< Κατα Λουκαν 12 >

1 εν οισ επισυναχθεισων των μυριαδων του οχλου ωστε καταπατειν αλληλουσ ηρξατο λεγειν προσ τουσ μαθητασ αυτου πρωτον προσεχετε εαυτοισ απο τησ ζυμησ των φαρισαιων ητισ εστιν υποκρισισ
Nthawi yomweyo, anthu miyandamiyanda atasonkhana, ndi kumapondanapondana, Yesu anayamba kuyankhula poyamba kwa ophunzira ake, nati, “Chenjereni ndi yisiti wa Afarisi, amene ndi chinyengo.
2 ουδεν δε συγκεκαλυμμενον εστιν ο ουκ αποκαλυφθησεται και κρυπτον ο ου γνωσθησεται
Palibe chinthu chophimbika chimene sichidzawululika, kapena chobisika chimene sichidzadziwika.
3 ανθ ων οσα εν τη σκοτια ειπατε εν τω φωτι ακουσθησεται και ο προσ το ουσ ελαλησατε εν τοισ ταμειοισ κηρυχθησεται επι των δωματων
Chimene mwanena mu mdima chidzamveka dzuwa likuwala, ndipo zimene mwanongʼona mʼkhutu mʼchipinda chamʼkati, zidzayankhulidwa pa denga la nyumba.
4 λεγω δε υμιν τοισ φιλοισ μου μη φοβηθητε απο των αποκτενοντων το σωμα και μετα ταυτα μη εχοντων περισσοτερον τι ποιησαι
“Ine ndikuwuzani, abwenzi anga, musachite mantha ndi amene amapha thupi chifukwa akatero sangachitenso kanthu.
5 υποδειξω δε υμιν τινα φοβηθητε φοβηθητε τον μετα το αποκτειναι εξουσιαν εχοντα εμβαλειν εισ την γεενναν ναι λεγω υμιν τουτον φοβηθητε (Geenna g1067)
Koma Ine ndidzakuonetsani amene muyenera kumuopa: Wopani Iye, amene pambuyo pakupha thupi, ali ndi mphamvu yakukuponyani ku gehena. Inde, Ine ndikuwuzani, muopeni Iye. (Geenna g1067)
6 ουχι πεντε στρουθια πωλειται ασσαριων δυο και εν εξ αυτων ουκ εστιν επιλελησμενον ενωπιον του θεου
Kodi atimba asanu samagulidwa ndi ndalama ziwiri? Ngakhale zili chomwecho palibe imodzi ya izo imene imayiwalika ndi Mulungu.
7 αλλα και αι τριχεσ τησ κεφαλησ υμων πασαι ηριθμηνται μη ουν φοβεισθε πολλων στρουθιων διαφερετε
Ndithudi, tsitsi lonse la mʼmutu mwanu ndi lowerengedwa. Musachite mantha; inu ndi oposa kwambiri mpheta zambiri.
8 λεγω δε υμιν πασ οσ αν ομολογηση εν εμοι εμπροσθεν των ανθρωπων και ο υιοσ του ανθρωπου ομολογησει εν αυτω εμπροσθεν των αγγελων του θεου
“Ine ndikukuwuza kuti, aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Mwana wa Munthu adzamuvomerezanso pamaso pa angelo a Mulungu.
9 ο δε αρνησαμενοσ με ενωπιον των ανθρωπων απαρνηθησεται ενωπιον των αγγελων του θεου
Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu adzakanidwanso pamaso pa angelo a Mulungu.
10 και πασ οσ ερει λογον εισ τον υιον του ανθρωπου αφεθησεται αυτω τω δε εισ το αγιον πνευμα βλασφημησαντι ουκ αφεθησεται
Ndipo aliyense amene ayankhulira Mwana wa Munthu mawu oyipa adzakhululukidwa, koma iye wochitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa.
11 οταν δε προσφερωσιν υμασ επι τασ συναγωγασ και τασ αρχασ και τασ εξουσιασ μη μεριμνατε πωσ η τι απολογησησθε η τι ειπητε
“Akadzakutengerani ku masunagoge pamaso pa oweruza ndi a maulamuliro, musadere nkhawa mmene mudzadzitchinjirizire nokha kapena chimene mudzayankhule,
12 το γαρ αγιον πνευμα διδαξει υμασ εν αυτη τη ωρα α δει ειπειν
pakuti Mzimu Woyera nthawi imeneyo adzakuphunzitsani zoyenera kunena.”
13 ειπεν δε τισ αυτω εκ του οχλου διδασκαλε ειπε τω αδελφω μου μερισασθαι μετ εμου την κληρονομιαν
Munthu wina mʼgulu la anthu anati kwa Iye, “Aphunzitsi, muwuzeni mʼbale wanga andigawireko chuma chamasiye.”
14 ο δε ειπεν αυτω ανθρωπε τισ με κατεστησεν δικαστην η μεριστην εφ υμασ
Yesu anayankha kuti, “Munthu iwe, ndani anandiyika Ine kukhala woweruza kapena wogawa chuma pakati panu?”
15 ειπεν δε προσ αυτουσ ορατε και φυλασσεσθε απο τησ πλεονεξιασ οτι ουκ εν τω περισσευειν τινι η ζωη αυτω εστιν εκ των υπαρχοντων αυτου
Kenaka Iye anawawuza kuti, “Chenjerani! Khalani tcheru ndi makhalidwe onse adyera; moyo wa munthu sukhala chifukwa cha kuchuluka kwa zimene ali nazo.”
16 ειπεν δε παραβολην προσ αυτουσ λεγων ανθρωπου τινοσ πλουσιου ευφορησεν η χωρα
Ndipo Iye anawawuza fanizo ili, “Munda wa munthu wina wachuma unabereka kwambiri.
17 και διελογιζετο εν εαυτω λεγων τι ποιησω οτι ουκ εχω που συναξω τουσ καρπουσ μου
Iye anaganiza kuti, ‘Ndichite chiyani? Ndilibe malo osungiramo mbewu zanga.’
18 και ειπεν τουτο ποιησω καθελω μου τασ αποθηκασ και μειζονασ οικοδομησω και συναξω εκει παντα τα γενηματα μου και τα αγαθα μου
“Ndipo Iye anati, ichi ndi chimene ndidzachite: Ndidzaphwasula nkhokwe zanga zonse ndi kumanga zokulirapo, ndipo ndidzasungira mʼmenemo mbewu ndi katundu.
19 και ερω τη ψυχη μου ψυχη εχεισ πολλα αγαθα κειμενα εισ ετη πολλα αναπαυου φαγε πιε ευφραινου
Ndipo ndidzawuza moyo wanga kuti, ‘Uli nazo zinthu zabwino zambiri zimene zikhalepo zaka zambiri, usapupulume; idya, imwa ndi kukondwera.’”
20 ειπεν δε αυτω ο θεοσ αφρον ταυτη τη νυκτι την ψυχην σου απαιτουσιν απο σου α δε ητοιμασασ τινι εσται
“Koma Mulungu anati kwa iye, ‘Iwe wopusa! Usiku womwe uno moyo wako udzachotsedwa kwa iwe, ndipo ndi ndani amene adzatenge zimene iwe wadzikonzera?’
21 ουτωσ ο θησαυριζων εαυτω και μη εισ θεον πλουτων
“Umu ndi mmene zidzakhalire ndi aliyense amene amadziwunjikira chuma, koma si wachuma pamaso pa Mulungu.”
22 ειπεν δε προσ τουσ μαθητασ αυτου δια τουτο υμιν λεγω μη μεριμνατε τη ψυχη υμων τι φαγητε μηδε τω σωματι τι ενδυσησθε
Kenaka Yesu anati kwa ophunzira ake, “Choncho Ine ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu, zimene mudzadya; kapena za thupi lanu, zimene mudzavala.
23 η ψυχη πλειον εστιν τησ τροφησ και το σωμα του ενδυματοσ
Moyo uposa chakudya, ndi thupi liposa chovala.
24 κατανοησατε τουσ κορακασ οτι ου σπειρουσιν ουδε θεριζουσιν οισ ουκ εστιν ταμειον ουδε αποθηκη και ο θεοσ τρεφει αυτουσ ποσω μαλλον υμεισ διαφερετε των πετεινων
Taonani makwangwala: iwo safesa kapena kukolola, alibe nyumba zosungamo zinthu kapena nkhokwe; komabe, Mulungu amawadyetsa. Koposa kotani inu amene ndi ofunikira kuposa mbalame.
