< איכה 3 >

אני הגבר ראה עני בשבט עברתו 1
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
אותי נהג וילך חשך ולא אור 2
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
אך בי ישב יהפך ידו כל היום 3
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
בלה בשרי ועורי שבר עצמותי 4
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
בנה עלי ויקף ראש ותלאה 5
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
במחשכים הושיבני כמתי עולם 6
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
גדר בעדי ולא אצא הכביד נחשתי 7
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
גם כי אזעק ואשוע שתם תפלתי 8
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
גדר דרכי בגזית נתיבתי עוה 9
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
דב ארב הוא לי אריה (ארי) במסתרים 10
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
דרכי סורר ויפשחני שמני שמם 11
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
דרך קשתו ויציבני כמטרא לחץ 12
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
הביא בכליתי בני אשפתו 13
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
הייתי שחק לכל עמי נגינתם כל היום 14
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
השביעני במרורים הרוני לענה 15
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
ויגרס בחצץ שני הכפישני באפר 16
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
ותזנח משלום נפשי נשיתי טובה 17
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
ואמר אבד נצחי ותוחלתי מיהוה 18
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
זכר עניי ומרודי לענה וראש 19
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
זכור תזכור ותשיח (ותשוח) עלי נפשי 20
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
זאת אשיב אל לבי על כן אוחיל 21
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
חסדי יהוה כי לא תמנו כי לא כלו רחמיו 22
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
חדשים לבקרים רבה אמונתך 23
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
חלקי יהוה אמרה נפשי על כן אוחיל לו 24
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
טוב יהוה לקוו לנפש תדרשנו 25
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
טוב ויחיל ודומם לתשועת יהוה 26
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
טוב לגבר כי ישא על בנעוריו 27
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
ישב בדד וידם כי נטל עליו 28
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
יתן בעפר פיהו אולי יש תקוה 29
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
יתן למכהו לחי ישבע בחרפה 30
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
כי לא יזנח לעולם אדני 31
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
כי אם הוגה ורחם כרב חסדיו 32
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
כי לא ענה מלבו ויגה בני איש 33
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
לדכא תחת רגליו כל אסירי ארץ 34
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
להטות משפט גבר נגד פני עליון 35
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
לעות אדם בריבו אדני לא ראה 36
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
מי זה אמר ותהי אדני לא צוה 37
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
מפי עליון לא תצא הרעות והטוב 38
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
מה יתאונן אדם חי גבר על חטאו 39
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
נחפשה דרכינו ונחקרה ונשובה עד יהוה 40
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
נשא לבבנו אל כפים אל אל בשמים 41
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
נחנו פשענו ומרינו אתה לא סלחת 42
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
סכותה באף ותרדפנו הרגת לא חמלת 43
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
סכותה בענן לך מעבור תפלה 44
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
סחי ומאוס תשימנו בקרב העמים 45
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
פצו עלינו פיהם כל איבינו 46
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
פחד ופחת היה לנו השאת והשבר 47
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
פלגי מים תרד עיני על שבר בת עמי 48
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
עיני נגרה ולא תדמה מאין הפגות 49
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
עד ישקיף וירא יהוה משמים 50
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
עיני עוללה לנפשי מכל בנות עירי 51
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
צוד צדוני כצפור איבי חנם 52
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
צמתו בבור חיי וידו אבן בי 53
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
צפו מים על ראשי אמרתי נגזרתי 54
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
קראתי שמך יהוה מבור תחתיות 55
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
קולי שמעת אל תעלם אזנך לרוחתי לשועתי 56
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
קרבת ביום אקראך אמרת אל תירא 57
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
רבת אדני ריבי נפשי גאלת חיי 58
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
ראיתה יהוה עותתי שפטה משפטי 59
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
ראיתה כל נקמתם--כל מחשבתם לי 60
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
שמעת חרפתם יהוה כל מחשבתם עלי 61
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
שפתי קמי והגיונם עלי כל היום 62
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
שבתם וקימתם הביטה אני מנגינתם 63
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
תשיב להם גמול יהוה כמעשה ידיהם 64
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
תתן להם מגנת לב תאלתך להם 65
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
תרדף באף ותשמידם מתחת שמי יהוה 66
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.

< איכה 3 >