< Luc 21 >

1 Ayant levé les yeux, Jésus vit des riches qui mettaient leurs offrandes dans le trésor du temple.
Yesu atayangʼana, anaona olemera akuyika mphatso zawo mu chosungira ndalama za mʼNyumba ya Mulungu.
2 Il vit aussi une pauvre veuve qui y mettait deux pites.
Iye anaonanso mkazi wamasiye wosauka akuyikamo timakopala tiwiri.
3 Et il dit: Je vous dis en vérité, que cette pauvre veuve a plus mis que personne.
Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mkazi wamasiye wosaukayu wapereka zambiri kuposa ena onsewa.
4 Car tous ceux-là ont mis, dans les offrandes de Dieu, de leur superflu; mais celle-ci y a mis de son nécessaire tout ce qu'elle avait pour vivre.
Anthu onsewa atapa mphatso zawo kuchokera pa zochuluka zimene ali nazo; koma uyu, mwa umphawi wake, wapereka zonse zimene ali nazo.”
5 Et comme quelques-uns disaient que le temple était orné de belles pierres et d'offrandes, il dit:
Ena mwa ophunzira ake ankachita ndemanga za mmene Nyumba ya Mulungu anayikongoletsera ndi miyala yokongola ndiponso zinthu zina zomwe anthu anapereka kwa Mulungu. Koma Yesu anati,
6 Vous contemplez ces choses! Des jours viendront où il n'y sera laissé pierre sur pierre, qui ne soit renversée.
“Koma zimene mukuziona panozi, nthawi idzafika pamene ngakhale mwala umodzi omwe sudzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
7 Et ils lui demandèrent: Maître, quand donc ces choses arriveront-elles, et par quel signe connaîtra-t-on qu'elles sont sur le point d'arriver?
Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, kodi zonsezi zidzachitika liti? Ndipo tidzaonera chiyani kuti zili pafupi kuchitika?”
8 Et il dit: Prenez garde de ne pas être séduits; car plusieurs viendront en mon nom, disant: C'est moi qui suis le Christ, et le temps approche. Ne les suivez donc pas.
Iye anayankha kuti, “Chenjerani kuti musanyengedwe. Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati ‘Ine ndine Iye’ ndi kuti ‘Nthawi yayandikira.’ Musadzawatsate iwo.
9 Or quand vous entendrez parler de guerres et de séditions, ne vous épouvantez pas; car il faut que ces choses arrivent auparavant; mais ce ne sera pas si tôt la fin.
Mukadzamva zankhondo ndi zipolowe, musadzachite mantha. Zinthu izi ziyenera kuchitika poyamba, koma chimaliziro sichidzafika nthawi yomweyo.”
10 Il leur dit aussi: Une nation s'élèvera contre une autre nation, et un royaume contre un autre royaume;
Kenaka anawawuza kuti, “Mtundu wa anthu udzawukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu kuwukira ufumu wina.
11 Et il y aura de grands tremblements de terre en divers lieux, et des famines et des pestes; et il paraîtra des choses épouvantables, et de grands signes dans le ciel.
Kudzakhala zivomerezi zazikulu, njala ndi miliri mʼmalo osiyanasiyana, ndi zinthu zoopsa ndi zizindikiro zamphamvu kuchokera kumwamba.
12 Mais, avant tout cela, ils mettront les mains sur vous, et vous persécuteront, vous livrant aux synagogues, et vous mettant en prison, et vous menant devant les rois et devant les gouverneurs, à cause de mon nom.
“Koma zonsezi zisanachitike, adzakugwirani ndi kukuzunzani. Adzakuperekani ku masunagoge ndi ku ndende, ndipo adzakutengerani pamaso pa mafumu ndi olamulira, ndipo zonsezi zidzachitika chifukwa cha dzina langa.
13 Et cela sera pour vous une occasion de témoignage.
Umenewu udzakhala mwayi wanu ochitira umboni.
14 Mettez-vous donc dans l'esprit de ne point préméditer votre défense.
Koma tsimikizani mtima kuti musadzade nkhawa za momwe mudzadzitchinjirizire.
15 Car je vous donnerai une bouche et une sagesse à laquelle tous vos adversaires ne pourront contredire, ni résister.
Pakuti Ine ndidzakupatsani mawu ndi nzeru kotero kuti palibe mmodzi wa adani anu adzathe kuwakana kapena kuwatsutsa.
16 Vous serez même livrés par vos parents, par vos frères, par vos proches et par vos amis; et ils feront mourir plusieurs d'entre vous.
Inu mudzaperekedwa ndi makolo anu, abale, anansi ndi abwenzi anu ndipo ena mwa inu adzakuphani.
17 Et vous serez haïs de tout le monde, à cause de mon nom.
Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine.
18 Mais il ne se perdra pas un cheveu de votre tête.
Koma palibe tsitsi limodzi la mʼmutu mwanu lidzawonongeke.
19 Possédez vos âmes par votre patience.
Mukadzalimbikira ndiye mudzapeze moyo.
20 Et quand vous verrez Jérusalem environnée par les armées, sachez que sa désolation approche.
“Mukadzaona Yerusalemu atazingidwa ndi magulu ankhondo, inu mudzadziwe kuti kuwonongeka kwake kuli pafupi.
