< Psalm 116 >

1 Weil auf mein Rufen hört der Herr, hab ich die Stunden meiner Andacht lieb;
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 er neigt sein Ohr zu mir, sooft ich rufe.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Umfangen mich des Todes Bande, und überkommt mich Höllenangst, und komme ich in Not und Jammer, (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 dann rufe ich des Herren Namen an; "Ach, rette, Herr, mein Leben!"
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Der Herr ist gnädig und ist mild; erbarmungsvoll ist unser Gott.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 Einfältige beschützt der Herr; bin ich unwürdig schon, so hilft er dennoch mir.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Zu deiner Ruhestätte, meine Seele, wende dich! Der Herr tut dir ja Gutes unverdient.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Du wahrst mein Leben vor dem Tode, mein Auge vor den Tränen und meine Füße vor dem Straucheln.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 So kann ich wandeln vor dem Herrn im Lande der Lebendigen.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Ich kann's bestätigen, was ich jetzt sage: Ich war so tief gebeugt.
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 Ich sprach in meiner Angst: "Die Menschenkinder trügen all."
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 Wie kann ich jetzt dem Herrn vergelten all das, was er an mir getan?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Des Heiles Kelch ergreife ich; des Herren Ruhm verkünde ich. -
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Was ich dem Herrn gelobt, das löse ich jetzt ein vor seinem ganzen Volke.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Bedeutungsvoll ist in des Herren Augen, wenn's um das Sterben seiner Frommen geht. -
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Ach, Herr, ich bin Dein Knecht; ich bin Dein Knecht, von Deiner Magd geboren. Wenn Du jetzt meine Bande lösest,
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 dann bringe ich Dir Dankesopfer dar und künde so des Herren Ruhm. -
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Was ich dem Herrn gelobt, das löse ich jetzt ein vor seinem ganzen Volke,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 im Haus des Herrn in seinen Höfen, Jerusalem, in deiner Mitte. Alleluja!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalm 116 >