< Psalm 13 >

1 Auf den Siegesspender, ein Lied von David. Wie lange willst Du mich vergessen, Herr, wie lange noch Dein Antlitz mir verhüllen?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
2 Wie lange soll ich meinen Geist mit Sinnen, mein Herz mit Sorgen täglich quälen? Wie lange noch mein Feind obsiegen über mich?
Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
3 Schau her, erhöre mich, Du Herr, mein Gott! Erleuchte meine Augen, daß ich des Todes nicht entschlafe,
Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
4 daß nicht mein Feind sich rühme: "Den hab ich bezwungen", nicht meine Gegner jubeln, daß ich wanke!
mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
5 Ich baue fest auf Deine Huld. Mein Herz frohlocke über Deine Hilfe!
Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
6 Ich will dem Herrn lobsingen, wenn er mir Gutes unverdient getan.
Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.

< Psalm 13 >