< Nehemia 7 >

1 Als nun die Mauer gebaut war, setzte ich die Thüren ein, und es wurden die Thorhüter mit der Aufsicht betraut.
Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
2 Und ich beorderte zu Befehlshabern über Jerusalem meinen Bruder Hanani und Hananja, den Obersten der Burg; denn er war ein so zuverlässiger und gottesfürchtiger Mann, wie wenige.
Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
3 Und ich wies sie an: Die Thore Jerusalems dürfen nicht eher geöffnet werden, als bis die Sonne heiß scheint. Und während die Wachtposten noch dastehen, soll man die Thürflügel schließen und verriegeln. Und dann soll man Wachen aus den Einwohnern Jerusalems aufstellen, einen jeden auf seinem Posten und zwar einen jeden gegenüber seinem Hause.
Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
4 Es war aber die Stadt von großer Ausdehnung, jedoch nur wenig Volks in ihr, und manche Häuser waren nicht wieder aufgebaut.
Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
5 Da gab mir mein Gott in den Sinn, die Edlen und die Vorsteher und das Volk zur Anfertigung eines Geschlechtsverzeichnisses zu versammeln. Da fand ich das Geschlechtsbuch derer, die zuerst heraufgezogen waren, und fand darin geschrieben:
Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6 Dies sind die Angehörigen der Provinz Juda, die aus der Gefangenschaft der Weggeführten, die Nebukadnezar, der König von Babel, weggeführt hatte, heraufzogen und nach Jerusalem und Juda, ein jeder in seine Stadt, heimkehrten,
Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
7 die mit Serubabel, Jesua, Nehemia, Asarja, Raamja, Nahemani, Mardochai, Bilsan, Mispereth, Bigevai, Nehum und Baana kamen. Die Zahl der Männer des Volkes Israel betrug:
Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
8 Die Nachkommen Pareos': 2172.
Zidzukulu za Parosi 2,172
9 Die Nachkommen Sephatjas: 372.
Zidzukulu za Sefatiya 372
10 Die Nachkommen Arahs: 652.
Zidzukulu za Ara 652
11 Die Nachkommen Pahath-Moabs, nämlich die Nachkommen Jesuas und Joabs: 2818.
Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
12 Die Nachkommen Elams: 1254.
Zidzukulu za Elamu 1,254
13 Die Nachkommen Sattus: 845.
Zidzukulu za Zatu 845
14 Die Nachkommen Sakkais: 760.
Zidzukulu za Zakai 760
15 Die Nachkommen Binnuis: 648.
Zidzukulu za Binuyi 648
16 Die Nachkommen Bebais: 628.
Zidzukulu za Bebai 628
17 Die Nachkommen Asgads: 2322.
Zidzukulu za Azigadi 2,322
18 Die Nachkommen Adonikams: 667.
Zidzukulu za Adonikamu 667
19 Die Nachkommen Bigevais: 2067.
Zidzukulu za Abigivai 2,067
20 Die Nachkommen Adins: 655.
Zidzukulu za Adini 655
21 Die Nachkommen Aters von Hiskia: 98.
Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
22 Die Nachkommen Hasums: 328.
Zidzukulu za Hasumu 328
23 Die Nachkommen Bezais: 324.
Zidzukulu za Bezayi 324
24 Die Nachkommen Hariphs: 112.
Zidzukulu za Harifu 112
25 Die Leute von Gibeon: 95.
Zidzukulu za Gibiyoni 95.
26 Die Leute von Bethlehem und Netopha: 188.
Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
27 Die Leute von Anathoth: 128.
Anthu a ku Anatoti 128
28 Die Männer von Beth-Asmaveth: 42.
Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
29 Die Männer von Kirjath-Jearim, Kaphira und Beeroth: 743.
Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
30 Die Männer von Rama und Geba: 621.
Anthu a ku Rama ndi Geba 621
31 Die Männer von Michmas: 122.
Anthu a ku Mikimasi 122
32 Die Männer von Bethel und Ai: 123.
Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
33 Die Männer von Nebo: 52.
Anthu a ku Nebo winayo 52
34 Die Nachkommen des anderen Elam: 1254.
Ana a Elamu wina 1,254
35 Die Nachkommen Harims: 320.
Zidzukulu za Harimu 320
36 Die Leute von Jericho: 345.
Zidzukulu za Yeriko 345
37 Die Leute von Lod, Hadid und Ono: 721.
Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
38 Die Leute von Senaa: 3930.
Zidzukulu za Senaya 3,930.
