< Isaia 45 >

1 PENEI o Iehova i olelo mai ai no kona mea i poniia, No Kuro, nona ka lima akau a'u i hooikaika ai, E hoopio i na lahuikanaka imua ona; A e kala no hoi au i ko na puhaka o na'lii, I hamama na puka imua ona, Aole hoi e paniia na pukapa.
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 E hele no wau imua ou, a e hoolaumania i na wahi apuupuu, E wawahi no au i na pani puka keleawe, A e uhaki ia'u na kaola hao.
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 E haawi aku no au ia oe i ka waiwai o ka pouli, A me ka ukana i hunaia ma kahi nalowale, I ike ai oe, owau no Iehova, ka mea i hea aku ia oe ma ka inoa, Ke Akua hoi o ka Iseraela.
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 No ka'u kauwa, no Iakoba, No ka Iseraela hoi, ka mea a'u i wae ai, Ua hea aku no au ia oe; Ma kou inoa ua hea aku au ia oe, Aole nae oe i ike mai ia'u.
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 Owau no Iehova, aohe mea e ae, Aohe Akua e ae, ke kaawale au; Na'u no e kaei aku ia oe, aole nae oe i ike mai ia'u;
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 I ike lakou, mai ka puka ana a ka la mai, A mai ke komohana mai hoi, Aohe mea e ae, ke kaawale au; Owau no o Iehova, aohe mea e ae.
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 Ka mea nana i hana ka malamalama, A nana hoi i hana ka pouli, Nana i hana ka pomaikai, Nana hoi i hana ka poino, Owau no Iehova, ka mea nana e hana keia mau mea a pau.
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 E hoonakulukulu oukou, e na lani, mai luna mai, E hanini hoi na aouli i ka pono; E hamama hoi ka honua, a e hua mai i ke ola, E ulu pu mai no me ka pono; Na'u, na Iehova ia i hana.
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Auwe ke kanaka paio aku i kona mea nana ia i hana? Na mea lepo me na mea lepo o ka honua! E olelo anei ka lepokiaha, i ka mea nana ia e hooponopono, Heaha kau e hana nei? A o ka mea au i hana'i, Aole ona lima?
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 Auwe ka mea olelo i ka makuakane, Heaha kau e hoohanau ai? A i ka makuwahine hoi, Ua hanau oe i ke aha?
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Ke olelo mai nei o Iehova, ka Mea Hemolele o ka Iseraela, penei, O ka Mea hoi nana ia i hana, E ninau mai oukou ia'u i na mea e hiki mai ana no ka'u mau keiki, A e kauoha mai oukou ia'u ma ka hana a kuu mau lima.
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 Na'u no i hana ka honua nei, A hana no hoi au i na kanaka maluna iho; Na kuu mau lima no i hohola aku i na lani, A na'u hoi i kauoha aku i ko lakou lehulehu a pau.
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 Ua hoala no au ia ia, no ka pono, Na'u no e hoopololei i kona mau aoao, Nana no e hana i ko'u kulanakauhale, A nana no e hookuu aku i ko'u poe pio; Aole no ka uku, a me ka waiwai kipe, Wahi a Iehova o na kaua.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Ke i mai nei o Iehova penei, E hele mai no ianei, iou la, Ka waiwai o Aigupita, a me ka mea kuai o Aitiopa, A me ko Seba, ka poe kanaka nunui, a e lilo lakou nou. E hahai no lakou ia oe; me ka paa ana i na kaula hao lakou e hele mai ai, A e moe no lakou ilalo imua ou, E nonoi aku no lakou ia oe, me ka olelo iho, He oiaio no, me oe no ke Akua, aohe Akua e ae.
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 He oiaio no, o ke Akua no oe nana i huna ia oe iho, E ke Akua o ka Iseraela, ka mea e ola'i.
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 Ua hilahila, a ua hoopalaimaka lakou a pau; Holo pu no iloko o ka hilahila, ka poe hana akuakii.
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 E hoolaia no o ka Iseraela maloko o Iehova, me ke ola mau loa; Aole oukou e hilahila, aole hoi e hoopalaimaka, ia ao aku, ia ao aku.
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 No ka mea, penei ka olelo ana mai a Iehova, Ka mea nana i hana na lani; Oia ke Akua, ka mea nana i hana ka honua, a kukulu hoi, Ka mea nana ia i hoopaa, aole hoi ia i hana makehewa ia mea, Hana no oia ia i wahi e nohoia'i; Owau no Iehova, aohe mea e ae,
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 Aole au i olelo ma kahi malu, ma kahi pouli o ka honua; Aole au i olelo aku i na pua a Iakoba, E imi makehewa oukou ia'u. Owau o Iehova, ka mea e olelo ana ma ka pono, Ka mea e hai. aku ana i na mea pololei.
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 E hoakoakoa oukou, a hele mai, E houluulu pu oukou, e ka poe i pakele o na aina. He poe ike ole ka poe kukulu i ka laau o ko lakou akua kalaiia, A pule aku i ke akua hiki ole ke hoola.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 E hai aku, e lawe mai hoi ia lakou; Oia, e kukakuka pa lakou. Nawai i hai i keia, mai kahiko mai, A hoikeike hoi ia, mai kela wa mai? Aole anei owau. o Iehova? Aole hoi he Akua e ae, ke Kaawale au; O ke Akua pono, ka mea e ola'i, aohe mea e ae.
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 E haliu mai oukou ia'u a e hoolaia no oukou, E na kukulu o ka honua; No ka mea, owau no ke Akua, aohe mea e ae.
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 Ua hoohiki au ia'u iho, Ua puka aku hoi ka olelo, mai ko'u waha aku ma ka pono, Aole ia i hoi hou, no ka mea, la'u no e kukuli ai na kuli a pau, a e hoohiki no hoi na elelo a pau.
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 He oiaio, e olelo mai ia'u, maloko o Iehova na mea pono, a me ka ikaika, Ia ia no lakou e hele mai ai; A e hilahila auanei ka poe a pau i inaina aku ia ia.
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 Maloko o Iehova e hoaponoia'i na pua a pau o ka Iseraela, A malaila hoi e hoonani ai.
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

< Isaia 45 >