< Klagelieder 5 >

1 Gedenke, Jahwe, was uns widerfahren; schau her und sieh unsere Schmach!
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 Unser Erbbesitz ist Fremden zugefallen, unsere Häuser Ausländern.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 Wir sind Waisen geworden, vaterlos, unsere Mütter zu Witwen.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 Unser Wasser trinken wir um Geld, unser Holz bekommen wir nur gegen Zahlung.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 Unsere Verfolger sitzen uns auf dem Nacken; sind wir ermattet, gönnt man uns keine Ruhe.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 Ägypten reichten wir die Hand, Assur, um satt zu werden.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 unsere Väter fehlten; sie sind nicht mehr, und wir tragen ihre Verschuldungen.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Knechte herrschen über uns; niemand entreißt uns ihrer Hand.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 Mit Gefahr unseres Lebens holen wir unser Brot voller Angst vor dem Schwert und der Pest.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Unsere Haut ist geschwärzt wie ein Ofen, von den Gluten des Hungers.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 Frauen in Zion haben sie geschändet, Jungfrauen in den Städten Judas.
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 Fürsten wurden durch ihre Hand gehenkt, der Vornehmen Ansehn für nichts geachtet.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 Jünglinge nahmen sie zum Mahlen, und Knaben strauchelten unter der Last von Holz.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 Verschwunden sind die Greise am Thor, das Saitenspiel der Jünglinge.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 Geschwunden ist unseres Herzens Freude; in Klage ist unser Reigen verwandelt.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 Die Krone ist uns vom Haupte gefallen: wehe uns, daß wir gesündigt haben!
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 Darüber ist unser Herz siech geworden, darob unsere Augen trübe,
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 über den Zionsberg, der verwüstet ist, auf dem sich Füchse tummeln.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 Du, Jahwe, thronst auf ewig, dein Stuhl steht von Geschlecht zu Geschlecht.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Warum willst du uns für immer vergessen, uns lebenslang verlassen?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Bekehre uns zu dir, Jahwe, so kehren wir um; erneuere unsere Tage, wie vor Alters!
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 Oder hast du uns ganz verworfen, bist überaus auf uns erzürnt?
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

< Klagelieder 5 >