< Job 40 >

1 Und Jahwe antwortete Hiob und sprach:
Yehova anati kwa Yobu:
2 Hadern mit dem Allmächtigen will der Tadler? Der Ankläger Gottes antwortete darauf!
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Dann antwortete Hiob Jahwe und sprach:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 Fürwahr, zu gering bin ich; was soll ich dir erwidern? Ich lege meine Hand auf meinen Mund.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Einmal habe ich geredet und werde es nicht wiederholen - ein zweites Mal, und werde es nicht wieder thun!
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Dann antwortete Jahwe Hiob aus Wettersturm und sprach:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 Auf, gürte deine Lenden wie ein Mann: Ich will dich fragen und du belehre mich!
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Willst du gar mein Recht zunichte machen, mich verdammen, damit du Recht behaltest?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Hast du denn einen Arm wie Gott und vermagst du mit gleichem Schall wie er zu donnern?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Schmücke dich doch mit Majestät und Hoheit! Umkleide dich mit Glanz und Herrlichkeit!
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Laß sich ergießen deines Zornes Fluten und wirf mit einem Blicke jeden Stolzen nieder!
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Mit einem Blicke demütige jeden Stolzen und strecke die Gottlosen zu Boden.
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Birg sie im Staube allzumal, banne ihr Angesicht an verborgenem Ort,
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 so will auch ich dich loben, daß deine Rechte dir Sieg verschafft!
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Sieh nur das Nilpferd, das ich schuf wie dich; Gras frißt es wie ein Rind!
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Sieh nur seine Kraft in seinen Lenden und seine Stärke in den Muskeln seines Leibes.
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 Es streckt seinen Schwanz wie eine Ceder aus, die Sehnen seiner Schenkel sind dicht verschlungen.
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 Seine Knochen sind Röhren von Erz, seine Gebeine wie ein eiserner Stab.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 Das ist der Erstling von Gottes Walten; der es schuf, reicht dar sein Schwert.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 Denn Futter tragen ihm die Berge, wo alle Tiere des Feldes spielen.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 Unter Lotusbüschen lagert es, im Versteck von Rohr und Schilf.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 Lotusbüsche überdachen es, um ihm Schatten zu geben, des Baches Weiden umfangen es.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Wenn der Strom anschwillt, bangt es nicht, bleibt ruhig, wenn ein Jordan gegen seinen Rachen andringt.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Vermag es einer von vorn zu packen, mit Sprenkeln ihm die Nase zu durchbohren?
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?

< Job 40 >