< II Samuela 1 >

1 MAHOPE iho o ka make ana o Saula, a ua hoi hou mai o Davida mai ka luku ana i ka Amaleka, a noho iho o Davida elua la i Zikelaga;
Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
2 A i ke kolu o ka la, aia hoi, he kanaka i hele mai, mai ke kahua kaua, mai Saula mai, me kona kapa i haehaeia, a me ka lepo maluna o kona poo; a hiki aku la ia io Davida la, moe iho la ia ma ka honua, a hoomaikai aku la.
Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
3 I aku la o Davida ia ia, Mai hea mai oe i hele mai nei? I mai la kela ia ia, Ua pakele mai nei au mai ke kahua kaua mai o ka Iseraela.
Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
4 I aku la o Davida ia ia, Pehea kela mea? Ke noi aku nei au ia oe, e hai mai ia'u. I mai la kela, Ua hee aku la na kanaka mai ke kaua aku, a ua haule na kanaka he nui loa a make: ua make hoi o Saula a me kana keikikane o Ionatana.
Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
5 I aku la o Davida i ke kanaka opiopio nana i hai mai ia ia, Pehea kau ike ana, ua make o Saula a me Ionatana kana keiki?
Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
6 I mai la ua kanaka opiopio la nana i hai mai ia ia, A i ko'u hiki wale ana aku maluna o ka puu o Gileboa, aia hoi, e kalele ana o Saula maluna iho o kona ihe; a hahai ikaika mai la na halekaa a me na hoohololio mahope ona.
Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
7 Alawa ae la ia i hope, ike mai la ia'u, a kahea mai la ia'u: i aku la au, Eia no wau.
Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
8 Ninau mai kela ia'u, Owai oe? Olelo aku la au, He Amaleka wau.
Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
9 I hou mai la ia ia'u, Ke noi aku nei au ia oe, e ku oe maluna iho o'u, a e pepehi mai ia'u; no ka mea, ke kau mai nei ka poniuniu maluna iho o'u, a ke koe nei ke ola okoa iloko o'u.
“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
10 A ku iho la au maluna ona, a pepehi iho la ia ia; no ka mea, ua ike pono au, aole ia e ola mahope iho o kona haule ana: lawe ae la no au i ka papale alii maluna o kona poo, a me ke kupee ma kona lima, a ua halihali mai nei au ia mau mea i kuu haku.
“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
11 Alaila, lalau iho la o Davida i kona kapa, a haehae iho la, a pela no hoi na kanaka a pau me ia.
Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
12 Kanikau aku la lakou me ka uwe aku, a hookeai iho la lakou a hiki i ke ahiahi, no Saula a no Ionatana kana keiki, a no ka poe kanaka o Iehova, a no ka ohana a Iseraela; no ka mea, ua haule lakou i ka pahikaua.
Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
13 Ninau aku la o Davida i ke kanaka opiopio nana i hai mai ia ia, Nohea oe? I mai la kela, He keiki au na kekahi malihini, he Amaleka.
Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
14 I aku la o Davida ia ia, Heaha kou mea i makau ole ai i ka o aku i kou lima e pepehi i ka Iehova mea i poniia?
Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
15 Kahea aku la o Davida i kekahi kanaka opiopio, i aku la, E neenee aku oe, a e lele aku maluna ona. Pepehi aku la kela ia ia, a make iho la ia.
Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
16 I aku la o Davida ia ia, Maluna o kou poo iho ke koko ou: no ka mea, ua ahewa mai la kou waha iho ia oe, i ka i ana, Ua pepehi no au i ka Iehova mea i poniia.
Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
17 Kanikau aku la o Davida i keia kanikau ana ia Saula a ia Ionatana kana keiki.
Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
18 (Kauoha aku la hoi ia e ao i na mamo a Iuda i ke kakaka: aia hoi ua kakauia maloko o ka buke a Iasera.)
Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
19 O ka nani o ka Iseraela, ua pepehiia oia maluna o na wahi kiekie ou; Kai ka haule ana o ka poe ikaika?
“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
20 Mai hai aku ia mea ma Gata, Mai kala aku hoi ia ma na alanui o Asekelona; O hauoli na kaikamahine a ka poe Pilisetia, O haanui hoi na kaikamahine a ka poe okipoepoe ole ia.
“Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
21 E na puu o Gileboa, aole make hau, Aole hoi he ua maluna iho o oukou; Aole hoi na mahinaai o na hua mua: Ilaila kahi i hooleiia'ku ai ka palekaua o ka mea ikaika, Ka palekaua o Saula i poni ole ia i ka aila.
“Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
22 Mai ke koko ae o ka poe i make, A mai ka momona ae o ka poe ikaika, Aole i hoi ihope ke kakaka o Ionatana, Aole hoi i hoi nele mai ka pahikaua a Saula.
“Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
23 Ua aloha no, a ua oluolu hoi o Saula a o Ionatana i ko laua ola ana, A i ko laua make ana, aole laua i hookaawaleia. Ua oi aku ko laua mama i ko na aeto, A me ko laua ikaika i ko na liona.
“Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
24 E na kaikamahine o ka Iseraela, e kanikau aku oukou ia Saula, Nana oukou i hoaahu aku i ke kapa ula, a me na mea nani: Nana i hoonani i ko oukou kapa i ke gula.
“Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
25 Kai ka haule ana o ka poe ikaika iwaena o ke kaua ana! E Ionatana, ua pepehiia oe maluna o na wahi kiekie ou.
“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 Ua ehaeha loa au nou, e kuu hoahanau, e Ionatana: He oluolu loa oe ia'u, he kupanaha kou aloha ia'u, E oi mai ana i ke aloha o na wahine.
Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
27 Kai ka haule ana o ka poe ikaika, A me ka pau ana o na mea kaua!
“Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”

< II Samuela 1 >