< Psalm 29 >

1 Ein Lied, von David. - Ihr Gottessöhne! Bringet für den Herrn herbei, bringt Kostbarkeiten, Schätze für den Herrn!
Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
2 Bringt für den Herrn die Schätze, seines Namens würdig! Werft vor den Herrn euch hin mit Schmuck fürs Heiligtuni! -
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
3 Des Herrn Stimme dröhnet über den Gewässern. Der Gott der Herrlichkeit ließ donnern; der Herr war über mächtigen Gewässern.
Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
4 Des Herrn Stimme schallt in Kraft; des Herrn Stimme schallt mit Majestät.
Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
5 Des Herrn Stimme splittert Zedern. Der Herr zerschmettert Zedern Libanons.
Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
6 Er ließ den Libanon gleich einem Kalbe hüpfen, den Sirjon wie ein Büffeljunges.
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
7 Des Herrn Stimme spaltet Feuerflammen.
Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
8 Des Herrn Stimme macht die Wüste beben. Einst ließ der Herr die Wüste Kades zittern.
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
9 Des Herrn Stimme macht, daß Rehe werfen, und daß entblößt die Wälder werden. Mit ihrer ganzen Kraft bestellt er Schätze in sein Heiligtum. -
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
10 Und überm Sintflutregen hatte einst der Herr gethront. Der Herr war König schon in alten Zeiten.
Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 Der Herr verleihe Schätze seinem Volk! Mit Frieden segne doch der Herr sein Volk!
Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

< Psalm 29 >