< Nombres 16 >

1 Et Coré, fils de Jitsehar, fils de Kahath, fils de Lévi, forma un parti avec Dathan et Abiram, fils d'Eliab, et On, fils de Peleth, ceux-ci fils de Ruben;
Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
2 et ils se soulevèrent contre Moïse avec deux cent cinquante hommes des enfants d'Israël, Princes de l'Assemblée, appelés au Conseil, personnages notables,
ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
3 et ils se réunirent contre Moïse et Aaron, et ils leur dirent: Vous en faites trop! Car cette Assemblée! c'est tout autant d'hommes consacrés, et l'Éternel est au milieu d'eux; pourquoi donc vous élevez-vous au-dessus de l'Assemblée de l'Éternel?
Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
4 A l'ouïe de ces propos Moïse se jeta la face contre terre,
Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
5 et s'adressant à Coré et à toute sa faction il leur dit: Demain l'Éternel fera connaître qui est à Lui et qui est consacré pour lui donner accès auprès de Lui; et celui qu'il choisira, Il lui donnera accès auprès de Lui.
Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
6 Faites ceci: Prenez des encensoirs, Coré et tout son parti,
Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
7 et mettez-y du feu et jetez-y de l'encens devant l'Éternel, demain, et c'est l'homme que choisira l'Éternel, qui sera le consacré. Vous en faites trop, enfants de Lévi!
ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
8 Et Moïse dit à Coré: Écoutez donc, enfants de Lévi!
Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
9 Est-ce trop peu pour vous que le Dieu d'Israël vous ait triés dans l'Assemblée d'Israël pour vous donner accès auprès de Lui pour faire le service de la Résidence de l'Éternel, et pour paraître devant l'Assemblée officiant pour elle?
Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
10 A toi et à tous tes frères, enfants de Lévi avec toi, Il donne accès auprès de Lui, et vous prétendez encore au Sacerdoce!
Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
11 C'est pour cela que vous vous liguez toi et tout ton parti contre l'Éternel; Aaron en effet, qui est-il pour que vous murmuriez contre lui?
Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
12 Et Moïse envoya mander Dathan et Abiram, fils d'Eliab. Mais ils dirent: Nous n'irons point.
Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
13 N'est-ce pas assez de nous avoir tirés d'un pays découlant de lait et de miel pour nous faire périr dans le désert, que tu t'ériges en dominateur au-dessus de nous?
Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
14 Tu ne nous as point non plus conduits dans un pays découlant de lait et de miel, ni mis en possession de champs et de vignes. Veux-tu arracher les yeux à ces hommes? Nous n'irons point.
Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
15 Alors Moïse fut fort irrité et il dit à l'Éternel: Ne regarde pas leur offrande! Je ne leur ai pas enlevé un âne, et n'ai pas fait tort à un d'eux.
Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
16 Et Moïse dit à Coré: Demain paraissez, toi et tout ton parti, devant l'Éternel, toi et eux avec Aaron,
Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
17 et prenez chacun votre encensoir, et y mettez de l'encens, et apportez devant l'Éternel chacun votre encensoir, deux cent cinquante encensoirs; et toi et Aaron vous viendrez aussi chacun avec son encensoir.
Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
18 Ils prirent donc chacun leur encensoir, et y mirent du feu et y jetèrent de l'encens, et ils parurent à la porte de la Tente du Rendez-vous, ainsi que Moïse et Aaron.
Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
19 Et Coré en opposition avec eux convoqua toute l'Assemblée à la porte de la Tente du Rendez-vous. Alors la gloire de l'Éternel apparut à toute l'Assemblée.
Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
20 Et l'Éternel parla à Moïse et Aaron en ces termes:
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
21 Séparez-vous de ce parti-là: je vais l'exterminer à l'instant.
“Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
22 Et ils se jetèrent face contre terre, et dirent: O Dieu, Dieu des esprits de toute chair, un homme seul a péché: t'irriteras-tu contre toute l'Assemblée?
Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
23 Et l'Éternel dit à Moïse:
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
24 Parle à l'Assemblée en ces termes: Retirez-vous de tous les côtés à distance de la demeure de Coré, de Dathan et d'Abiram.
“Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
25 Alors Moïse se leva et se rendit chez Dathan et Abiram, et il fut suivi par les Anciens d'Israël.
Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
26 Et il dit à l'Assemblée: Éloignez-vous des tentes de ces sacrilèges, et ne touchez rien de ce qui est à eux, afin que vous ne soyez pas emportés par tous leurs péchés.
Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
27 Et ils s'éloignèrent de tous les côtés à distance de la demeure de Coré, et de Dathan et d'Abiram. Et Dathan et Abiram sortirent et se placèrent à la porte de leurs tentes avec leurs femmes, leurs fils, et leurs enfants.
Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
28 Et Moïse dit: A ceci vous reconnaîtrez que l'Éternel m'a donné la mission de faire tout ce qui a été fait, et que je n'ai pas agi de mon chef:
Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
29 Si ces gens meurent de la mort commune à tous les hommes, et subissent la dispensation commune à tous les hommes, ce n'est pas l'Éternel qui m'a envoyé;
Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
30 mais si l'Éternel crée un fait inouï, et si la terre s'entr'ouvre et les engloutit eux et tout ce qui est à eux, et qu'ils descendent vivants aux Enfers, vous reconnaîtrez que ces gens-là ont répudié l'Éternel. (Sheol h7585)
Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
31 Et lorsqu'il eut achevé de prononcer toutes ces paroles, le sol qui était sous leurs pieds se fendit,
Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
32 et la terre s'entr'ouvrit et les engloutit eux et leurs maisons, et tous les hommes qui tenaient à Coré, et tout leur avoir, et
ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
33 ils descendirent avec tout ce qu'ils possédaient, vivants dans les Enfers, et la terre les recouvrit et ils furent exterminés du milieu de l'Assemblée. (Sheol h7585)
Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
34 Et à leurs cris tous les Israélites qui les entouraient s'enfuirent; car ils disaient: Nous craignons que la terre ne nous engloutisse.
Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
35 Et un feu envoyé par l'Éternel consuma les deux cent cinquante hommes qui avaient offert l'encens.
Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
36 Et l'Éternel parla à Moïse en ces termes:
Yehova anawuza Mose kuti,
37 Dis à Eléazar, fils du Prêtre Aaron, de retirer de l'incendie les encensoirs, et jettes-en le feu au loin, car ce sont choses sacrées,
“Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
38 ces encensoirs de ces hommes qui ont perdu la vie pour leurs péchés; et qu'on les étende en lames dont on plaquera l'Autel; car on les a présentés devant l'Éternel et ils sont devenus sacrés, et ce sera un monument pour les enfants d'Israël.
Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
39 Alors le Prêtre Eléazar prit les encensoirs d'airain qu'avaient présentés les incendiés, et on en fit des lames dont on plaqua l'Autel,
Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
40 pour rappeler ce souvenir aux enfants d'Israël, afin qu'aucun étranger n'appartenant pas à la race d'Aaron ne s'approchât pour brûler l'encens devant l'Éternel et qu'il ne lui advînt comme à Coré et à son parti, ainsi que l'Éternel l'avait dit par l'organe de Moïse.
monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
41 Et il y eut des murmures de toute l'Assemblée des enfants d'Israël le lendemain contre Moïse et contre Aaron; ils disaient: Vous avez fait mourir le peuple de l'Éternel.
Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
42 Et comme l'Assemblée s'attroupait contre Moïse et contre Aaron, ceux-ci se dirigèrent vers la Tente du Rendez-vous; et voici, la nuée la couvrit, et la Gloire de l'Éternel apparut.
Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
43 Et Moïse et Aaron arrivèrent devant la Tente du Rendez-vous.
Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
44 Et l'Éternel parla à Moïse en ces termes:
ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
45 Otez-vous du milieu de cette Assemblée, car je vais la consumer soudain. Alors ils se jetèrent face contre terre.
“Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
46 Et Moïse dit à Aaron: Prends l'encensoir et y mets du feu pris sur l'Autel, et y jette de l'encens, et le promène en hâte dans l'Assemblée, et fais la propitiation pour eux; car l'Éternel a donné cours à Sa colère, le fléau a commencé.
Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
47 Et Aaron prit [l'encensoir], comme avait dit Moïse, et courut au milieu de l'Assemblée, et voilà que le fléau avait commencé parmi le peuple; et il offrit l'encens et fit la propitiation pour le peuple.
Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
48 Et il se plaça entre les morts et les vivants, et le fléau fut arrêté.
Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
49 Et il y eut quatorze mille sept cents personnes qui périrent par ce fléau, sans compter ceux qui étaient morts à propos de Coré.
Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
50 Et Aaron revint auprès de Moïse à l'entrée de la Tente du Rendez-vous, et le fléau était arrêté.
Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.

< Nombres 16 >