< Psalm 105 >

1 Dem Herrn sagt Dank! Verherrlicht seinen Namen! Macht seine Taten den Nationen kund!
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Lobsingt von ihm! Lobt ihn! Erzählt von seinen Wundern all!
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 In seinem heiligen Namen rühmet euch! Von Herzen freue sich, wer nach dem Herrn sucht!
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Verlanget nach dem Herrn und seiner Herrlichkeit! Stets sucht sein Angesicht!
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Gedenkt der Wunder, die er tat, der Zeichen, seiner Richtersprüche!
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 Geschlecht du, seines Knechtes Abraham, ihr Söhne Jakobs, seines Auserwählten! -
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Der Herr ist unser Gott, und auf der ganzen Erde gelten seine Urteilssprüche.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 In Ewigkeit gedenkt er seines Bundes und seines Wortes, das er sprach, ins tausendste Geschlecht,
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 des Bunds, den er mit Abraham geschlossen für Israel als einen ewigen Bund,
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 den er für Jakob als ein Recht bestätigt, und seines Eides, den er Isaak zugeschworen.
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 "Dir", sprach er, "geb' ich Kanaan, als euer zugemessen Erbe." -
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 Noch klein war damals ihre Zahl, noch winzig klein und fremd darin.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 Sie wanderten von einem Heidenvolk zum andern, von einem Reich zu einer andern Nation.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 Er gab nicht zu, daß jemand sie bedrückte; er warnte ihretwegen Könige:
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 "Vergreift euch nicht an den von mir Gesalbten! Fügt keinen Schaden meinen Sehern zu!" -
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Er rief alsdann ins Land den Hunger, jedwede Brotesstütze brechend.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Er sandte einen Mann vor ihnen her; zum Sklaven ward Joseph verkauft.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 in Fesseln zwang man seine Füße; in Eisen ward sein Hals gelegt,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 bis in Erfüllung ging, was er verheißen, und ihn der Spruch des Herrn bewährte.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Da ließ der König ihn entfesseln; der Völkerherrscher ließ ihn frei.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Er machte ihn zum Herrn in seinem Hause und zum Verwalter über all sein Gut,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 daß er nach seinem Sinne seine Fürsten lenkte und seine Ältesten belehrte. -
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Alsdann kam nach Ägypten Israel, und Jakob ward ein Gast im Lande Chams.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Er machte fruchtbar dort sein Volk, für seine Feinde allzu zahlreich.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Nun wandte er ihr Herz zum Hasse wider Gottes Volk, zur Arglist gegen seine Diener.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Er sandte Moses, seinen Diener, und Aaron, den er sich erkoren.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Sie zeigten ihnen seine Wunder und taten Zeichen in dem Lande Chams.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Er sandte Finsternis, und dunkel ward's; doch achteten sie nicht auf seinen Wink.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Er wandelte in Blut ihr Wasser, und ihre Fische ließ er sterben.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Er ließ ihr Land von Fröschen wimmeln bis in die Kammern ihrer Könige.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Er sprach; da kam ein Fliegenschwarm und Mücken in ihr ganz Gebiet.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Für Regen gab er ihnen Hagel und Feuerflammen auf ihr Land,
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 schlug ihren Weinstock, ihren Feigenbaum darnieder. zersplitterte die Bäume all in ihren Grenzen.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Er sprach; da kamen Heuschrecken und Ungeziefer ohne Zahl.
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 Sie fraßen alles Gras in ihrem Land und fraßen ihre Feldfrucht ab.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 In ihrem Lande schlug er alle Erstgeburt, die Erstlinge all ihrer Kraft. -
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Er führte sie mit Gold und Silber aus dem Lande, und unter seinen Stämmen war kein Müder.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Ägypten ward ob ihres Wegzugs froh; denn Angst vor ihnen hatte sie befallen.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Er breitete zum Schirme eine Wolke aus und Feuer, um bei Nacht zu leuchten.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 Auf ihre Bitte ließ er Wachteln kommen und schenkte ihnen Himmelsspeise zur Genüge.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Er öffnete den Fels, daß Wasser flossen, in dürrem Lande Ströme rieselten.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 Denn er gedachte seines heiligen Wortes und seines Dieners Abraham.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 So führte er sein Volk mit Jubel fort, mit Jauchzen seine Auserwählten.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 Der Heiden Länder gab er ihnen, ließ sie die Frucht des Völkerfleißes erben,
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 auf daß sie seine Rechte hielten, und seine Lehren treu bewahrten. Alleluja!
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalm 105 >