< Psalm 38 >

1 Ein Psalm Davids, um in Erinnerung zu bringen. Jahwe, nicht in deinem Zorne strafe mich und nicht in deinem Grimme züchtige mich!
Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
2 Denn deine Pfeile haben sich in mich herabgesenkt, und deine Hand fuhr herab auf mich.
Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 An meinem Leibe blieb nichts unversehrt infolge deines Grimms, nichts heil an meinen Gebeinen infolge meiner Sünde.
Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 Denn meine Verschuldungen gehen über mein Haupt; wie eine schwere Last sind sie mir zu schwer.
Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
5 Es stinken, es eitern meine Beulen infolge meiner Thorheit.
Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
6 Ich bin überaus gekrümmt, gebeugt; immerfort gehe ich trauernd einher.
Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
7 Denn meine Lenden sind voll Brand, und an meinem Leibe blieb nichts unversehrt.
Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 Ich bin überaus erstarrt und zerschlagen; ich stöhne lauter, als ein Löwe brüllt.
Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 O Herr, all' mein Begehren ist dir offenbar, und mein Seufzen ist dir nicht verborgen.
Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 Mein Herz pocht heftig, meine Kraft hat mich verlassen; selbst meiner Augen Licht ist nicht bei mir.
Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 Die mich liebten und mir freund waren, treten abseits bei meiner Pein, und die mir nahe standen, halten sich fern.
Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
12 Und die mir nach dem Leben trachten, legten Schlingen, und die mein Unglück suchen, beschlossen Verderben und sinnen immerfort auf Trug.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 Ich aber, gleich einem Tauben, höre nicht und bin wie ein Stummer, der seinen Mund nicht aufthut.
Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 Ich ward wie einer, der nicht hört, in dessen Munde keine Widerrede ist.
Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 Denn auf dich, Jahwe, habe ich geharrt; du wirst erhören, Herr, mein Gott.
Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 Denn ich spreche: daß sie nur nicht über mich frohlocken! Da mein Fuß wankte, thaten sie groß wider mich.
Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
17 Denn ich bin des Hinfallens gewärtig, und mein Schmerz verläßt mich nie.
Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 Denn meine Schuld muß ich bekennen, gräme mich wegen meiner Sünde.
Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 Aber zahlreich sind, die mich ohne Ursache anfeinden, und viel sind derer, die mich grundlos hassen.
Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 Indem sie mir Gutes mit Bösem vergelten, befehden sie mich, dafür, daß ich dem Guten nachjage.
Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 Verlaß mich nicht, Jahwe; mein Gott, sei nicht fern von mir!
Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
22 Eile mir zu Hilfe, Herr, mein Heil!
Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

< Psalm 38 >