< Psalm 97 >

1 Jahwe ward König! Es frohlocke die Erde, es sollen sich freuen zahlreiche Inseln!
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Gewölk und Dunkel ist um ihn her; Gerechtigkeit und Recht ist die Grundfeste seines Throns.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 Feuer geht vor ihm her und verbrennt ringsum seine Feinde.
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 Seine Blitze erleuchteten den Erdkreis; die Erde sah's und erzitterte.
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 Berge zerschmolzen wie Wachs vor Jahwe, vor dem Herrn der ganzen Erde.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 Der Himmel verkündete seine Gerechtigkeit, und alle Völker sahen seine Herrlichkeit.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Beschämt sind alle, die Bildern dienen, die sich der Götzen berühmen: werft euch nieder vor ihm, all' ihr Götter!
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 Zion hörte es und ward fröhlich, und es frohlockten die Töchter Judas um deiner Gerichte willen, Jahwe.
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 Denn du, Jahwe, bist der Höchste auf der ganzen Erde, bist hoch erhaben über alle Götter.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Die ihr Jahwe liebt, hasset das Arge! Er bewahrt die Seelen seiner Frommen; aus der Gewalt der Gottlosen rettet er sie.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 Licht geht den Frommen auf und Freude denen, die redliches Sinnes sind.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Freut euch, ihr Frommen, über Jahwe und dankt seinem heiligen Namen!
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.

< Psalm 97 >