< Psalm 25 >

1 Von David. Zu dir, Jahwe, erhebe ich meine Seele.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 Mein Gott, auf dich vertraue ich, laß mich nicht zu Schanden werden; laß meine Feinde nicht über mich frohlocken!
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 Werden doch alle, die auf dich harren, nimmermehr zu Schanden; zu Schanden werden, die ohne Ursach abtrünnig wurden.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Jahwe, zeige mir deine Wege, lehre mich deine Steige!
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Laß mich in deiner Wahrheit wandeln und lehre mich; denn du bist der Gott, der mir hilft: auf dich harre ich alle Zeit.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Gedenke deiner Barmherzigkeit, Jahwe, und deiner Gnadenerweisungen; denn von Ewigkeit her sind sie.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Der Sünden meiner Jugend und meiner Übertretungen gedenke nicht; nach deiner Gnade gedenke du meiner, um deiner Güte willen, Jahwe!
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Gütig und wahrhaftig ist Jahwe, darum weist er Sündern den rechten Weg.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Er läßt die Elenden im Rechte wandeln und lehrt die Elenden seinen Weg.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Alle Wege Jahwes sind Gnade und Wahrheit für die, die seinen Bund und seine Zeugnisse bewahren.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Um deines Namens willen, Jahwe, vergieb mir meine Schuld, denn sie ist groß!
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Wer ist der Mann, der Jahwe fürchtet? Er unterweist ihn über den Weg, den er wählen soll.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Ein solcher wird im Glücke weilen, und seine Nachkommen werden das Land besitzen.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Die Freundschaft Jahwes wird denen, die ihn fürchten, zu teil, und seine Ordnungen thut er ihnen kund.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Meine Augen blicken stets auf Jahwe, denn er wird meine Füße aus dem Netze ziehn.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Wende dich zu mir und sei mir gnädig, denn ich bin einsam und elend!
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Den Nöten meines Herzens schaffe Raum und führe mich heraus aus meiner Bedrängnis!
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Siehe an mein Elend und meine Not und vergieb mir alle meine Sünden.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Siehe an meine Feinde, wie zahlreich sie sind und mit ungerechtem Hasse mich hassen.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Bewahre meine Seele und errette mich; laß mich nicht zu Schanden werden, denn bei dir suche ich Zuflucht.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Unschuld und Redlichkeit mögen mich behüten, denn ich harre auf dich.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 O Gott, erlöse Israel aus allen seinen Nöten!
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Psalm 25 >