< Psalm 23 >

1 Ein Lied, von David. - Mein Hirte ist der Herr; mir mangelt nichts.
Salimo la Davide. Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.
2 Er lagert mich auf grünen Auen; er leitet mich zu stillen Wassern,
Amandigoneka pa msipu wobiriwira, amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,
3 lenkt mein Begehr und leitet mich auf rechten Pfaden zu seines Namens Wohnstatt hin. -
amatsitsimutsa moyo wanga. Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo chifukwa cha dzina lake.
4 Und walle ich im Tal des Todesschattens, ich fürchte keinerlei Gefahr; denn Du begleitest mich. Ein Trost sind mir Dein Stab und Deine Rute, die mir zur Leitung dienen.
Ngakhale ndiyende mʼchigwa cha mdima wakuda bii, sindidzaopa choyipa, pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu zimanditonthoza.
5 Du richtest mir ein Mahl vor meinen Neidern zu. Du salbst mein Haupt mit Öl und schenkst mir vollen Becher ein.
Mumandikonzera chakudya adani anga akuona. Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta; chikho changa chimasefukira.
6 In meinem Leben folgt mir Glück und Huld, und immer weile ich im Haus des Herrn.
Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata masiku onse a moyo wanga, ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova kwamuyaya.

< Psalm 23 >