39 Die Priester: Die Nachkommen Jedajas vom Hause Jesua: 973.
Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
40 Die Nachkommen Immers: 1052.
Zidzukulu za Imeri 1,052
41 Die Nachkommen Pashurs: 1247.
Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
42 Die Nachkommen Harims: 1017.
Zidzukulu za Harimu 1,017.
43 Die Leviten: Die Nachkommen Jesuas und Kadmiels, von den Nachkommen Hodejas: 74.
Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
44 Die Sänger: Die Nachkommen Asaphs: 148.
Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
45 Die Thorhüter: Die Nachkommen Sallums, die Nachkommen Aters, die Nachkommen Talmons, die Nachkommen Akkubs, die Nachkommen Hatitas, die Nachkommen Sobais: 138.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
46 Die Tempeldiener: Die Nachkommen Zihas, die Nachkommen Hasuphas, die Nachkommen Tabbaoths,
Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
47 die Nachkommen Keros', die Nachkommen Sias, die Nachkommen Padons,
Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
48 die Nachkommen Lebanas, die Nachkommen Hagabas, die Nachkommen Salmais,
Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
49 die Nachkommen Hanans, die Nachkommen Giddels, die Nachkommen Gahars,
Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
50 die Nachkommen Reajas, die Nachkommen Rezins, die Nachkommen Nekodas,
Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
51 die Nachkommen Gassams, die Nachkommen Usas, die Nachkommen Paseahs,
Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
52 die Nachkommen Besais, die Nachkommen der Meuniter, die Nachkommen der Nephisiter,
Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
53 die Nachkommen Bakbuks, die Nachkommen Kauphas, die Nachkommen Harhurs,
Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
54 die Nachkommen Bazeliths, die Nachkommen Mehidas, die Nachkommen Harsas,
Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
55 die Nachkommen Barkos', die Nachkommen Siseras, die Nachkommen Themahs,
Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
56 die Nachkommen Neziahs, die Nachkommen Hatiphas.
Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
57 Die Nachkommen der Sklaven Salomos: Die Nachkommen Sotais, die Nachkommen Sophereths, die Nachkommen Peridas,
Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
58 die Nachkommen Jaalas, die Nachkommen Darkons, die Nachkommen Giddels,
zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
59 die Nachkommen Sephatjas, die Nachkommen Hattils, die Nachkommen des Pochereth-Hazzebaim, die Nachkommen Amons,
zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
60 sämtliche Tempeldiener und Nachkommen der Sklaven Salomos: 392.
Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
61 Und diese sind es, die aus Tel-Melah, Tel-Harsa, Cherub, Addon und Immer heraufzogen, ohne daß sie ihre Familie und ihre Abstammung angeben konnten, ob sie aus Israel stammten:
Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62 Die Nachkommen Delajas, die Nachkommen Tobias, die Nachkommen Nekodas: 642.
Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
63 Und von den Priestern: Die Nachkommen Habajas, die Nachkommen Hakkoz', die Nachkommen Barsillais, der eine von den Töchtern des Gileaditers Barsillai geheiratet hatte und nach ihrem Namen genannt wurde.
Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
64 Diese suchten ihre Geschlechtsverzeichnisse, aber sie waren nicht zu finden; daher wurden sie vom Priestertum ausgeschlossen.
Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
65 Und der Statthalter verbot ihnen, vom Hochheiligen zu essen, bis wieder ein Priester für die Handhabung der Urim und Tummim erstehen würde.
Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66 Die ganze Gemeinde betrug zusammen 42360,
Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
67 ungerechnet ihre Sklaven und Sklavinnen; deren gab es 7337 und dazu kamen 245 Sänger und Sängerinnen.
Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
68 Rosse hatten sie: 736, Maultiere: 245,
Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69 Kamele: 435, Esel: 6720.
Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70 Und ein Teil der Familienhäupter spendete zum Tempeldienst. Der Statthalter spendete für den Schatz: an Gold tausend Drachmen, fünfzig Sprengschalen, 30 Priesterröcke.
Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
71 Und einige von den Familienhäuptern spendeten zum Schatze für den Tempeldienst: an Gold 20000 Drachmen und an Silber 2200 Minen.
Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
72 Und was das übrige Volk spendete, betrug an Gold 20000 Drachmen und an Silber 2000 Minen, und siebenundsechzig Priesterröcke.
Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73 Und so wohnten die Priester und die Leviten und die Thorhüter und die Sänger und ein Teil des Volks und die Tempeldiener und sämtliche Israeliten in ihren Städten.
Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.

< Nehemia 7 >