< Luc 6 >

1 Le jour du second-premier sabbat, Jésus passant par des blés, ses disciples arrachaient des épis et les mangeaient, après les avoir froissés dans leurs mains.
Tsiku lina la Sabata Yesu ankadutsa mʼminda yatirigu, ndipo ophunzira ake anayamba kubudula ngala zatirigu, namazifikisa mʼmanja mwawo ndi kumadya.
2 Des pharisiens dirent: «Pourquoi faites-vous ce qui n'est pas permis le jour du sabbat?»
Ena mwa Afarisi anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mukuchita zosaloledwa pa tsiku la Sabata?”
3 Et Jésus prenant la parole, leur dit: «N'avez-vous pas lu ce que fit David, lorsqu'il eut faim, lui et ceux qui étaient avec lui:
Yesu anawayankha iwo kuti, “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita pamene iye ndi anzake anali ndi njala?
4 comment il entra dans la maison de Dieu, prit les pains de proposition, en mangea, et en donna même à ceux qui l'accompagnaient, quoiqu'il ne soit permis qu'aux sacrificateurs d'en manger?»
Iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndipo atatenga buledi wopatulika anadya amene ndi ololedwa kudya ansembe okha. Ndipo anaperekanso wina kwa anzake.”
5 Et il ajouta: «Le Fils de l'homme est maître même du sabbat.»
Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Mwana wa Munthu ndi Ambuye wa Sabata.”
6 Il lui arriva, un autre jour de sabbat, d'entrer dans la synagogue, et d'y enseigner. Il y avait là un homme dont la main droite était sèche.
La Sabata lina Iye analowa mʼsunagoge kukaphunzitsa ndipo mʼmenemo anapeza munthu wadzanja lolumala.
7 Les scribes et les pharisiens observaient Jésus, pour voir s'il faisait des guérisons le jour du sabbat, afin d'avoir sujet de l'accuser.
Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo ankamuyangʼana kuti apeze chifukwa Yesu, choncho anamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati Iye akanamuchiritsa pa Sabata.
8 Jésus pénétrant leurs pensées, dit à l'homme qui avait la main sèche: «Lève-toi, et tiens-toi là au milieu; » et lui, s'étant levé, se tint debout.
Koma Yesu anadziwa zimene ankaganiza ndipo anati kwa munthu wadzanja lolumalayo, “Tanyamuka ndipo uyime patsogolo pa onsewa.” Choncho iye ananyamuka nayima pamenepo.
9 Jésus leur dit: «Je vous demande s'il est permis, le jour du sabbat, de faire bien ou de faire mal, de sauver la vie ou de l'ôter?»
Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Ndikufunseni, kodi chololedwa pa Sabata ndi chiti: kuchita chabwino kapena kuchita choyipa, kupulumutsa moyo kapena kuwononga?”
10 Puis, ayant promené ses regards sur eux tous, il dit à cet homme: «Étends la main.» Il le fit, et sa main fut guérie.
Iye atawayangʼana onsewo, anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye anaterodi, ndipo dzanja lake linachiritsidwa.
11 Les scribes et les pharisiens furent remplis de fureur; et ils conféraient ensemble pour savoir ce qu'ils feraient à Jésus.
Koma iwo anapsa mtima nayamba kukambirana wina ndi mnzake chomwe akanamuchitira Yesu.
12 En ce temps-là, Jésus se rendit à la montagne pour prier Dieu, et il passa toute la nuit en prière.
Tsiku lina, masiku amenewo, Yesu anapita ku phiri kukapemphera ndipo anakhala usiku wonse akupemphera kwa Mulungu.
