< 1 Chronik 24 >

1 Die Nachkommen Aarons aber hatten auch ihre Abteilungen. Die Söhne Aarons waren Nadab, Abihu, Eleasar und Ithamar.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 Nadab und Abihu aber starben vor ihrem Vater, ohne Söhne zu hinterlassen, und so bekleideten nur Eleasar und Ithamar das Priesteramt.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 Und David nebst Zadok, der von den Nachkommen Eleasars war, und Ahimelech, der von den Nachkommen Ithamars war, teilten sie je nach ihrem Amt in ihren Dienst ein.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 Es befand sich aber, daß die Nachkommen Eleasars hinsichtlich der Geschlechtshäupter zahlreicher waren, als die Nachkommen Ithamars; daher teilte man sie so, daß auf Eleasar sechzehn, auf Ithamar acht Familienhäupter kamen.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 Und zwar teilte man sie, die einen wie die anderen, durchs Los ab; denn es gab Fürsten des Heiligtums und Fürsten Gottes sowohl unter den Nachkommen Eleasars, als unter den Nachkommen Ithamars.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 Und Semaja, der Sohn Nethaneels, der Schreiber aus der Zahl der Leviten, schrieb sie auf in Gegenwart des Königs und der Fürsten und des Priesters Zadok und Ahimelechs, des Sohnes Abjathars, sowie der Familienhäupter der Priester und Leviten. Je eine Familie wurde von der Linie Eleasar und je eine von der Linie Ithamar ausgelost.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 Das erste Los fiel auf Jojarib, das zweite auf Jedaja,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 das dritte auf Harim, das vierte auf Seorim,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 das fünfte auf Malchia, das sechste auf Mijamin,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 das siebente auf Hakkoz, das achte auf Abia,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 das neunte auf Jesua, das zehnte auf Sechanja,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 das elfte auf Eljasib, das zwölfte auf Jakim,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 das dreizehnte auf Huppa, das vierzehnte auf Jesebeab,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 das fünfzehnte auf Bilga, das sechzehnte auf Immer,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 das siebzehnte auf Hesir, das achtzehnte auf Happizzez,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 das neunzehnte auf Pethahja, das zwanzigste auf Jeheskel,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 das einundzwanzigste auf Jachin, das zweiundzwanzigste auf Gamul,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 das dreiundzwanzigste auf Delaja, das vierundzwanzigste auf Maasja.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 Das ist ihre Amtsordnung für ihren Dienst, den Tempel Jahwes zu betreten, gemäß der Vorschrift, die ihr Ahnherr Aaron für sie erlassen hatte, so wie es Jahwe, der Gott Israels ihm befohlen hatte.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 Was aber die übrigen Nachkommen Levis betrifft, so waren von den Nachkommen Amrams Subael, von den Nachkommen Subaels Jehdeja,
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 von den Nachkommen Rehabjas das Oberhaupt Jissia,
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 von den Jizharitern Selomoth, von den Nachkommen Selomoths Jahath;
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 von den Nachkommen Hebrons aber waren: Jeria, das Oberhaupt, Amarja, der zweite, Jahasiel, der dritte, Jekameam, der vierte.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 Die Nachkommen Ussiels waren: Micha, von den Nachkommen Michas Samir.
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 Der Bruder Michas war Jissia; von den Nachkommen Jissias war Sacharja.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 Die Nachkommen Meraris waren Mahli und Musi, und die Nachkommen seines Sohnes Jaasia.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 Die Nachkommen Meraris von seinem Sohne Jaasia waren: Soham, Sakkur und Ibri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 Von Mali war Eleasar; der hatte keine Söhne.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 Von Kis: Die Nachkommen Kis' waren: Jerahmeel.
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 Die Nachkommen Musis waren: Mahli, Eder und Jerimoth. Das sind die Nachkommen der Leviten nach ihren Familien.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 Und auch sie warfen Lose, so gut wie ihre Stammesgenossen, die Nachkommen Aarons, in Gegenwart des Königs David und Zadoks und Ahimelechs und der Familienhäupter der Priester und Leviten, und zwar die Familienhäupter so gut wie ihre jüngeren Brüder.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Chronik 24 >