< Sprueche 7 >

1 Mein Sohn, behalte meine Reden! Bei dir verwahr, was ich dich heiße!
Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
2 Bewahr dir meine Vorschriften, so wirst du leben, und meine Weisung wie den Augapfel!
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Bind sie an deine Finger! Auf deines Herzens Tafel schreibe sie!
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Zur Weisheit sprich: "Du bist mir Schwester", nenn Einsicht deine Freundin,
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 auf daß sie dich vor einem andere Weib bewahre, vor einer Fremden, die einschmeichelnd redet!
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 Durchs Fenster meines Hauses, durchs Gitter schaute ich hinaus.
Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
7 Da sah ich einen Jüngling bei den noch Unerfahrenen, bemerkte bei den jungen Leuten einen Unvorsichtigen,
Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
8 der auf der Gasse nahe einer Ecke ging und in der Richtung meines Hauses schritt
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9 in Dämmerung, am Abende des Tags, in stiller Nachtzeit, in der Dunkelheit.
Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 Da tritt auf einmal ihm das Weib entgegen im Dirnenanzug mit geschnürter Brust.
Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 Unruhig trieb sie sich herum; zu Hause hatten ihre Füße keine Ruhe.
(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 Ein Schritt jetzt auf die Straße und auf den Markt ein Schritt; sie lauerte an jeder Ecke.
Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 Jetzt hascht sie ihn, küßt ihn; mit frecher Miene redet sie ihn an:
Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 "Schlachtopfer darzubringen, lag mir ob; ich habe heute mein Gelübde nun entrichtet.
“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 Deswegen bin ich ausgegangen, um dich zu suchen. Ich habe dich gefunden.
Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 Mit Decken habe ich bedeckt mein Lager, mit buntem Linnen aus Ägypten.
Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 Mit Myrrhen habe ich besprengt mein Lager, mit Aloë und Zimtgewürz.
Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 So komm! Wir wollen bis zum Morgen an der Liebe uns berauschen, in Liebe uns genießen.
Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 Der Mann ist nicht daheim; er zog auf Reisen in die Ferne.
Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
20 Er nahm den Beutel samt dem Gelde mit sich; am Vollmondstag erst kehrt er wieder heim."
Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 So bringt sie ihn herum durch ihr verführerisches Reden und reißt ihn fort durch ihre glatten Lippen.
Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 Er folgt ihr nach, der Harmlose, gleich einem Stier, den man zur Schlachtbank führt, gleich einem Hund zum Stricke,
Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 gleich einem Hirsch dahin, wo ihm ein Pfeil die Leber spaltet, gleich einem Vogel, der zur Schlinge eilt, und merkt es nicht, daß es sein Leben gilt.
mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 Nun, Söhne, horcht auf mich! Auf meines Mundes Reden merket!
Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
25 Laß nicht dein Herz zu ihren Wegen biegen! Verirr dich nicht auf ihre Steige!
Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
26 Denn viel sind der Erschlagenen, die sie gefällt, und viele sind's, die sie gemordet.
Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Die Wege, die zu ihrem Hause führen, sind Wege zu der Unterwelt. Sie führen zu des Todes Kammern. (Sheol h7585)
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)

< Sprueche 7 >