< Psalm 138 >

1 Von David. - Dich preise ich von ganzem Herzen; begeistert singe ich Dir zu.
Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
2 In Deinem heiligen Tempel werfe ich mich nieder und preise Deinen Namen hoch für Deine Huld und Treue. Denn über allen Deinen Ruhm hinaus hast Du Dein Wort verherrlicht.
Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
3 Sooft ich zu Dir rufe, hörst Du mich, und so entlockst Du mir die kühnsten Wünsche.
Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
4 Dich preisen alle Erdenkönige, wenn Deines Mundes Worte sie vernehmen. -
Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
5 Sie singen von des Herren Wegen; der Ruhm des Herrn ist groß.
Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
6 Denn hoch erhaben ist der Herr und blickt doch auf das Niedrige, und ist er noch so hoch, so nimmt er doch aus weiter Ferne wahr. -
Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
7 Und wandle ich auch mitten in der Not, erhältst Du dennoch mich am Leben; zu meiner Feinde Zorn streckst Deine Hand Du aus und hilfst mir so mit Deiner Rechten.
Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
8 Der Herr vollführt's für mich. Herr! Ewig währet Deine Huld. Laß nicht von Deiner Hände Werk!
Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.

< Psalm 138 >