< II Na Lii 21 >

1 HE umikumamalua na makahiki o Manase, i kona wa i lilo ai i alii, a he kanalimakumamalima na makahiki ana i alii ai ma Ierusalema, A o Hepeziba ka inoa o kona makuwahine.
Manase anakhala mfumu ali ndi zaka khumi ndi ziwiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 55. Amayi ake anali Hefiziba.
2 A hana ino aku la ia imua o Iehova, e like me na mea haumia o na lahuikanaka a Iehova i kipaku ae mai ke alo aku o na mamo a Iseraela.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira mchitidwe wonyansa wa mitundu imene Yehova anayipirikitsa pofika Aisraeli.
3 A hana hou aku la ia i na heiau a Hezekia a kona makuakane i wawahi ai; a kukulu iho la ia i na kuahu no Baala, a hana hoi i kii o Aseterota, e like me ka hana a Ahaba, ke alii o ka Iseraela; a hoomana aku la i na puali a pau o ka lani, a malama ia lakou.
Iyetu anamanganso malo opembedzera mafano amene Hezekiya abambo ake anawawononga. Anamangira Baala maguwa a nsembe ndi mtengo wa fano la Asera monga anachitira Ahabu mfumu ya Israeli ndipo ankapembedza zolengedwa zonse zamlengalenga.
4 A hana aku la ia i na kuahu iloko o ka hale o Iehova, kahi a Iehova i i mai ai, Ma Ierusalema e waiho ai au i ko'u inoa.
Anamanga maguwa ansembewa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Mu Yerusalemu ndidzayikamo Dzina langa.”
5 Hana aku la hoi ia i na kuahu no na puali a pau o ka lani ma na pahale elua o ka hale o Iehova.
Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova, Manase anamangamo maguwa opembedzerapo zinthu zamlengalenga.
6 A kaumaha aku la ia i kana keikikane i ke ahi, a nana i ke ao, a hookilokilo, a ninau i na uhane ino, a i na kupua; ua nui kana hana hewa ana imua o Iehova e hoonaukiuki ia ia.
Iye anapsereza mwana wake pa moto ngati nsembe, ankachita za matsenga, ankawombeza mawula, ankapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndiponso ankapembedza mizimu. Iyeyo anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova ndipo anakwiyitsa Yehovayo.
7 A kukulu iho la no ia i kii kalaiia no Aseterota, ka mea ana i hana'i, ma ka hale, kahi a Iehova i i mai ai ia Davida a ia Solomona kana keiki, Ma keia hale, a ma Ierusalema, ka mea a'u i wae ai mailoko mai o na ohana a pau o ka Iseraela, e waiho mau loa ai au i ko'u inoa:
Iye anatenga fano losema la Asera limene analipanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Yehova, Nyumba imene Yehova ananena kwa Davide ndi mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba iyi ndi mu Yerusalemu ndiwo malo amene ndasankha pakati pa mafuko onse a Aisraeli kuyikamo Dzina langa kwamuyaya.
8 Aole hoi au e hoonee hou aku i ka wawae o ka Iseraela mai ka aina aku a'u i haawi aku ai i ko lakou poe kupuna, ke makaala io lakou e hana, e like me na mea a pau a'u i kauoha aku ai ia lakou, a me ke kanawai a pau a Mose ka'u kauwa i kauoha aku ai ia lakou.
Sindidzalola kuti Aisraeli achotsedwe mʼdziko lawo limene ndinapatsa makolo awo ngati iwowo adzasamala kuchita zinthu zonse zimene ndinawalamula ndi kusunga malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anawapatsa.”
9 Aole hoi lakou i lohe; aka, hoowalewale ae la o Manase ia lakou e hookela aku i ka hana hewa ana mamua o ko na lahuikanaka a Iehova i luku ai imua o ka poe mamo a Iseraela.
Koma anthu sanamvere. Manase anawasocheretsa, kotero kuti anachita zoyipa zambiri kupambana anthu a mitundu ina amene Yehova anawawononga pamene Aisraeli ankafika.
10 A olelo mai o Iehova ma kana poe kauwa ma na kaula, i mai la,
Yehova anayankhula kudzera mwa atumiki ake, aneneri kuti,
11 No ka mea, ua hana aku o Manase i keia mau mea haumia, i ka hewa oi aku imua o na mea a pau a ka Amora i hana'i mamua ona, a ua hoolilo i ka Iuda i ka hewa ma kona mau kii;
“Manase mfumu ya Yuda wachita machimo onyansawa ndipo wachita zoyipa kupambana Aamori amene analipo kale iye asanabadwe ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda ndi mafano ake.
12 No ia mea, ke olelo mai nei o Iehova ke Akua o ka Iseraela, Aia hoi, e lawe mai ana au i ka ino maluna o Ierusalema, a o ka Iuda, i ka mea e kani ai na pepeiao elua o na mea a pau i lohe.
