< Psalm 106 >

1 Alleluja! Dem Herrn sagt Dank! Denn er ist gut! Auf ewig währet seine Huld.
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Wer redet würdig von des Herren großen Taten, verkündet all sein Lob?
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 Heil denen, die das Richtige befolgen und es zu jeder Zeit recht machen! -
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Gedenke meiner, Herr, begnadigst Du Dein Volk und kommt Dein Heil, so denk auch meiner,
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 daß Deiner Auserwählten Glück ich noch erlebe und mich der Freude Deines Volkes freue und mit den ewig Deinen jubiliere!
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 Gesündigt haben wir mit unsren Vätern, unrecht und frevelhaft gehandelt.
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Schon unsere Väter merkten nicht auf Deine Wunder in Ägypten und dachten nicht an Deine Gnadenfülle. - Sie haderten am Meer, des Schilfmeers wegen.
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 Um seines Namens willen half er ihnen, um seine Stärke kundzutun.
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 Er schalt das Schilfmeer; es versiegte. Er führte sie durch Fluten wie durch eine Trift,
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 entriß sie aus der Hasser Hand, befreite sie aus Feindes Macht.
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 Das Wasser deckte ihre Dränger; nicht einer blieb von ihnen übrig.
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 Da glaubten sie an seine Worte und stimmten einen Lobgesang ihm an.
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 Doch schnell vergaßen sie dann seine Taten und harrten seines Rates nicht.
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 Sie wurden in der Wüste lüstern, versuchten Gott im wasserlosen Land.
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 Da gab er ihnen ihr Begehr: Erbrechen sandte er in ihren Hals.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 Im Lager aber wurden sie auf Moses eifersüchtig und auf den Heiligen des Herrn, auf Aaron.
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 Die Erde tat sich auf, verschlang den Dathan, begrub die Rotte Abirams.
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 In ihrer Rotte flammte Feuer auf, und eine Flamme fraß die Frevler. -
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Am Horeb machten sie ein Kalb und beteten ein Gußbild an,
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 vertauschten ihres Gottes Herrlichkeit mit der Gestalt des Stiers, der Gras verzehrt,
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 vergaßen Gott, der sie gerettet, der Großes in Ägypten hat getan,
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 Erstaunliches im Lande Chams, Erschreckliches am Roten Meer.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 Er dachte dran, sie zu vertilgen; da trat vor ihm sein Auserwählter, Moses, in die Bresche, um seinen Grimm vom Unheil abzuwenden. -
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Doch sie verschmähten das ersehnte Land und glaubten seinem Worte nicht.
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 In ihren Zelten murrten sie, gehorchten nicht des Herren Stimme.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 Da schwur er ihnen hoch und teuer, sie in der Wüste zu vertilgen,
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 den Heiden preiszugeben ihren Stamm und diesen in die Länder zu versprengen. -
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Sie paarten sich zu Ehren Baal Peors und aßen Totenopfer.
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 Sie reizten ihn durch ihre Taten; da brach die Pest bei ihnen aus.
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Und Pinechas stand auf und schlichtete; da ward die Pest gehemmt.
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 Ihm ward es zum Verdienst gerechnet und seinen Enkeln immerfort.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 Und sie erzürnten ihn am Haderwasser, und ihretwegen mußte Moses leiden.
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 Denn sie verbitterten ihm das Gemüt so daß er unbedacht mit seinen Worten war.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 Sie tilgten auch die Völker nicht, wie's ihnen doch der Herr gebot.
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 Sie mischten sich mit Heiden und lernten ihre Sitten.
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 Sie dienten ihren Götzen, und diese brachten sie zu Fall.
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 So opferten sie ihre Söhne und ihre Töchter den Dämonen.
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 Unschuldig Blut vergossen sie, das Blut der eigenen Söhne und der Töchter, die sie den Götzen Kanaans zum Opfer brachten. So ward das Land durch Mord entweiht.
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 Sie selbst bedeckten sich durch ihre Taten; durch ihre Werke wurden sie so untreu.
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 Da zürnte seinem Volk der Herr aufs heftigste, zum Abscheu wurde ihm sein Erbe.
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 Er gab sie in der Heiden Hand, und ihre Hasser herrschten über sie.
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 Und ihre Feinde drückten sie; sie mußten ihrer Macht sich beugen. -
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Zu vielen Malen hat er sie befreit; sie aber blieben voller Trotz bei ihrem Plan, verkamen so durch ihre Sünde.
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Er sah auf ihre Not, sooft er ihre Klage hörte, dachte er
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 an seinen Bund mit ihnen, ward andern Sinns in seiner großen Huld
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 und ließ sie Mitleid finden bei allen ihren Siegern. -
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Zu Hilfe uns, Herr, unser Gott! - Bring uns zusammen aus den Heidenvölkern, auf daß wir Deinem heiligen Namen danken, uns rühmen Deines Ruhmes! -
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Gepriesen sei der Herr, Gott Israels, von Ewigkeit zu Ewigkeit, und alles Volk soll sprechen: "Amen! Alleluja!"
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.

< Psalm 106 >