13 Quand il fit jour, il appela ses disciples, et en choisit douze, auxquels il donna le nom d'Apôtres,
Kutacha, anayitana ophunzira ake ndipo anasankha khumi ndi awiri a iwo amene anawayika kukhala atumwi:
14 savoir, Simon, qu'il appela Pierre, et André son frère, Jacques, Jean, Philippe, Barthélemi,
Simoni (amene anamutcha Petro), mʼbale wake wa Andreya, Yakobo, Yohane, Filipo, Bartumeyu,
15 Matthieu, Thomas, Jacques fils d'Alphée, Simon appelé le zélateur,
Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alufeyo, Simoni amene amatchedwa Zaleti,
16 Jude fils de Jacques, et Judas Iscariot, qui fut un traître.
Yudasi mwana wa Yakobo ndi Yudasi Isikarioti amene anamupereka.
17 Il descendit avec eux et s'arrêta sur un plateau, où se trouvaient une foule de ses disciples, et une multitude de gens qui étaient venus de toute là Judée, de Jérusalem et du littoral de Tyr et de Sidon, pour l'entendre et pour être guéris de leurs maladies.
Iye anatsika pamodzi ndi atumwiwo ndipo anayima pamalo athyathyathya. Gulu lalikulu la ophunzira ake, gulu lalikulu la anthu ochokera ku Yudeya konse, ku Yerusalemu ndi ochokera mʼmphepete mwa nyanja ya Turo ndi Sidoni anali pomwepo.
18 Ceux qui étaient tourmentés par des esprits impurs étaient guéris;
Iwo anabwera kudzamvetsera ndi kuchiritsidwa ku matenda awo. Osautsidwa ndi mizimu yoyipa anachiritsidwa,
19 et toute la foule cherchait à le toucher, parce qu'il sortait de sa personne une vertu qui les guérissait tous.
ndipo anthu ankayesetsa kuti amukhudze chifukwa mphamvu imatuluka mwa Iye ndi kuchiritsa onse.
20 Alors, levant les yeux sur ses disciples, il dit: «Vous êtes bienheureux, vous qui êtes pauvres, parce que le royaume de Dieu est à vous.
Akuyangʼana ophunzira ake, Iye anati, “Odala ndinu amene ndi osauka, chifukwa ufumu wa Mulungu ndi wanu.
21 Vous êtes bienheureux, vous qui avez faim maintenant, parce que vous serez rassasiés. Vous êtes bienheureux, vous qui pleurez maintenant, parce que vous rirez.
Inu amene mukumva njala tsopano, ndinu odala chifukwa mudzakhutitsidwa. Inu amene mukulira tsopano, ndinu odala chifukwa mudzasekerera.
22 Bienheureux serez-vous, quand on vous haïra, quand on vous chassera, qu'on vous insultera et qu'on rejettera votre nom comme un nom infâme, à cause du Fils de l'homme.
Ndinu odala, anthu akamakudani, kukusalani ndi kukunyozani ndi kumayipitsa dzina lanu chifukwa cha Mwana wa Munthu.
23 Réjouissez-vous en ce jour-là et bondissez de joie, car votre récompense est grande dans le ciel: c'est ainsi que leurs pères traitaient les prophètes.
“Nthawi imeneyo sangalalani ndipo lumphani ndi chimwemwe chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba. Pakuti ndi zomwezonso zimene makolo awo anachitira aneneri.
24 Mais, malheur à vous, riches, parce que vous avez déjà votre consolation!
“Ndinu atsoka, anthu olemera, popeza mwalandiriratu zokusangalatsani.
25 Malheur à vous, rassasiés, parce que vous aurez faim! Malheur à vous, qui riez maintenant, parce que vous serez dans l'affliction et que vous pleurerez!
Tsoka inu amene mukudya bwino tsopano, chifukwa mudzakhala ndi njala. Ndinu atsoka, amene mukusekerera tsopano, chifukwa mudzabuma ndi kulira.
26 Malheur à vous, lorsque tous les hommes diront du bien de vous, car c'est ce que leurs pères faisaient à l'égard des faux prophètes!
Ndinu atsoka, anthu akamakuyamikirani, popeza makolo anu anawachitira aneneri onama zomwezi.”