25 τισ δε εξ υμων μεριμνων δυναται προσθειναι επι την ηλικιαν αυτου πηχυν ενα
Ndi ndani wa inu akhoza kuwonjeza ora pa moyo wake chifukwa cha kudandaula?
26 ει ουν ουτε ελαχιστον δυνασθε τι περι των λοιπων μεριμνατε
Popeza simungathe kuchita kanthu kakangʼono aka, nʼchifukwa chiyani mumadandaula ndi zinazi?
27 κατανοησατε τα κρινα πωσ αυξανει ου κοπια ουδε νηθει λεγω δε υμιν ουδε σολομων εν παση τη δοξη αυτου περιεβαλετο ωσ εν τουτων
“Taonani mmene maluwa amakulira. Iwo sagwira ntchito kapena kusoka zovala. Koma Ine ndikuwuzani kuti, ngakhale Solomoni muulemelero wake wonse sanavalepo ngati limodzi la awa.
28 ει δε τον χορτον εν τω αγρω σημερον οντα και αυριον εισ κλιβανον βαλλομενον ο θεοσ ουτωσ αμφιεννυσιν ποσω μαλλον υμασ ολιγοπιστοι
Ngati umu ndi mmene Mulungu amavekera udzu wakuthengo, umene lero ulipo ndipo mawa uponyedwa pa moto, nanga Iye adzakuvekani inu motani. Haa! Inu achikhulupiriro chochepa!
29 και υμεισ μη ζητειτε τι φαγητε η τι πιητε και μη μετεωριζεσθε
Ndipo musayike mtima wanu pa zimene mudzadye kapena kumwa; musade nazo nkhawa.
30 ταυτα γαρ παντα τα εθνη του κοσμου επιζητει υμων δε ο πατηρ οιδεν οτι χρηζετε τουτων
Pakuti anthu akunja amathamanga kufunafuna zinthu zotere, ndipo Atate amadziwa kuti mumazifuna zimenezi.
31 πλην ζητειτε την βασιλειαν του θεου και ταυτα παντα προστεθησεται υμιν
Koma funafunani ufumu wake, ndipo mudzapatsidwa zonsezi.
32 μη φοβου το μικρον ποιμνιον οτι ευδοκησεν ο πατηρ υμων δουναι υμιν την βασιλειαν
“Musachite mantha, inu kagulu kankhosa, pakuti zinakondweretsa Atate anu kuti akupatseni ufumu.
33 πωλησατε τα υπαρχοντα υμων και δοτε ελεημοσυνην ποιησατε εαυτοισ βαλαντια μη παλαιουμενα θησαυρον ανεκλειπτον εν τοισ ουρανοισ οπου κλεπτησ ουκ εγγιζει ουδε σησ διαφθειρει
Gulitsani zonse zimene muli nazo, ndipo ndalama zake mupereke kwa osauka. Dzipezereni zikwama zandalama zimene sizidzatha, ndi kudzikundikira chuma chomwe sichidzatha kumwamba, kumene mbala sizingafikeko, ndipo dzimbiri silingawononge.
34 οπου γαρ εστιν ο θησαυροσ υμων εκει και η καρδια υμων εσται
Popeza kumene kuli chuma chanu, mtima wanunso udzakhala komweko.”
35 εστωσαν υμων αι οσφυεσ περιεζωσμεναι και οι λυχνοι καιομενοι
“Khalani okonzekeratu ndipo nyale zanu ziziyaka,
36 και υμεισ ομοιοι ανθρωποισ προσδεχομενοισ τον κυριον εαυτων ποτε αναλυση εκ των γαμων ινα ελθοντοσ και κρουσαντοσ ευθεωσ ανοιξωσιν αυτω
ngati anthu oyembekezera kubwera kwa mbuye wawo kuchokera kuphwando la ukwati, kuti pamene afika ndi kugogoda akhoza nthawi yomweyo kumutsekulira chitseko.
