< מִשְׁלֵי 27 >

אל-תתהלל ביום מחר כי לא-תדע מה-ילד יום 1
Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
יהללך זר ולא-פיך נכרי ואל-שפתיך 2
Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
כבד-אבן ונטל החול וכעס אויל כבד משניהם 3
Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
אכזריות חמה ושטף אף ומי יעמד לפני קנאה 4
Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
טובה תוכחת מגלה-- מאהבה מסתרת 5
Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
נאמנים פצעי אוהב ונעתרות נשיקות שונא 6
Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
נפש שבעה תבוס נפת ונפש רעבה כל-מר מתוק 7
Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
כצפור נודדת מן-קנה-- כן-איש נודד ממקומו 8
Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
שמן וקטרת ישמח-לב ומתק רעהו מעצת-נפש 9
Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
רעך ורעה (ורע) אביך אל-תעזב-- ובית אחיך אל-תבוא ביום אידך טוב שכן קרוב מאח רחוק 10
Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
חכם בני ושמח לבי ואשיבה חרפי דבר 11
Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
ערום ראה רעה נסתר פתאים עברו נענשו 12
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
קח-בגדו כי-ערב זר ובעד נכריה חבלהו 13
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
מברך רעהו בקול גדול--בבקר השכים קללה תחשב לו 14
Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
דלף טורד ביום סגריר ואשת מדונים (מדינים) נשתוה 15
Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
צפניה צפן-רוח ושמן ימינו יקרא 16
Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
ברזל בברזל יחד ואיש יחד פני-רעהו 17
Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
נצר תאנה יאכל פריה ושמר אדניו יכבד 18
Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
כמים הפנים לפנים-- כן לב-האדם לאדם 19
Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
שאול ואבדה לא תשבענה ועיני האדם לא תשבענה (Sheol h7585) 20
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
מצרף לכסף וכור לזהב ואיש לפי מהללו 21
Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
אם תכתוש-את-האויל במכתש בתוך הריפות-- בעלי לא-תסור מעליו אולתו 22
Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
ידע תדע פני צאנך שית לבך לעדרים 23
Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
כי לא לעולם חסן ואם-נזר לדור דור (ודור) 24
Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
גלה חציר ונראה-דשא ונאספו עשבות הרים 25
Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
כבשים ללבושך ומחיר שדה עתודים 26
ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
ודי חלב עזים--ללחמך ללחם ביתך וחיים לנערותיך 27
Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.

< מִשְׁלֵי 27 >