< Job 35 >

1 Und wieder hob Elihu an und sprach:
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 "Ja, hältst du das für Recht und meinst du das mit 'meinem Rechthaben vor Gott'?
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 Du sagst: 'Was nützt es Dir? Was nützt es mir, wenn ich nicht sündige?'
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 Ich will dir drauf die Antwort geben und deinen Freunden hier bei dir.
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Schau auf zum Himmel; sieh! Blick zu den hohen Wolken über dir empor!
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 Du hast gesündigt. Was tust du ihm damit? Sind deiner Sünden noch so viel, was machst du ihm damit?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 Und bist du fromm, was schenkst du ihm? Was nur empfängt er da aus deiner Hand?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 Doch deinesgleichen geht dein Frevel an, die Menschenkinder deine Frömmigkeit.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 Man schreit wohl über der Bedrückung Menge, führt Klage ob der Großen Macht.
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 Doch niemand fragt: 'Wo bleibt da Gott, mein Schöpfer, der in der Nachtzeit spricht,
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 der vor des Feldes Tieren uns belehrt, uns vor des Himmels Vögeln Weisheit schenkt?'
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Dann schreit man ob des Übermuts der Bösen; doch er schenkt kein Gehör.
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Zu nichts führt es, so sagst du, nimmer höre Gott, und der Allmächtige seh' dies Treiben nicht,
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 zumal du sagst, du könnest ihn nicht sehen; der Streitfall liege ihm zwar vor, du aber müßtest immer auf ihn warten,
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 und weil er sich nicht zeige, so strafe er im Zorne; er wolle nichts von Urteil wissen.
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 Da redet Job denn doch gar unvernünftig; er macht viel Redens ohne Einsicht."
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

< Job 35 >