< Psalm 75 >

1 Dem Musikmeister, “verdirb nicht!” Ein Psalm Asaphs. Ein Lied. Wir danken dir, Gott, wir danken, und die deinen Namen anrufen, verkündigen deine Wunder.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 “Wenn ich die Zeit gekommen finde, so richte ich, wie es recht ist.
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 “Wenn die Erde und alle ihre Bewohner vor Furcht vergehn - ich stelle ihre Säulen fest!” (Sela)
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 Ich spreche zu den Übermütigen: Seid nicht übermütig! und zu den Gottlosen: Hebt euer Horn nicht hoch!
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Hebt euer Horn nicht hoch empor, redet nicht Freches wider den Fels!
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 Denn nicht vom Aufgang und nicht vom Niedergang und nicht aus der Wüste kommt Erhöhung,
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 sondern Gott ist Richter: diesen erniedrigt und jenen erhöht er!
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 Denn Jahwe hat einen Becher in der Hand mit schäumendem Wein und voll von Mischtrank und er schenkt daraus: ja, auch seine Hefen müssen schlürfen und trinken alle Gottlosen auf Erden.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 Ich aber will immerdar jubeln, will dem Gott Jakobs lobsingen.
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 Und alle Hörner der Gottlosen will ich abhauen, aber die Hörner der Frommen sollen hoch erhoben sein!
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

< Psalm 75 >