< Psalm 129 >

1 Ein Stufenlied. - Sie haben mich schon oft von Jugend an bedrängt." So spreche Israel!
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
2 "Schon oft von Jugend an bedrängt, jedoch nicht überwältigt.
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
3 Mit meinem Rücken pflügten sie und dehnten ihre Ackerfelder in die Weite.
Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
4 Der Herr jedoch, gerecht, zerhaut der Frevler Stränge."
Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5 In Schande sollen weichen all die Hasser Sions.
Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6 Sie seien wie das Gras auf Dächern, das vor dem Blühen schon verdorrt!
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
7 Der Schnitter füllt nicht seine Hand damit, nicht seinen Schoß der Garbenbinder.
sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
8 Und keiner der Vorübergehenden ruft: "Des Herren Segen über euch! Wir grüßen euch im Namen des Herrn."
Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

< Psalm 129 >