< Psalm 4 >

1 Auf den Siegesspender, mit Saitenspiel, ein Lied, von David. Erhöre mich, Gott meines Heils, dieweil ich rufe! Verschaffe Luft mir in der Not! Sei gnädig Herr! Erhöre mein Gebet! -
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
2 Wie lang, ihr Männer, wird geschändet meine Ehre und liebet ihr den Tand und jaget nach dem Truge? (Sela)
Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
3 Bedenkt, daß seine Frommen so der Herr auszeichnet: "Mich hört der Herr, sobald ich zu ihm rufe."
Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
4 Wenn ihr euch keine Ruhe gönnet, dann sündiget doch nicht! Zerbrecht ihr euch den Kopf auf eurem Lager, dann schweiget wenigstens! (Sela)
Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
5 Bringt lieber richtige Opfer dar! Vertraut dem Herrn! -
Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
6 Die Masse sagt: "Wer läßt uns Gutes nur genießen?" Uns aber laß das Licht, Herr, Deines Angesichtes leuchten!
Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
7 Mehr Freude legst Du mir ins Herz, als wenn sich Korn und Wein vermehrt.
Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
8 Ich kann mich sorglos niederlegen und mich demSchlummer überlassen; denn Du läßt mich ganz ungestört und sicher ruhen, Herr.
Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.

< Psalm 4 >