< Hesekiel 38 >

1 Und es geschah Jehovahs Wort zu mir, sprechend:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Menschensohn, richte dein Angesicht gegen Gog, das Land Magog, den Fürsten, das Haupt von Meschech und Thubal, und weissage wider ihn,
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
3 Und sprich: So spricht der Herr Jehovah: Siehe, Ich bin wider dich, Gog, du Fürst, Haupt von Meschech und Thubal,
Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
4 Und Ich wende dich zurück und tue Haken in deine Kinnbacken und bringe heraus dich und all deine Streitmacht, Rosse und Reiter, alle vollkommen gekleidet, eine große Versammlung mit Schild und Tartsche, allesamt fassend die Schwerter.
Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
5 Perser, Kusch und Pud mit ihnen, sie alle mit Tartsche und Helm.
Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
6 Gomer und alle seine Scharen, Beth Thogarmah, an den Seiten der Mitternacht, und alle seine Scharen, viele Völker mit dir.
Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
7 Sei bereit und bereite dich, du und alle deine Versammlung, die sich um dich angesammelt, und sei ihnen zur Hut.
“‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
8 Nach vielen Tagen wirst du heimgesucht werden, in der Zukunft Jahren wirst du kommen in ein Land, das vom Schwert zurückgebracht aus vielen Völkern zusammengebracht worden, auf die Berge Israels, die beständig eine Öde gewesen, das aus den Völkern herausgebracht worden ist, und wohnen allesamt sicher.
Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
9 Und wie ein Unwetter ziehst du herauf, du kommst, wie eine Wolke, das Land zu bedecken wirst du sein, du und all deine Scharen, und viele Völker mit dir.
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
10 So spricht der Herr Jehovah: Und geschehen wird an jenem Tag, daß Dinge in dein Herz aufsteigen und du böse Gedanken denkst,
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
11 Und sprichst: Ich will hinaufziehen in ein offenliegendes Land, will kommen zu denen, die rasten, die wohnen in Sicherheit. Sie alle wohnen ohne Mauer und Riegel, und Torflügel haben sie keine.
Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
12 Um Beute zu erbeuten und Raub zu rauben, und deine Hand zurückzukehren wider die Öden, die bewohnt sind, und wider ein Volk, das aus den Völkerschaften ist gesammelt worden, und Viehherden und Habe sich schafft und wohnt im Nabel der Erde.
Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
13 Scheba und Dedan und die Händler von Tharschisch und alle seine jungen Löwen werden zu dir sagen: Bist du gekommen Beute zu erbeuten, um Raub zu rauben, hast deine Versammlung du angesammelt, auf daß du Silber und Gold wegtragest, Viehherde und Habe wegnehmest, um große Beute zu erbeuten?
Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
14 Darum weissage, Menschensohn, und sprich zu Gog: So spricht der Herr Jehovah: Wirst du nicht an jenem Tag es wissen, daß Mein Volk Israel wohnt in Sicherheit?
“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
15 Und du kommst von deinem Ort, von den Seiten der Mitternacht, du und viele Völker mit dir, sie alle auf Rossen reitend, eine große Versammlung und viele Streitmacht.
Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
16 Und ziehst herauf wider Mein Volk Israel, wie eine Wolke das Land zu bedecken. In der Zukunft der Tage wird es geschehen, daß Ich dich in Mein Land hereinbringe, auf daß die Völkerschaften Mich erkennen, wie Ich Mich durch dich, o Gog, vor ihren Augen heilige.
Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
17 So spricht der Herr Jehovah: Bist du es, von dem Ich in den Tagen der Vorzeit durch die Hand Meiner Knechte, der Propheten Israels, geredet habe, die in jenen Tagen jahrelang weissagten, daß Ich dich wider sie hereinbringen würde?
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
18 Und wird geschehen an selbigem Tage, am Tage, da Gog auf den Boden Israels kommt, sagt der Herr Jehovah, daß Mein Grimm aufsteigt in Meinem Zorn.
Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
19 Und in Meinem Eifer, im Feuer Meines Wütens, rede Ich: Fürwahr, an jenem Tage wird ein großes Erdbeben sein auf dem Boden Israels,
Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
20 Daß vor Meinem Angesicht beben die Fische des Meeres und der Himmel Gevögel und das wilde Tier des Feldes und all das Kriechtier, das auf dem Boden kriecht, und jeder Mensch auf den Angesichten des Bodens; und Berge werden umgerissen und Felsenwände fallen und zur Erde fällt jede Mauer.
Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
21 Und Ich rufe wider ihn auf allen Meinen Bergen das Schwert, spricht der Herr Jehovah, das Schwert des Mannes soll wider seinen Bruder sein.
Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
22 Und Ich will mit ihm rechten mit Pest und mit Blut, und mit überflutendem Platzregen; und Steine des Hagels, Feuer und Schwefel, lasse Ich regnen über ihn und über seine Scharen, und über die vielen Völker, die mit ihm sind.
Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
23 Und Ich erweise Mich groß und heilige Mich, und tue Mich kund vor den Augen vieler Völkerschaften, auf daß sie wissen, daß Ich Jehovah bin.
Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”

< Hesekiel 38 >