< Job 8 >

1 Darauf erwidert Bildad von Schuach:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 "Wie lange willst du solches reden und wüten mit der Worte Sturm?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Ist Gott etwa ein Rechtsverdreher? Und beugt gerechte Sache der Allmächtige?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Wenn deine Kinder gegen ihn gesündigt und er sie um der Sünde willen in den Tod geschickt,
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 so solltest du an Gott dich wenden und zum Allmächtigen um Gnade flehen.
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Dann würde er dir Schutz gewähren, falls du nur rein und lauter bist, und stellte auch die Wohnung wieder her, die dir gebührt.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Dann würde auch dein früheres Los gering erscheinen, die Zukunft aber herrlich für dich sein.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Befrage dich bei den vergangenen Zeiten; gib auf der Väter Weisheit acht!
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 Wir sind von gestern, unerfahren; denn wie ein Schatten sind auf Erden unsere Tage.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Doch jene, können sie dich nicht belehren? Sie geben tiefgeschöpftes Wissen.
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Wird etwa Schilfkraut ohne Sumpf sehr hoch? Wird Gras, wo Wasser fehlt, recht groß?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Noch ist's im Trieb, nicht reif zum Schnitt, und schon ist's dürr, grünt alles andere noch.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 So geht's mit allen Gottvergessenen. So wird des Frevlers Stolz vernichtet,
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 er, dessen Zuversicht nur Sommerfäden und dessen Hoffnung Spinngewebe sind.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Er stützt sich auf sein Haus; doch hält's nicht stand. Er hält sich fest daran; doch bleibt's nicht stehen.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Wenn er auch in der Sonne grünt und seine Ranken weit in seinen Garten gehen,
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Verflechten seine Wurzeln sich zuhauf, wie ein Gemäuer anzusehen,
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 wenn er von seinem Ort ihn tilgt, verleugnet dieser ihn: 'Ich habe niemals dich gesehen!'
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Das ist da seines Schicksals 'Wonne', und andere steigen aus dem Staub empor.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Den Frommen kann Gott nicht verachten; der Übeltäter Hand hält er nicht fest. -
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Dein Mund wird noch des Lachens voll und voll von Jubel deine Lippen.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Und deine Hasser kleiden sich in Schande, und nicht mehr ist der Bösen Zelt."
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >