< Psalm 145 >

1 Ein Loblied, von David. - Erheben will ich Dich, mein Gott, Du König, und Deinen Namen immerdar und ewig preisen.
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Ich will Dich jeden Tag lobpreisen und immer und auf ewig Deinen Namen rühmen: -
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 "Groß ist der Herr und hoch zu preisen und unerforschlich seine Größe",
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 daß ein Geschlecht dem andere Deine Werke rühme und Deine großen Taten künde.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 Vom wundervollen Glanze Deiner Herrschergröße, von Deinen Wundertaten will ich singen.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 Daß man von Deiner Schreckenstaten Größe rede, will ich von Deinen Großtaten erzählen.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Lob Deiner großen Güte ströme aus, und Jubel preise Deine Liebe! -
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 Der Herr ist gnädig und barmherzig, geduldig und von großer Güte.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 Der Herr ist gütig gegen alle, voll Liebe zu seinen Geschöpfen all.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Dich sollen alle Deine Werke loben, Herr, und Deine Frommen Dich lobpreisen!
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 Von Deines Reiches Glanze sollen sie erzähle und Deine Macht verkünden
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 und so die andern Deine großen Taten lehren und Deines Reiches Pracht und Herrlichkeit!
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Dein Reich ist ja ein Reich für alle Zeiten, und Deine Herrschaft reicht bis zu den äußersten Geschlechtern.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Der Herr stützt alle Wankenden und richtet alle, die gebeugt sind, auf.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Die Augen aller schauen hin auf Dich; Du speisest sie zur rechten Zeit.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Du öffnest Deine Hand und sättigst alles, was da lebt, mit Lust. -
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 In allen seinen Wegen ist der Herr so gütig, in allen seinen Werken liebevoll.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Der Herr ist allen nahe, die ihn rufen, ja allen, die mit Recht ihn rufen dürfen,
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 erfüllt die Wünsche derer, die ihn fürchten, vernimmt ihr Schreien und errettet sie.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Der Herr behütet alle, die ihn lieben, und rottet alle Frevler aus.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 So singt mein Mund das Lob des Herrn, daß alles Fleisch lobpreise seinen heiligen Namen für immer und auf ewig.
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.

< Psalm 145 >