27 Mais je vous dis, à vous qui m'écoutez, aimez vos ennemis; faites du bien à ceux qui vous haïssent;
“Koma Ine ndikuwuza inu amene mukundimva: Kondani adani anu, chitirani zabwino amene amakudani.
28 bénissez ceux qui vous maudissent; priez pour ceux qui vous maltraitent.
Dalitsani amene amakutembererani, apempherereni amene amakusautsani.
29 Si quelqu'un te frappe sur une joue, présente-lui l'autre, et si quelqu'un t'enlève ton manteau, laisse-lui prendre aussi ta tunique.
Ngati wina akumenyani patsaya limodzi mupatseninso tsaya linalo. Ngati wina akulanda mwinjiro wako, umulole atenge ndi mkanjo omwe.
30 Donne à tout homme qui te demande, et ne réclame pas ton bien à celui qui te le prend.
Mupatseni aliyense amene akupemphani kanthu ndipo ngati wina atenga chinthu chanu, musamulamule kuti akubwezereni.
31 Comme vous voulez que les hommes fassent pour vous, faites de même pour eux.
Inu muwachitire anthu ena, zomwe mukanafuna kuti iwo akuchitireni.
32 Si vous aimez ceux qui vous aiment, quel gré vous en doit-on savoir? Les pécheurs aussi aiment ceux qui les aiment.
“Ngati mukonda okhawo amene amakukondani, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amakonda amene amawakondanso.
33 Si vous faites du bien à ceux qui vous en font, quel gré vous en doit-on savoir? Les pécheurs aussi en font autant.
Ndipo ngati muchita zabwino kwa amene ndi abwino kwa inu, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amachita izi.
34 Si vous prêtez à ceux de qui vous espérez être remboursés, quel gré vous en doit-on savoir?» Des pécheurs aussi prêtent à des pécheurs, afin qu'on leur rende la pareille.
Ndipo ngati mukongoza amene mukuyembekeza kuti abweza, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amabwereketsa kwa ochimwa anzawo, ndipo amayembekezera kubwezeredwa zonse.
35 Mais aimez vos ennemis, faites du bien, et prêtez sans rien espérer: votre récompense sera grande; et vous serez fils du Très-Haut, car il est bon envers les ingrats et les méchants.
Koma kondani adani anu, achitireni zabwino, akongozeni koma osayembekezera kulandira kanthu. Pamenepo mphotho yanu idzakhala yayikulu ndipo inu mudzakhala ana a Wammwambamwamba, chifukwa ndi wokoma mtima kwa anthu osayamika ndi oyipa.
36 Soyez donc miséricordieux, comme votre Père est miséricordieux.
Khalani achifundo, monga momwe Atate anu ali achifundo.”
37 Ne jugez point, et vous ne serez point jugés; ne condamnez point, et vous ne serez point condamnés; absolvez, et l'on vous absoudra;
“Musaweruze, ndipo inu simudzaweruzidwa. Musatsutse ndipo inu simudzatsutsidwa. Khululukirani ena ndipo mudzakhululukidwa.
38 donnez, et l’on vous donnera: on vous donnera dans votre robe une bonne mesure, serrée, secouée et débordante; car on se servira pour vous de la même mesure avec laquelle vous aurez mesuré.
Perekani ndipo mudzapatsidwa. Adzakupatsani mʼthumba mwanu muyeso wabwino, wotsenderezeka, wokhutchumuka ndi wosefukira. Pakuti muyeso umene mumagwiritsa ntchito, ndi omwewo adzakuyeserani.”
39 Il ajouta cette comparaison: «Un aveugle peut-il conduire un aveugle? Ne tomberont-ils pas tous deux dans une fosse?»
Iye anawawuzanso fanizo ili, “Kodi munthu wakhungu angatsogolere munthu wakhungu mnzake? Kodi onse sadzagwera mʼdzenje?
