< שמואל ב 22 >

וידבר דוד ליהוה את דברי השירה הזאת ביום הציל יהוה אתו מכף כל איביו ומכף שאול 1
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
ויאמר יהוה סלעי ומצדתי ומפלטי לי 2
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
אלהי צורי אחסה בו מגני וקרן ישעי משגבי ומנוסי משעי מחמס תשעני 3
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
מהלל אקרא יהוה ומאיבי אושע 4
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
כי אפפני משברי מות נחלי בליעל יבעתני 5
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
חבלי שאול סבני קדמני מקשי מות (Sheol h7585) 6
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
בצר לי אקרא יהוה ואל אלהי אקרא וישמע מהיכלו קולי ושועתי באזניו 7
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
ותגעש (ויתגעש) ותרעש הארץ מוסדות השמים ירגזו ויתגעשו כי חרה לו 8
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
עלה עשן באפו ואש מפיו תאכל גחלים בערו ממנו 9
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
ויט שמים וירד וערפל תחת רגליו 10
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
וירכב על כרוב ויעף וירא על כנפי רוח 11
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
וישת חשך סביבתיו סכות חשרת מים עבי שחקים 12
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
מנגה נגדו בערו גחלי אש 13
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
ירעם מן שמים יהוה ועליון יתן קולו 14
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
וישלח חצים ויפיצם ברק ויהמם (ויהם) 15
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
ויראו אפקי ים יגלו מסדות תבל בגערת יהוה מנשמת רוח אפו 16
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
ישלח ממרום יקחני ימשני ממים רבים 17
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
יצילני מאיבי עז משנאי כי אמצו ממני 18
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
יקדמני ביום אידי ויהי יהוה משען לי 19
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
ויצא למרחב אתי יחלצני כי חפץ בי 20
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
יגמלני יהוה כצדקתי כבר ידי ישיב לי 21
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
כי שמרתי דרכי יהוה ולא רשעתי מאלהי 22
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
כי כל משפטו לנגדי וחקתיו לא אסור ממנה 23
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
ואהיה תמים לו ואשתמרה מעוני 24
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
וישב יהוה לי כצדקתי כברי לנגד עיניו 25
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
עם חסיד תתחסד עם גבור תמים תתמם 26
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
עם נבר תתבר ועם עקש תתפל 27
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
ואת עם עני תושיע ועיניך על רמים תשפיל 28
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
כי אתה נירי יהוה ויהוה יגיה חשכי 29
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
כי בכה ארוץ גדוד באלהי אדלג שור 30
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
האל תמים דרכו אמרת יהוה צרופה-- מגן הוא לכל החסים בו 31
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
כי מי אל מבלעדי יהוה ומי צור מבלעדי אלהינו 32
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
האל מעוזי חיל ויתר תמים דרכו (דרכי) 33
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
משוה רגליו (רגלי) כאילות ועל במתי יעמדני 34
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
מלמד ידי למלחמה ונחת קשת נחושה זרעתי 35
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
ותתן לי מגן ישעך וענתך תרבני 36
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
תרחיב צעדי תחתני ולא מעדו קרסלי 37
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
ארדפה איבי ואשמידם ולא אשוב עד כלותם 38
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
ואכלם ואמחצם ולא יקומון ויפלו תחת רגלי 39
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
ותזרני חיל למלחמה תכריע קמי תחתני 40
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
ואיבי תתה לי ערף משנאי ואצמיתם 41
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
ישעו ואין משיע אל יהוה ולא ענם 42
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
ואשחקם כעפר ארץ כטיט חוצות אדקם ארקעם 43
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
ותפלטני מריבי עמי תשמרני לראש גוים עם לא ידעתי יעבדני 44
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
בני נכר יתכחשו לי לשמוע אזן ישמעו לי 45
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
בני נכר יבלו ויחגרו ממסגרותם 46
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
חי יהוה וברוך צורי וירם אלהי צור ישעי 47
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
האל הנתן נקמת לי ומריד עמים תחתני 48
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
ומוציאי מאיבי ומקמי תרוממני מאיש חמסים תצילני 49
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
על כן אודך יהוה בגוים ולשמך אזמר 50
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
מגדיל (מגדול) ישועות מלכו ועשה חסד למשיחו לדוד ולזרעו עד עולם 51
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”

< שמואל ב 22 >