37 μακαριοι οι δουλοι εκεινοι ουσ ελθων ο κυριοσ ευρησει γρηγορουντασ αμην λεγω υμιν οτι περιζωσεται και ανακλινει αυτουσ και παρελθων διακονησει αυτοισ
Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo pobwera adzawapeze akudikira. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti adzakonzekera kuwatumikira, adzakhala nawo pa tebulo ndipo adzabwera ndi kuwatumikira.
38 και εαν ελθη εν τη δευτερα φυλακη και εν τη τριτη φυλακη ελθη και ευρη ουτωσ μακαριοι εισιν οι δουλοι εκεινοι
Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo adzawapeze ali okonzeka, ngakhale iye atabwera pa ora lachiwiri kapena lachitatu usiku.
39 τουτο δε γινωσκετε οτι ει ηδει ο οικοδεσποτησ ποια ωρα ο κλεπτησ ερχεται εγρηγορησεν αν και ουκ αν αφηκεν διορυγηναι τον οικον αυτου
Koma zindikirani izi: Ngati mwini nyumba akanadziwa ora limene mbala ibwera, sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
40 και υμεισ ουν γινεσθε ετοιμοι οτι η ωρα ου δοκειτε ο υιοσ του ανθρωπου ερχεται
Inunso muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa ora limene simukumuyembekezera Iye.”
41 ειπεν δε αυτω ο πετροσ κυριε προσ ημασ την παραβολην ταυτην λεγεισ η και προσ παντασ
Petro anafunsa kuti, “Kodi mukunena fanizoli kwa ife, kapena kwa aliyense?”
42 ειπεν δε ο κυριοσ τισ αρα εστιν ο πιστοσ οικονομοσ και φρονιμοσ ον καταστησει ο κυριοσ επι τησ θεραπειασ αυτου του διδοναι εν καιρω το σιτομετριον
Ambuye anayankha kuti, “Kodi tsono woyangʼanira wokhulupirika ndi wanzeru ndani? Kodi ndi amene mbuye wake wamuyika kukhala oyangʼanira antchito ake kuti aziwapatsa ndalama yachakudya pa nthawi yake yoyenera?
43 μακαριοσ ο δουλοσ εκεινοσ ον ελθων ο κυριοσ αυτου ευρησει ποιουντα ουτωσ
Zidzamukhalira bwino wantchito amene mbuye wake adzamupeza akuchita zimene pamene iye abwera.
44 αληθωσ λεγω υμιν οτι επι πασιν τοισ υπαρχουσιν αυτου καταστησει αυτον
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
45 εαν δε ειπη ο δουλοσ εκεινοσ εν τη καρδια αυτου χρονιζει ο κυριοσ μου ερχεσθαι και αρξηται τυπτειν τουσ παιδασ και τασ παιδισκασ εσθιειν τε και πινειν και μεθυσκεσθαι
Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo aziganiza mu mtima mwake kuti, ‘Bwana wanga akuchedwa kwambiri kubwera,’ ndipo kenaka ndi kuyamba kumenya antchito aamuna ndi aakazi ndi kudya, kumwa ndi kuledzera.
46 ηξει ο κυριοσ του δουλου εκεινου εν ημερα η ου προσδοκα και εν ωρα η ου γινωσκει και διχοτομησει αυτον και το μεροσ αυτου μετα των απιστων θησει
Mbuye wake adzabwera tsiku limene iye sakumuyembekezera ndi ora limene iye sakudziwa. Iye adzamulanga ndi kumusiya kumalo kumene kuli osakhulupirira.
47 εκεινοσ δε ο δουλοσ ο γνουσ το θελημα του κυριου εαυτου και μη ετοιμασασ μηδε ποιησασ προσ το θελημα αυτου δαρησεται πολλασ
“Wantchito amene amadziwa chifuniro cha mbuye wake koma wosakonzeka kapena wosachita chimene mbuye wake akufuna adzakwapulidwa zikwapu zambiri.