Choncho Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taonani, ndikubweretsa pa Yerusalemu ndi Yuda mavuto akuti aliyense amene adzawamve adzathedwa nzeru.
13 A e kau aku au maluna o Ierusalema i ke kaulaana o Samaria, a me ka mea kaupaona o ko ka hale o Ahaba; a e holoi maloo aku au ia Ierusalema, e like me ka mea nana e holoi maloo ke kiaha, holoi no ia, a huli ia ia ilalo ke alo.
Ndidzalanga Yerusalemu ndi Yuda pogwiritsa ntchito muyeso umene ndinalangira Samariya ndi Ahabu pamodzi ndi nyumba yake. Ndidzayeretsa Yerusalemu monga mmene munthu amachitira popukuta mbale ndipo atayipukuta amayivundikira pansi.
14 A e haalele au i ke koena o ko'u hooilina, a e haawi aku au ia lakou iloko o ka lima o ko lakou poe enemi; a e lilo lakou i poe pio, a i waiwai pio no ko lakou poe enemi;
Ndidzawataya anthu otsala amene ndi cholowa changa ndipo ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo. Adzachotsedwa ndipo adaniwo adzawalanda zinthu zonse
15 No ka mea, ua hana hewa lakou imua o'u, a ua hoonaukiuki lakou ia'u mai ka manawa mai a ko lakou poe kupuna i puka ae mai Aigupita mai a hiki i keia wa.
chifukwa anachita zoyipa pamaso panga ndipo akhala akundikwiyitsa kuchokera tsiku limene makolo awo anatuluka mu Igupto mpaka lero lino.’”
16 I hookahe ae la o Manase i ke koko hala ole he nui loa, a hoopiha iho la oia ia Ierusalema mai kela aoao a hiki i keia aoao; he okoa kona hewa, o ka hoolilo ana i ka Iuda i ka hewa e hana hewa imua o Iehova.
Kuwonjezera apo, Manase anakhetsa kwambiri magazi a anthu osalakwa mpaka magaziwo kuyenderera mu Yerusalemu kuyambira mbali ina mpaka mbali ina, kuphatikiza pa kuchimwitsa Yuda, kotero kuti anthu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
17 A o na hana i koe a Manase, a o na mea a pau ana i hana'i, a o kona hewa ana i hewa'i, aole anei i kakauia lakou iloko o ka buke oihanaalii a na'lii o ka Iuda?
Ntchito zina za Manase ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
18 A hiamoe iho la o Manase me kona poe kupuna, a kanuia oia ma ke kihapai o kona hale, ma ke kihapai o Uza: a noho alii iho la o Amona kana keiki ma kona hakahaka.
Manase anagona ndi makolo ake ndipo anayikidwa mʼmanda mʼmunda wa Uza, ku nyumba yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
19 He iwakaluakumamalua na makahiki o Amona i kona wa i lilo ai i alii: a elua makahiki o kona noho alii ana ma Ierusalema. A o Mesulemeta ka inoa o kona makuwahine. ke kaikamahine a Haruza no Ioteba.
Amoni anakhala mfumu ali ndi zaka 22 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka ziwiri. Amayi ake anali Mesulemeti mwana wa Haruzi, wochokera ku Yotiba.
20 A hana ino aku la ia imua o Iehova e like me ka Manase, ka kona makuakane i hana'i.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Manase abambo ake.
21 A hele aku ia ma na aoao a pau a kona makuakane i hele ai, a malama aku i na kii a kona makuakane i malama'i, a hoomana aku la ia lakou.
Anatsatira makhalidwe onse a abambo ake. Ankapembedza mafano amene abambo akewo ankawapembedza ndipo ankawagwadira.
22 Haalele no oia ia Iehova ke Akua o kona poe kupuna, aole ia i hele ma ka aoao o Iehova.
Iyeyo anasiya Yehova Mulungu wa makolo ake ndipo sanayende mʼnjira ya Yehova.
23 A kipi ae la na kauwa a Amona ia ia, a pepehi iho la i ke alii maloko o kona hale iho.
Nduna za Amoni zinamuchita chiwembu ndipo zinamupha mʼnyumba yake.
24 A pepehi aku la na kanaka o ka aina i ka poe a pau i kipi i ke alii ia Amona; a hooalii aku la na kanaka o ka aina ia Iosia kana keiki ma kona hakahaka.
Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anachitira chiwembu Mfumu Amoni, nayika Yosiya mwana wake kukhala mfumu mʼmalo mwake.
25 A o na mea i koe a Amona i hana'i, aole anei i kakania lakou iloko o ka buke oihanaalii a na'lii o ka Iuda?
Ntchito zina za Amoni ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
26 A kanu lakou ia ia iloko o kona halelua iho ma ke kihapai o Uza; a noho alii iho la o Iosia kana keiki ma kona hakahaka.
Iye anayikidwa mʼmanda ake mʼmunda wa Uza. Ndipo Yosiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< II Na Lii 21 >