< Psalm 111 >

1 Alleluja! Aus ganzem Herzen danke ich dem Herrn im Kreis der Frommen und in der Gemeinde.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 Des Herren Werke sind gewaltig, wie ausgesucht für alle ihre Zwecke.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 Sein Wirken ist nur Pracht und Glanz, und ewig währet seine Liebe.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Er sorgt für seiner Wunder Fortbestand; erbarmungsvoll und gnädig ist der Herr.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 Er spendet Nahrung denen, die ihn fürchten, auf immer seines Bundes eingedenk.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 Er zeigte seinem Volke seiner Taten höchstes Maß, wie er das Eigentum der Heiden ihnen zum Besitze gab.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 Von Recht und Treue zeugt ja seiner Hände Werk; was er verfügt, ist alles wohlgemeint.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 Für alle Zeiten sind sie festgesetzt und ausgeführt mit Treue und Gerechtigkeit.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 Er sandte seinem Volk Erlösung und schloß auf ewig seinen Bund. "Furchtbarer", "Heiliger" ist sein Name.
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 Der Weisheit Anfang ist die Furcht des Herrn. Wer also tut, der führt sich gut. Sein Ruhm besteht für ewige Zeiten.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< Psalm 111 >