< Psalm 128 >

1 Wallfahrtslieder. Wohl einem jeden, der Jahwe fürchtet, der auf seinen Wegen wandelt!
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
2 Was deine Hände erarbeitet, das wirst du genießen; wohl dir, du hast es gut!
Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
3 Dein Weib ist wie ein fruchtbarer Weinstock im Innern deines Hauses, deine Söhne wie Ölbaum-Setzlinge rings um deinen Tisch.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
4 Ja wahrlich, so wird der Mann gesegnet, der Jahwe fürchtet.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
5 Jahwe segne dich vom Zion her, so wirst du alle deine Lebenstage am Glück Jerusalems deine Lust sehen
Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
6 und Söhne deiner Söhne erleben. Friede über Israel!
ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.

< Psalm 128 >