< Psalm 25 >

1 Von David. - Nach Dir verlangt mich, Herr.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 Mein Gott, auf Dich nur hoffe ich. Laß nimmer mich zuschanden werden! Laß meine Feinde über mich nicht jubeln!
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 Nicht einer, der auf Dich vertraut, wird je zuschanden. Doch leer gehn aus die Abgefallenen.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Belehre, Herr, mich über Deine Wege! Gewöhne mich an Deine Pfade!
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 In Deiner Treue leite mich! Gewöhne mich daran! Denn Du bist meines Heiles Gott; stets hoffe ich auf Dich. -
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Gedenke Deiner Liebe, Herr, und Güte! Sie sind von Ewigkeit.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Gedenk nicht meiner Jugendsünden, meiner Missetaten nicht! Gedenk mir dessen nur, was Deiner Gnade würdig ist, um Deiner Güte willen, Herr! -
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Der Herr ist gütig und wahrhaftig; drum zeigt er Irrenden die rechte Bahn.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Bedrückte leitet er, wie's richtig ist, gewöhnt an seinen Weg die Dulder.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Des Herrn Wege all' sind Lieb' und Treue für die, die seinen Bund und seine Lehren halten. -
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Um Deines Namens willen, Herr, vergib mir meine Schuld, so groß ist sie! -
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Ist irgendwo ein Mann in Furcht des Herrn, so zeigt er ihm den Weg, den jener wählen soll.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Ihm ist das Glück auch hold; sein Stamm ererbt das Land.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Des Herrn Geheimnis eignet denen, die ihn fürchten; in seinen Bund weiht er sie ein.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Mein Auge schaut stets auf den Herrn; denn meine Füße kann er vor dem Netz bewahren.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Schau her auf mich! Sei gnädig mir! Verlassen bin ich, elend.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Erweitere mein beklemmtes Herz! Aus meinen Nöten rette mich!
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Schau meine Pein, mein Elend an! Vergib mir alle meine Sünden! -
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Betrachte meine Feinde, welche Menge, den Haß, wie furchtbar sie mich hassen!
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Mein Leben schirme, rette mich, damit ich nicht zuschanden werde! Ich harre Dein.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Mir bleibe Unschuld! Mir bleibe Redlichkeit! Ich harre Dein.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Erlöse Israel aus allen seinen Nöten, Gott!
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Psalm 25 >