40 Le disciple n'est pas au-dessus de son maître: tout disciple sera traité comme son maître.
Wophunzira sangapose mphunzitsi wake, koma yense amene waphunzitsidwa bwinobwino adzakhala ngati mphunzitsi wake.
41 Pourquoi vois-tu la paille qui est dans l'oeil de ton frère, tandis que tu ne remarques pas la poutre qui est dans ton oeil?
“Kodi ndi chifukwa chiyani mumaona kachitsotso mʼdiso la mʼbale wanu ndi kusasamala mtengo uli mʼdiso mwanu?
42 Ou comment peux-tu dire à ton frère: «Frère, laisse-moi ôter la paille qui est dans ton oeil, » toi qui ne vois pas la poutre qui est dans le tien? Hypocrite, ôte premièrement la poutre de ton oeil, alors tu verras à ôter la paille qui est dans l'oeil de ton frère;
Kodi munganene bwanji kwa mʼbale wanu kuti, ‘Mʼbale nʼtakuchotsa kachitsotso mʼdiso mwako,’ pamene inu eni ake mukulephera kuona mtengo uli mʼdiso mwanu? Inu achiphamaso, yambani mwachotsa mtengo uli mʼdiso mwanu, ndipo kenaka mudzaona bwinobwino ndi kuchotsa kachitsotso mʼdiso la mʼbale wanu.”
43 car il n'y a pas de bon arbre qui produise de mauvais fruits, comme il n'y a pas de mauvais arbre qui produise de bons fruits:
Palibe mtengo wabwino umene umabala chipatso choyipa, kapena mtengo oyipa umene umabala chipatso chabwino.
44 chaque arbre se reconnaît à son fruit. On ne cueille pas des figues sur des épines et l'on ne vendange pas le raisin sur la ronce.
Mtengo uliwonse umadziwika ndi chipatso chake. Anthu sathyola nkhuyu pa mtengo waminga, kapena mphesa pa nthungwi.
45 L'homme de bien tire le bien du bon trésor de son coeur, et le méchant tire le mal de son mauvais trésor; car de l'abondance du coeur la bouche parle.
Munthu wabwino amatulutsa zinthu zabwino zosungidwa mu mtima mwake, koma munthu oyipa amatulutsa zinthu zoyipa zosungidwa mu mtima mwake. Pakamwa pake pamayankhula zimene zadzaza mu mtima mwake.
46 Pourquoi m'appelez-vous: «Seigneur, Seigneur, » et ne faites-vous pas ce que je dis?
“Kodi nʼchifukwa chiyani munditchula kuti, ‘Ambuye, Ambuye’ koma simuchita zimene Ine ndinena?
47 Je vous montrerai à qui ressemble tout homme qui vient à moi, qui écoute mes paroles et les met en pratique:
Ine ndidzakuonetsani mmene alili munthu amene amabwera kwa Ine ndi kumva mawu anga ndi kuwachita.
48 il est semblable à un homme qui bâtit une maison, et qui, ayant creusé profondément, en a posé les fondements sur le roc: une inondation étant survenue, le fleuve est venu donner contre cette maison, et n'a pu l'ébranler, parce qu'elle était bien bâtie.
Iye ali ngati munthu womanga nyumba, amene anakumba mozama nayika maziko ake pa mwala. Madzi osefukira atabwera ndi mphamvu, nawomba nyumbayo koma sinagwedezeka, chifukwa anayimanga bwino.
49 Mais celui qui écoute et ne pratique pas, est semblable à un homme qui a bâti une maison sur la terre, sans creuser de fondements: le fleuve est venu donner contre cette maison, et aussitôt elle s'est écroulée; et la ruine de cette maison a été grande.
Koma amene amamva mawu anga koma osawachita, akufanana ndi munthu amene anamanga nyumba yake koma yopanda maziko. Nthawi yomwe madziwo anawomba nyumbayo, inagwa ndipo inawonongekeratu.”

< Luc 6 >