< Zacharie 5 >

1 Puis je me retournai, et levai mes yeux pour regarder; et voici un rouleau volant.
Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
2 Alors il me dit: Que vois-tu? Et je répondis: Je vois un rouleau volant, dont la longueur est de vingt coudées, et sa largeur de dix coudées.
Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
3 Et il me dit: C'est là l'exécration du serment qui sort sur le dessus de toute la terre; car quiconque d'entre ce [peuple-ci] dérobe, sera puni comme elle; et quiconque d'entre ce [peuple]-ci jure, sera puni comme elle.
Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
4 Je déploierai cette exécration, dit l'Eternel des armées, et elle entrera dans la maison du larron, et dans la maison de celui qui jure [faussement] par mon Nom, et elle logera au milieu de leur maison, et la consumera avec son bois et ses pierres.
Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
5 Et l'Ange qui parlait avec moi sortit, et me dit: Lève maintenant tes yeux, et regarde ce qui sort.
Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
6 Et je dis: Qu'est-ce? Et il [répondit]: C'est un Epha qui sort dehors. Puis il dit: C'est l'œil que j'ai sur eux par toute la terre.
Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
7 Et voici, on portait une masse de plomb, et une femme était assise au milieu de l'Epha.
Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
8 Et il dit: C'est là la méchanceté; puis il la jeta au milieu de l'Epha, et mit la masse de plomb sur son ouverture.
Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
9 Puis levant mes yeux, je regardai, et voici deux femmes qui sortaient, et le vent soufflait dans leurs ailes; or elles avaient des ailes comme les ailes d'une cigogne; et elles enlevèrent l'Epha entre la terre et les cieux.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
10 Et je dis à l'Ange qui parlait avec moi: Où emportent-elles l'Epha?
Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
11 Et il me répondit: C'est pour lui bâtir une maison au pays de Sinhar laquelle étant établie, il sera là posé sur sa base.
Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”

< Zacharie 5 >