< תהילים 108 >

שיר מזמור לדוד נכון לבי אלהים אשירה ואזמרה אף-כבודי 1
Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
עורה הנבל וכנור אעירה שחר 2
Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
אודך בעמים יהוה ואזמרך בלאמים 3
Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
כי-גדול מעל-שמים חסדך ועד-שחקים אמתך 4
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
רומה על-שמים אלהים ועל כל-הארץ כבודך 5
Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
למען יחלצון ידידיך הושיעה ימינך וענני 6
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
אלהים דבר בקדשו--אעלזה אחלקה שכם ועמק סכות אמדד 7
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
לי גלעד לי מנשה ואפרים מעוז ראשי יהודה מחקקי 8
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
מואב סיר רחצי--על-אדום אשליך נעלי עלי-פלשת אתרועע 9
Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
מי יבלני עיר מבצר מי נחני עד-אדום 10
Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
הלא-אלהים זנחתנו ולא-תצא אלהים בצבאתינו 11
Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
הבה-לנו עזרת מצר ושוא תשועת אדם 12
Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
באלהים נעשה-חיל והוא יבוס צרינו 13
Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.

< תהילים 108 >