הללו את-שם יהוה 1
Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
יהי שם יהוה מברך-- מעתה ועד-עולם 2
Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
ממזרח-שמש עד-מבואו-- מהלל שם יהוה 3
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
רם על-כל-גוים יהוה על השמים כבודו 4
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
מי כיהוה אלהינו-- המגביהי לשבת 5
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
המשפילי לראות-- בשמים ובארץ 6
amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
מקימי מעפר דל מאשפת ירים אביון 7
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
להושיבי עם-נדיבים עם נדיבי עמו 8
amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
מושיבי עקרת הבית-- אם-הבנים שמחה הללו-יה 9
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

< תהילים 113 >