48 ο δε μη γνουσ ποιησασ δε αξια πληγων δαρησεται ολιγασ παντι δε ω εδοθη πολυ πολυ ζητηθησεται παρ αυτου και ω παρεθεντο πολυ περισσοτερον αιτησουσιν αυτον
Koma wantchito amene sadziwa koma nʼkuchita zinthu zoyenera chilango, adzakwapulidwa zikwapu zochepa. Aliyense amene anapatsidwa zambiri, adzayenera kubwezanso zambiri; ndipo amene anamusungitsa zambiri, adzamulamula kuti abweze zambirinso.”
49 πυρ ηλθον βαλειν εισ την γην και τι θελω ει ηδη ανηφθη
“Ine ndabwera kudzayatsa moto pa dziko lapansi, ndipo ndikanakonda ukanayaka kale.
50 βαπτισμα δε εχω βαπτισθηναι και πωσ συνεχομαι εωσ ου τελεσθη
Koma Ine ndiyenera kubatizidwa, ndipo ndikusautsika mu mtima mpaka utachitika!
51 δοκειτε οτι ειρηνην παρεγενομην δουναι εν τη γη ουχι λεγω υμιν αλλ η διαμερισμον
Kodi mukuganiza kuti Ine ndinabwera kudzabweretsa mtendere pa dziko lapansi? Ayi, Ine ndikukuwuzani kuti, ndinabweretsa kugawikana.
52 εσονται γαρ απο του νυν πεντε εν οικω ενι διαμεμερισμενοι τρεισ επι δυσιν και δυο επι τρισιν
Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo mʼbanja limodzi mudzakhala anthu asanu ndipo adzawukirana wina ndi mnzake, atatu kuwukira awiri, ndipo awiri kuwukira atatu.
53 διαμερισθησεται πατηρ επι υιω και υιοσ επι πατρι μητηρ επι θυγατρι και θυγατηρ επι μητρι πενθερα επι την νυμφην αυτησ και νυμφη επι την πενθεραν αυτησ
Anthu adzawukirana. Abambo kudzawukira mwana wawo wamwamuna, mwana wawoyo adzawukira abambo ake. Amayi adzawukira mwana wawo wamkazi, mwana wawoyo adzawukira amayi ake. Amayi adzawukira mpongozi wawo wamkazi, mpongoziyo adzawukira amayiwo.”
54 ελεγεν δε και τοισ οχλοισ οταν ιδητε την νεφελην ανατελλουσαν απο δυσμων ευθεωσ λεγετε ομβροσ ερχεται και γινεται ουτωσ
Iye anati kwa gulu la anthu, “Pamene mukuona mtambo ukukwera kummawa, nthawi yomweyo inu mumati, ‘kugwa mvula,’ ndipo imagwadi.
55 και οταν νοτον πνεοντα λεγετε οτι καυσων εσται και γινεται
Ndipo pamene mphepo yakummwera ikuwomba, inu mumati ‘kutentha’ ndipo kumaterodi.
56 υποκριται το προσωπον τησ γησ και του ουρανου οιδατε δοκιμαζειν τον δε καιρον τουτον πωσ ου δοκιμαζετε
Achiphamaso inu! Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a dziko lapansi ndi thambo. Zikutheka bwanji kuti simukudziwa kumasulira kwa nthawi ino?
57 τι δε και αφ εαυτων ου κρινετε το δικαιον
“Bwanji simukuzindikira nokha zoyenera kuchita?
58 ωσ γαρ υπαγεισ μετα του αντιδικου σου επ αρχοντα εν τη οδω δοσ εργασιαν απηλλαχθαι απ αυτου μηποτε κατασυρη σε προσ τον κριτην και ο κριτησ σε παραδω τω πρακτορι και ο πρακτωρ σε βαλη εισ φυλακην
Pamene mukupita kwa woweruza ndi amene munalakwirana naye, yesetsani kwambiri kuti muyanjane naye mʼnjiramo, chifukwa mukapanda kutero akhoza kukutengerani ku bwalo la milandu ndipo woweruzayo adzakuperekani kwa woyangʼanira ndende, ndipo woyangʼanira ndendeyo adzakuponyani mʼndende.
59 λεγω σοι ου μη εξελθησ εκειθεν εωσ ου και τον εσχατον λεπτον αποδωσ
Ine ndikuwuzani kuti, simudzatulukamo mpaka mutalipira ndalama zonse.”

< Κατα Λουκαν 12 >