< Job 22 >

1 Darauf erwidert Eliphaz von Teman mit den Worten:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 "Hat Gott von einem Manne Nutzen? Nein, nur zum eigenen Nutzen ist man fromm.
“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
3 Hat der Allmächtige etwas von deiner Tugend, Gewinn von deiner Lauterkeit?
Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
4 Zeiht er dich etwa deiner Frömmigkeit und zieht dich deshalb vor Gericht?
“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
5 Kann nicht dein Frevel mannigfaltig sein und deine Sünden ohne Maß?
Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
6 Gewiß hast du den Bruder ohne Grund gepfändet und Nackten ihre Kleider ausgezogen.
Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
7 Dem Müden hast du keinen Trunk gespendet und Hungrigen das Brot versagt.
Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
8 'Dem Mann der Faust gehört das Land, und nur der Stolze darf drin wohnen', so dachtest du.
ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
9 So hast du Witwen hilflos ziehen lassen; die Waisen hat dein Arm bedrückt.
Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
10 Deshalb sind Schlingen rings um dich und ängstigt jählings dich der Schrecken.
Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
11 Ist's nicht so, daß du gar nichts siehst, wenn Finsternis und Wasserwolken dich bedecken?
nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
12 Nun, ist nicht Gott so hoch in Himmelshöhen? Schau nur empor, wie hoch der Sterne Haupt!
“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
13 Da denkst du wohl: Wie kann denn Gott etwas bemerken? Kann er denn hinterm Wolkendunkel etwas unterscheiden?
Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
14 Umschleiern ihn doch Wolken, daß er nichts sehen kann, und auch der Himmelskreis ist in Bewegung.'
Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
15 Willst du denn von der Vorzeit Pfaden den betreten, den jene alten Sünder gingen?
Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
16 Sie, die gepackt zur Unzeit wurden, und deren Sein die Wasserflut verschlang,
Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
17 die einst zu Gott gesprochen: 'Bleib uns fern!' - Was tat doch ihnen der Allmächtige?
Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
18 Er, der mit Segen ihre Häuser füllte. Der Plan mit diesen Frevlern ist mir unbegreiflich. -
Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
19 Die Frommen sehen es noch heut und freuen sich; der Schuldlose verspottet sie!
“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
20 'Ist unser Widersacher nicht vernichtet? Und seinen Rest verzehrte noch das Feuer.'
Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
21 Vertrau allein auf ihn, so hast du Frieden! Durch jene wird dir reichlicher Gewinn.
“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
22 Laß dich von seinem Mund belehren! Zu Herzen nimm dir seine Worte!
Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
23 Wenn du gebessert zum Allmächtigen dich kehrst, entfernst aus deinem Zelte unrecht Gut,
Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
24 Golderz für Staub erachtend und für der Bäche Kiesel Ophirgold,
ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
25 daß dir so der Allmächtige zum Goldberg wird, zu einem Silberhaufen,
Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
26 dann kannst du vorm Allmächtigen dich dem verwöhnten Kinde gleich gebärden und kannst dein Angesicht zu Gott erheben.
Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
27 Du bittest ihn, er hört auf dich; was du gelobt, kannst du erfüllen.
Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
28 Was du dir vornimmst, wird dir glücken, und hell vor dir liegt deine Straße.
Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
29 Wenn du in Demut Hochmut eingestanden, dann hilft er auch dem Demutsvollen.
Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
30 So rettet er den Nichtschuldlosen; doch wird er nur gerettet durch deiner Hände Reinigung."
Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”

< Job 22 >