< איוב 31 >
ברית כרתי לעיני ומה אתבונן על-בתולה | 1 |
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
ומה חלק אלוה ממעל ונחלת שדי ממרמים | 2 |
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
הלא-איד לעול ונכר לפעלי און | 3 |
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
הלא-הוא יראה דרכי וכל-צעדי יספור | 4 |
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
אם-הלכתי עם-שוא ותחש על-מרמה רגלי | 5 |
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
ישקלני במאזני-צדק וידע אלוה תמתי | 6 |
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
אם תטה אשרי מני הדרך ואחר עיני הלך לבי ובכפי דבק מאום | 7 |
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
אזרעה ואחר יאכל וצאצאי ישרשו | 8 |
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
אם-נפתה לבי על-אשה ועל-פתח רעי ארבתי | 9 |
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
תטחן לאחר אשתי ועליה יכרעון אחרין | 10 |
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
כי-הוא (היא) זמה והיא (והוא) עון פלילים | 11 |
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
כי אש היא עד-אבדון תאכל ובכל-תבואתי תשרש | 12 |
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
אם-אמאס--משפט עבדי ואמתי ברבם עמדי | 13 |
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
ומה אעשה כי-יקום אל וכי-יפקד מה אשיבנו | 14 |
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
הלא-בבטן עשני עשהו ויכננו ברחם אחד | 15 |
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
אם-אמנע מחפץ דלים ועיני אלמנה אכלה | 16 |
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
ואכל פתי לבדי ולא-אכל יתום ממנה | 17 |
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
כי מנעורי גדלני כאב ומבטן אמי אנחנה | 18 |
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
אם-אראה אובד מבלי לבוש ואין כסות לאביון | 19 |
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
אם-לא ברכוני חלצו ומגז כבשי יתחמם | 20 |
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
אם-הניפותי על-יתום ידי כי-אראה בשער עזרתי | 21 |
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
כתפי משכמה תפול ואזרעי מקנה תשבר | 22 |
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
כי פחד אלי איד אל ומשאתו לא אוכל | 23 |
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
אם-שמתי זהב כסלי ולכתם אמרתי מבטחי | 24 |
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
אם-אשמח כי-רב חילי וכי-כביר מצאה ידי | 25 |
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
אם-אראה אור כי יהל וירח יקר הלך | 26 |
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
ויפת בסתר לבי ותשק ידי לפי | 27 |
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
גם-הוא עון פלילי כי-כחשתי לאל ממעל | 28 |
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
אם-אשמח בפיד משנאי והתעררתי כי-מצאו רע | 29 |
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
ולא-נתתי לחטא חכי-- לשאל באלה נפשו | 30 |
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
אם-לא אמרו מתי אהלי מי-יתן מבשרו לא נשבע | 31 |
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
בחוץ לא-ילין גר דלתי לארח אפתח | 32 |
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
אם-כסיתי כאדם פשעי-- לטמון בחבי עוני | 33 |
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
כי אערוץ המון רבה-- ובוז-משפחות יחתני ואדם לא-אצא פתח | 34 |
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
מי יתן-לי שמע לי-- הן-תוי שדי יענני וספר כתב איש ריבי | 35 |
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
אם-לא על-שכמי אשאנו אענדנו עטרות לי | 36 |
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
מספר צעדי אגידנו כמו-נגיד אקרבנו | 37 |
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
אם-עלי אדמתי תזעק ויחד תלמיה יבכיון | 38 |
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
אם-כחה אכלתי בלי-כסף ונפש בעליה הפחתי | 39 |
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
תחת חטה יצא חוח--ותחת-שערה באשה תמו דברי איוב | 40 |
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.