< Sophonie 1 >

1 [C'est ici] la parole de l'Eternel qui fut [adressée] à Sophonie fils de Cusi, fils de Guédalia, fils d'Amaria, fils d'Ezéchias, du temps de Josias fils d'Amon Roi de Juda.
Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
2 Je ferai entièrement périr toutes choses de dessus cette terre, dit l'Eternel.
“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
3 Je ferai périr l'homme et le bétail; je consumerai les oiseaux des cieux, et les poissons de la mer; et les ruines [arriveront] aux méchants, et je retrancherai les hommes de dessus cette terre, dit l'Eternel.
“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
4 J'étendrai ma main sur Juda, et sur tous les habitants de Jérusalem; je retrancherai de ce lieu-ci le reste des Bahalins, et les noms des prêtres des faux dieux, et les sacrificateurs;
Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
5 Et ceux qui se prosternent sur les toits devant l'armée des cieux, et ceux qui se prosternent devant l'Eternel, jurent par lui, et qui jurent aussi par Malcam:
amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
6 Et ceux qui se détournent de l'Eternel, et ceux qui n'ont point cherché l'Eternel, qui ne l'ont point recherché.
amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
7 Tais-toi, à cause de la présence du Seigneur l'Eternel, car la journée de l'Eternel est proche; l'Eternel a préparé le sacrifice, il a invité ses conviés.
Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
8 Et il arrivera au jour du sacrifice de l'Eternel que je punirai les Seigneurs, et les enfants du Roi, et tous ceux qui s'habillent de vêtements étrangers.
Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
9 Et je punirai en ce jour-là tous ceux qui sautent par-dessus le seuil, [et] ceux qui remplissent de violence et de fraude la maison de leurs maîtres.
Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
10 Et en ce jour-là dit l'Eternel, il y aura de grands cris vers la porte des poissons, et des hurlements vers la seconde [ville], et une grande désolation vers les coteaux.
“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
11 Vous qui habitez dans Mactès, hurlez; car tous ceux qui trafiquaient ont été défaits, et tous ceux qui apportaient de l'argent, ont été retranchés.
Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
12 Et il arrivera en ce temps-là, que je fouillerai Jérusalem avec des lampes, que je punirai les hommes qui sont figés sur leurs lies, et qui disent en leurs cœurs; L'Eternel ne [nous] fera ni bien ni mal.
Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
13 Et leurs biens seront au pillage, et leurs maisons en désolation, et ils auront bâti des maisons, mais ils n'y habiteront point; et ils auront planté des vignes, mais ils n'en boiront pas le vin.
Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
14 La grande journée de l'Eternel est proche, elle est proche, et elle se hâte fort; la journée de l'Eternel n'est que bruit; celui qui est en amertume, crie de toute sa force; Là sont les hommes forts.
Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
15 Cette journée-là est une journée de fureur, une journée de détresse et d'angoisse, une journée de bruit éclatant et effrayant, une journée de ténèbres et d'obscurité, une journée de nuées et de brouillards;
Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
16 Une journée de cornet et d'alarme contre les villes munies, et contre les hautes tours.
Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
17 Je mettrai les hommes dans la détresse, et ils marcheront comme des aveugles, parce qu'ils ont péché contre l'Eternel; et leur sang sera répandu comme de la poussière, et leur chair comme de la fiente.
Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
18 Ni leur argent ni leur or ne les pourront point délivrer en la journée de la fureur de l'Eternel; et tout ce pays sera dévoré par le feu de sa jalousie; car il se hâtera de consumer tous les habitants de ce pays.
Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.

< Sophonie 1 >