21 Alors, que ceux qui seront dans la Judée s'enfuient aux montagnes; que ceux qui seront au milieu de Jérusalem se retirent; et que ceux qui seront à la campagne ne rentrent point.
Pamenepo amene ali ku Yudeya adzathawire ku mapiri, amene ali mu mzinda adzatulukemo, ndi amene ali ku midzi asadzalowe mu mzinda.
22 Car ce seront des jours de châtiment, afin que toutes les choses qui sont écrites s'accomplissent.
Pakuti iyi ndi nthawi yachilango pokwaniritsa zonse zimene zinalembedwa.
23 Malheur aux femmes enceintes, et à celles qui allaiteront en ces jours-là; car il y aura une grande calamité sur ce pays, et de la colère contre ce peuple.
Zidzakhala zoopsa nthawi imenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! Kudzakhala masautso aakulu mʼdziko ndipo anthu onse adzawakwiyira.
24 Ils tomberont sous le tranchant de l'épée, et ils seront menés captifs parmi toutes les nations, et Jérusalem sera foulée par les nations, jusqu'à ce que les temps des nations soient accomplis.
Iwo adzaphedwa ndi lupanga ndi kutengedwa ukapolo kupita ku mayiko wonse. Yerusalemu adzaponderezedwa ndi anthu a mitundu ina mpaka nthawi ya a mitundu ina itakwaniritsidwa.
25 Et il y aura des signes dans le soleil, dans la lune et dans les étoiles; et sur la terre, les peuples seront dans la consternation et ne sachant que devenir, la mer et les flots faisant un grand bruit.
“Padzakhala zizindikiro zodabwitsa pa dzuwa, mwezi ndi nyenyezi. Pa dziko lapansi, mitundu ya anthu idzakhala mʼmasautso ndipo idzathedwa nzeru pakumva mkokomo ndi mafunde a mʼnyanja.
26 Les hommes seront comme rendant l'âme de frayeur, dans l'attente des choses qui surviendront dans le monde; car les puissances des cieux seront ébranlées.
Anthu adzakomoka chifukwa cha mantha, akadzamva za zimene zikubwera pa dziko lapansi, pakuti zinthu zamlengalenga zidzagwedezeka.
27 Et alors ils verront venir le Fils de l'homme sur une nuée, avec une grande puissance et une grande gloire.
Nthawi imeneyo adzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
28 Or quand ces choses commenceront d'arriver, regardez en haut, et levez la tête, parce que votre délivrance approche.
Zinthu izi zikadzayamba kuchitika, mudzayimirire ndi kutukula mitu yanu, chifukwa chipulumutso chanu chayandikira.”
29 Et il leur dit une similitude: Voyez le figuier et tous les arbres;
Iye anawawuza fanizo ili, “Taonani mtengo wamkuyu ndi mitengo ina yonse.
30 Quand ils poussent, vous jugez de vous-mêmes, en les voyant, que l'été est proche.
Ikamatulutsa masamba, mumakhoza kudzionera nokha ndi kudziwa kuti dzinja lili pafupi.
31 De même, lorsque vous verrez arriver ces choses, sachez que le royaume de Dieu est proche.
Chimodzimodzinso, mukadzaona zinthu zonsezi, dziwani kuti ufumu wa Mulungu uli pafupi.
32 Je vous dis en vérité, que cette génération ne passera point, que toutes ces choses n'arrivent.
“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika.
33 Le ciel et la terre passeront, mais mes paroles ne passeront point.
Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
34 Prenez donc garde à vous-mêmes, de peur que vos cœurs ne soient appesantis par la débauche, par l'ivrognerie et par les inquiétudes de cette vie; et que ce jour-là ne vous surprenne subitement.
“Samalani, kuti mitima yanu ingalemetsedwe ndi maphwando, kuledzera ndi kudera nkhawa za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingadzakupezeni modzidzimutsa ngati msampha.
35 Car il surprendra comme un filet tous ceux qui habitent sur la face de la terre.
Pakuti lidzafika pa onse okhala pa dziko lonse lapansi.
36 Veillez donc, et priez en tout temps, afin que vous soyez trouvés dignes d'éviter toutes ces choses qui doivent arriver, et de subsister devant le Fils de l'homme.
Khalani tcheru nthawi zonse ndi kupemphera kuti inu mudzathe kuthawa zonse zimene zili pafupi kuchitika, ndi kuti mudzathe kuyima pamaso pa Mwana wa Munthu.”
37 Or, Jésus enseignait dans le temple pendant le jour, et, la nuit, il sortait et se tenait sur la montagne appelée des Oliviers.
Tsiku lililonse Yesu amaphunzitsa ku Nyumba ya Mulungu, ndi madzulo ali wonse Iye amachoka kukakhala pa phiri la Olivi usiku wonse.
38 Et, dès le point du jour, tout le peuple venait à lui dans le temple pour l'écouter.
Ndipo anthu onse amabwera mmamawa kudzamumva Iye ku Nyumba ya Mulungu.

< Luc 21 >